Yeremiya 52
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kuwonongeka kwa Yerusalemu
52 Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina. 2 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu. 3 Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake.
Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
4 Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo. 5 Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
6 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya. 7 Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba, 8 koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
9 Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake. 10 Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda. 11 Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
12 Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu. 13 Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse. 14 Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu. 15 Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 16 Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
17 Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni. 18 Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova. 19 Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
20 Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka. 21 Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi. 22 Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija. 23 Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
24 Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata. 25 Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo. 26 Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula. 27 Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe.
Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo. 28 Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi:
Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
29 mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara,
anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
30 mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara,
Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo.
Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
Kumasulidwa kwa Yehoyakini
31 Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo. 32 Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni. 33 Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse. 34 Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.
Jeremiah 52
New International Version
The Fall of Jerusalem(A)(B)(C)
52 Zedekiah(D) was twenty-one years old when he became king, and he reigned in Jerusalem eleven years. His mother’s name was Hamutal daughter of Jeremiah; she was from Libnah.(E) 2 He did evil in the eyes of the Lord, just as Jehoiakim(F) had done. 3 It was because of the Lord’s anger that all this happened to Jerusalem and Judah,(G) and in the end he thrust them from his presence.(H)
Now Zedekiah rebelled(I) against the king of Babylon.
4 So in the ninth year of Zedekiah’s reign, on the tenth(J) day of the tenth month, Nebuchadnezzar king of Babylon marched against Jerusalem(K) with his whole army. They encamped outside the city and built siege works(L) all around it.(M) 5 The city was kept under siege until the eleventh year of King Zedekiah.
6 By the ninth day of the fourth month the famine in the city had become so severe that there was no food for the people to eat.(N) 7 Then the city wall was broken through, and the whole army fled.(O) They left the city at night through the gate between the two walls near the king’s garden, though the Babylonians[a] were surrounding the city. They fled toward the Arabah,[b] 8 but the Babylonian[c] army pursued King Zedekiah and overtook him in the plains of Jericho. All his soldiers were separated from him and scattered, 9 and he was captured.(P)
He was taken to the king of Babylon at Riblah(Q) in the land of Hamath,(R) where he pronounced sentence on him. 10 There at Riblah the king of Babylon killed the sons(S) of Zedekiah before his eyes; he also killed all the officials of Judah. 11 Then he put out Zedekiah’s eyes, bound him with bronze shackles and took him to Babylon, where he put him in prison till the day of his death.(T)
12 On the tenth day of the fifth(U) month, in the nineteenth year of Nebuchadnezzar king of Babylon, Nebuzaradan(V) commander of the imperial guard, who served the king of Babylon, came to Jerusalem. 13 He set fire(W) to the temple(X) of the Lord, the royal palace and all the houses(Y) of Jerusalem. Every important building he burned down. 14 The whole Babylonian army, under the commander of the imperial guard, broke down all the walls(Z) around Jerusalem. 15 Nebuzaradan the commander of the guard carried into exile(AA) some of the poorest people and those who remained in the city, along with the rest of the craftsmen[d] and those who had deserted(AB) to the king of Babylon. 16 But Nebuzaradan left behind(AC) the rest of the poorest people of the land to work the vineyards and fields.
17 The Babylonians broke up the bronze pillars,(AD) the movable stands(AE) and the bronze Sea(AF) that were at the temple of the Lord and they carried all the bronze to Babylon.(AG) 18 They also took away the pots, shovels, wick trimmers, sprinkling bowls,(AH) dishes and all the bronze articles used in the temple service.(AI) 19 The commander of the imperial guard took away the basins, censers,(AJ) sprinkling bowls, pots, lampstands,(AK) dishes(AL) and bowls used for drink offerings(AM)—all that were made of pure gold or silver.(AN)
20 The bronze from the two pillars, the Sea and the twelve bronze bulls(AO) under it, and the movable stands, which King Solomon had made for the temple of the Lord, was more than could be weighed.(AP) 21 Each pillar was eighteen cubits high and twelve cubits in circumference[e]; each was four fingers thick, and hollow.(AQ) 22 The bronze capital(AR) on top of one pillar was five cubits[f] high and was decorated with a network and pomegranates(AS) of bronze all around. The other pillar, with its pomegranates, was similar. 23 There were ninety-six pomegranates on the sides; the total number of pomegranates(AT) above the surrounding network was a hundred.(AU)
24 The commander of the guard took as prisoners Seraiah(AV) the chief priest, Zephaniah(AW) the priest next in rank and the three doorkeepers.(AX) 25 Of those still in the city, he took the officer in charge of the fighting men, and seven royal advisers. He also took the secretary(AY) who was chief officer in charge of conscripting the people of the land, sixty of whom were found in the city. 26 Nebuzaradan(AZ) the commander took them all and brought them to the king of Babylon at Riblah. 27 There at Riblah,(BA) in the land of Hamath, the king had them executed.
So Judah went into captivity, away(BB) from her land. 28 This is the number of the people Nebuchadnezzar carried into exile:(BC)
in the seventh year, 3,023 Jews;
29 in Nebuchadnezzar’s eighteenth year,
832 people from Jerusalem;
30 in his twenty-third year,
745 Jews taken into exile(BD) by Nebuzaradan the commander of the imperial guard.
There were 4,600 people in all.(BE)
Jehoiachin Released(BF)
31 In the thirty-seventh year of the exile of Jehoiachin(BG) king of Judah, in the year Awel-Marduk became king of Babylon, on the twenty-fifth day of the twelfth month, he released Jehoiachin king of Judah and freed him from prison. 32 He spoke kindly to him and gave him a seat of honor higher than those of the other kings who were with him in Babylon. 33 So Jehoiachin put aside his prison clothes and for the rest of his life ate regularly at the king’s table.(BH) 34 Day by day the king of Babylon gave Jehoiachin a regular allowance(BI) as long as he lived, till the day of his death.
Footnotes
- Jeremiah 52:7 Or Chaldeans; also in verse 17
- Jeremiah 52:7 Or the Jordan Valley
- Jeremiah 52:8 Or Chaldean; also in verse 14
- Jeremiah 52:15 Or the populace
- Jeremiah 52:21 That is, about 27 feet high and 18 feet in circumference or about 8.1 meters high and 5.4 meters in circumference
- Jeremiah 52:22 That is, about 7 1/2 feet or about 2.3 meters
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.