Add parallel Print Page Options

Za Chilango cha Turo

23 Uthenga wonena za Turo:

Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi:
    pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa
    ndipo mulibe nyumba kapena dooko.
Zimenezi anazimva
    pochokera ku Kitimu.

Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja,
    inu amalonda a ku Sidoni,
    iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
Pa nyanja zazikulu
    panabwera tirigu wa ku Sihori;
zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda
    ndi anthu a mitundu ina.

Chita manyazi, iwe Sidimu
    pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti,
“Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana;
    sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
Mawuwa akadzamveka ku Igupto,
    iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.

Wolokerani ku Tarisisi,
    lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja,
    mzinda wakalekale,
umene anthu ake ankapita
    kukakhala ku mayiko akutali?
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina,
    mzinda umene amalonda ake ndi akalonga
ndi otchuka
    pa dziko lapansi?
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi
    kuti athetse kunyada kwawo
    ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.

10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo
    inu anthu a ku Tarisisi,
    pakuti mulibenso chokutetezani.
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja
    ndipo wagwedeza maufumu ake.
Iye walamula kuti Kanaani
    agwetse malinga ake.
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse,
    inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa!

“Ngakhale muwolokere ku Kitimu,
    kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 Onani dziko la Ababuloni,
    anthu amenewa tsopano atheratu!
Asiriya asandutsa Turo kukhala
    malo a zirombo za ku chipululu;
anamanga nsanja zawo za nkhondo,
    anagumula malinga ake
    ndipo anawasandutsa bwinja.

14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi;
    chifukwa malinga ako agwetsedwa!

15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:

16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda,
    iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika;
imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri,
    kuti anthu akukumbukire.”

17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi. 18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.

A Prophecy Against Tyre

23 A prophecy against Tyre:(A)

Wail,(B) you ships(C) of Tarshish!(D)
    For Tyre is destroyed(E)
    and left without house or harbor.
From the land of Cyprus
    word has come to them.

Be silent,(F) you people of the island
    and you merchants(G) of Sidon,(H)
    whom the seafarers have enriched.
On the great waters
    came the grain of the Shihor;(I)
the harvest of the Nile[a](J) was the revenue of Tyre,(K)
    and she became the marketplace of the nations.

Be ashamed, Sidon,(L) and you fortress of the sea,
    for the sea has spoken:
“I have neither been in labor nor given birth;(M)
    I have neither reared sons nor brought up daughters.”
When word comes to Egypt,
    they will be in anguish(N) at the report from Tyre.(O)

Cross over to Tarshish;(P)
    wail, you people of the island.
Is this your city of revelry,(Q)
    the old, old city,
whose feet have taken her
    to settle in far-off lands?
Who planned this against Tyre,
    the bestower of crowns,
whose merchants(R) are princes,
    whose traders(S) are renowned in the earth?
The Lord Almighty planned(T) it,
    to bring down(U) her pride in all her splendor
    and to humble(V) all who are renowned(W) on the earth.

10 Till[b] your land as they do along the Nile,
    Daughter Tarshish,
    for you no longer have a harbor.
11 The Lord has stretched out his hand(X) over the sea
    and made its kingdoms tremble.(Y)
He has given an order concerning Phoenicia
    that her fortresses be destroyed.(Z)
12 He said, “No more of your reveling,(AA)
    Virgin Daughter(AB) Sidon, now crushed!

“Up, cross over to Cyprus;(AC)
    even there you will find no rest.”
13 Look at the land of the Babylonians,[c](AD)
    this people that is now of no account!
The Assyrians(AE) have made it
    a place for desert creatures;(AF)
they raised up their siege towers,(AG)
    they stripped its fortresses bare
    and turned it into a ruin.(AH)

14 Wail, you ships(AI) of Tarshish;(AJ)
    your fortress is destroyed!(AK)

15 At that time Tyre(AL) will be forgotten for seventy years,(AM) the span of a king’s life. But at the end of these seventy years, it will happen to Tyre as in the song of the prostitute:

16 “Take up a harp, walk through the city,
    you forgotten prostitute;(AN)
play the harp well, sing many a song,
    so that you will be remembered.”

17 At the end of seventy years,(AO) the Lord will deal with Tyre. She will return to her lucrative prostitution(AP) and will ply her trade with all the kingdoms on the face of the earth.(AQ) 18 Yet her profit and her earnings will be set apart for the Lord;(AR) they will not be stored up or hoarded. Her profits will go to those who live before the Lord,(AS) for abundant food and fine clothes.(AT)

Footnotes

  1. Isaiah 23:3 Masoretic Text; Dead Sea Scrolls Sidon, / who cross over the sea; / your envoys are on the great waters. / The grain of the Shihor, / the harvest of the Nile,
  2. Isaiah 23:10 Dead Sea Scrolls and some Septuagint manuscripts; Masoretic Text Go through
  3. Isaiah 23:13 Or Chaldeans