Yesaya 25
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nyimbo Yotamanda Yehova
25 Yehova ndinu Mulungu wanga;
ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,
pakuti mwachita zodabwitsa
zimene munakonzekeratu kalekale
mokhulupirika kwambiri.
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.
Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,
linga la anthu achilendo lero si mzindanso
ndipo sidzamangidwanso.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;
mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,
mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.
Mwakhala ngati pobisalirapo
pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.
Pakuti anthu ankhanza
ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.
Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.
Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,
inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera
anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.
Phwando la nyama yonona
ndi vinyo wabwino kwambiri.
7 Iye adzachotsa kulira
kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.
Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,
Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso
mwa munthu aliyense;
adzachotsa manyazi a anthu ake
pa dziko lonse lapansi,
Yehova wayankhula.
9 Tsiku limenelo iwo adzati,
“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;
ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.
Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;
tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;
ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,
ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,
ngati mmene amachitira munthu wosambira.
Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo
ngakhale luso la manja awo.
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali
ndipo adzawagwetsa
ndi kuwaponya pansi,
pa fumbi penipeni.
Isaiah 25
New International Version
Praise to the Lord
25 Lord, you are my God;(A)
I will exalt you and praise your name,(B)
for in perfect faithfulness(C)
you have done wonderful things,(D)
things planned(E) long ago.
2 You have made the city a heap of rubble,(F)
the fortified(G) town a ruin,(H)
the foreigners’ stronghold(I) a city no more;
it will never be rebuilt.(J)
3 Therefore strong peoples will honor you;(K)
cities of ruthless(L) nations will revere you.
4 You have been a refuge(M) for the poor,(N)
a refuge for the needy(O) in their distress,
a shelter from the storm(P)
and a shade from the heat.
For the breath of the ruthless(Q)
is like a storm driving against a wall
5 and like the heat of the desert.
You silence(R) the uproar of foreigners;(S)
as heat is reduced by the shadow of a cloud,
so the song of the ruthless(T) is stilled.
6 On this mountain(U) the Lord Almighty will prepare
a feast(V) of rich food for all peoples,
a banquet of aged wine—
the best of meats and the finest of wines.(W)
7 On this mountain he will destroy
the shroud(X) that enfolds all peoples,(Y)
the sheet that covers all nations;
8 he will swallow up death(Z) forever.
The Sovereign Lord will wipe away the tears(AA)
from all faces;
he will remove his people’s disgrace(AB)
from all the earth.
The Lord has spoken.(AC)
9 In that day(AD) they will say,
“Surely this is our God;(AE)
we trusted(AF) in him, and he saved(AG) us.
This is the Lord, we trusted in him;
let us rejoice(AH) and be glad in his salvation.”(AI)
10 The hand of the Lord will rest on this mountain;(AJ)
but Moab(AK) will be trampled in their land
as straw is trampled down in the manure.
11 They will stretch out their hands in it,
as swimmers stretch out their hands to swim.
God will bring down(AL) their pride(AM)
despite the cleverness[a] of their hands.
12 He will bring down your high fortified walls(AN)
and lay them low;(AO)
he will bring them down to the ground,
to the very dust.
Footnotes
- Isaiah 25:11 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.