Yesaya 18
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Za Kulangidwa kwa Kusi
18 Tsoka kwa anthu a ku Kusi.
Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo,
mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi,
ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro,
kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala,
ndi woopedwa ndi anthu.
Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena.
Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Inu nonse anthu a pa dziko lonse,
inu amene mumakhala pa dziko lapansi,
pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri
yangʼanani,
ndipo pamene lipenga lilira
mumvere.
4 Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti,
“Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana,
monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha,
monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka
ndiponso mphesa zitayamba kupsa,
Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira,
ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama
ndiponso zirombo zakuthengo;
mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe,
ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse,
zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala,
kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe,
mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo,
anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.
Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.
Isaiah 18
New International Version
A Prophecy Against Cush
18 Woe(A) to the land of whirring wings[a]
along the rivers of Cush,[b](B)
2 which sends envoys(C) by sea
in papyrus(D) boats over the water.
Go, swift messengers,
to a people tall and smooth-skinned,(E)
to a people feared far and wide,
an aggressive(F) nation of strange speech,
whose land is divided by rivers.(G)
3 All you people of the world,(H)
you who live on the earth,
when a banner(I) is raised on the mountains,
you will see it,
and when a trumpet(J) sounds,
you will hear it.
4 This is what the Lord says to me:
“I will remain quiet(K) and will look on from my dwelling place,(L)
like shimmering heat in the sunshine,(M)
like a cloud of dew(N) in the heat of harvest.”
5 For, before the harvest, when the blossom is gone
and the flower becomes a ripening grape,
he will cut off(O) the shoots with pruning knives,
and cut down and take away the spreading branches.(P)
6 They will all be left to the mountain birds of prey(Q)
and to the wild animals;(R)
the birds will feed on them all summer,
the wild animals all winter.
7 At that time gifts(S) will be brought to the Lord Almighty
from a people tall and smooth-skinned,(T)
from a people feared(U) far and wide,
an aggressive nation of strange speech,
whose land is divided by rivers(V)—
the gifts will be brought to Mount Zion, the place of the Name of the Lord Almighty.(W)
Footnotes
- Isaiah 18:1 Or of locusts
- Isaiah 18:1 That is, the upper Nile region
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.