Add parallel Print Page Options

Uthenga Wonena za Aamoni

49 Yehova ananena izi:

Amoni,

“Kodi Israeli alibe ana aamuna?
    Kapena alibe mlowamʼmalo?
Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi?
    Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Koma nthawi ikubwera,”
    akutero Yehova,
“pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo
    ku Raba, likulu la Amoni;
ndipo malo awo opembedzera milungu yawo
    adzatenthedwa ndi moto.
Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo
    kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,”
            akutero Yehova.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika!
    Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba!
Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu;
    thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga,
chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo,
    pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Chifukwa chiyani mukunyadira
    chigwa chanu,
inu anthu osakhulupirika
    amene munadalira chuma chanu nʼkumati:
    ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe
    zochokera kwa onse amene akuzungulira,”
            akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse.
“Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake.
    Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.

“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,”
            akutero Yehova.

Uthenga Wonena za Edomu

Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu:

“Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani?
    Kodi anzeru analeka kupereka uphungu?
    Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Inu anthu a ku Dedani, thawani,
    bwererani ndi kukabisala ku makwalala
chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau
    popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu
    akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Anthu akuba akanafika usiku
    akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau.
    Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo,
    kotero kuti sadzathanso kubisala.
Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka.
    Palibe wonena kuti,
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza.
    Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’ ”

12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho. 13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”

14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova:
    Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti,
“Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu!
    Konzekerani nkhondo!”

15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina.
    Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga;
    kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
iwe amene umakhala mʼmapanga
    a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri.
Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,
    ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
            akutero Yehova.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha.
    Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo
    chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora,
    pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,”
            akutero Yehova,
“motero palibe munthu
    amene adzakhala mu Edomu.

19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani
    kupita ku malo a msipu wobiriwira,
Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo.
    Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine.
Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani?
    Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova
    ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani.
Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo
    ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera;
    kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka
    nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu
    idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

Uthenga Wonena za Damasiko

23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa:

“Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha
    chifukwa amva nkhani yoyipa.
Mitima yawo yagwidwa ndi mantha
    ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka.
    Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa
    chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu.
Ali ndi nkhawa komanso mantha
    ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Mzinda wotchuka
    ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa;
    ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,”
            akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko;
    moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”

Uthenga Wonena za Kedara ndi Hazori

28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa:

“Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara.
    Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo,
    ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo.
    Mutengenso ngamira zawo.
Anthu adzafuwula kwa iwo kuti,
    ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’

30 “Thawani mofulumira!
    Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,”
            akutero Yehova.
“Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu;
    wakonzekera zoti alimbane nanu.

31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere,
    umene ukukhala mosatekeseka,”
            akutero Yehova,
“mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo;
    anthu ake amakhala pa okha.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa,
    ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa.
Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali.
    Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,”
            akutero Yehova.
33 “Hazori adzasanduka bwinja,
    malo okhalamo nkhandwe
mpaka muyaya.
    Palibe munthu amene adzayendemo.”

Uthenga Wonena za Elamu

34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:

35 Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu,
    umene uli chida chawo champhamvu.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu
    kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga;
ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi,
    ndipo sipadzakhala dziko
    limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo
    komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo.
Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga
    ndipo adzakhala pa mavuto,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawapirikitsa ndi lupanga
    mpaka nditawatheratu.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu
    ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,”
            akutero Yehova.

39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera
    anthu a ku Elamu dziko lawo,”
            akutero Yehova.

49 DE los hijos de Ammón. Así ha dicho Jehová: ¿No tiene hijos Israel? ¿No tiene heredero? ¿Por qué tomó como por heredad el rey de ellos á Gad, y su pueblo habitó en sus ciudades?

Por tanto, he aquí vienen días, ha dicho Jehová, en que haré oir en Rabba de los hijos de Ammón clamor de guerra; y será puesta en montón de asolamiento, y sus ciudades serán puestas á fuego, é Israel tomará por heredad á los que los tomaron á ellos, ha dicho Jehová.

Aulla, oh Hesbón, porque destruída es Hai; clamad, hijas de Rabba, vestíos de sacos, endechad, y rodead por los vallados, porque el rey de ellos fué en cautiverio, sus sacerdotes y sus príncipes juntamente.

¿Por qué te glorías de los valles? Tu valle se deshizo, oh hija contumaz, la que confía en sus tesoros, la que dice: ¿Quién vendrá contra mí?

He aquí yo traigo sobre ti espanto, dice el Señor Jehová de los ejércitos, de todos tus alrededores; y seréis lanzados cada uno en derechura de su rostro, y no habrá quien recoja al errante.

Y después de esto haré tornar la cautividad de los hijos de Ammón, dice Jehová.

De Edom. Así ha dicho Jehová de los ejércitos: ¿No hay más sabiduría en Temán? ¿ha perecido el consejo en los sabios? ¿corrompióse su sabiduría?

Huid, volveos, escondeos en simas para estar, oh moradores de Dedán; porque el quebrantamiento de Esaú traeré sobre él, al tiempo que lo tengo de visitar.

Si vendimiadores vinieran contra ti, ¿no dejarán rebuscos? Si ladrones de noche, tomarán lo que hubieren menester.

10 Mas yo desnudaré á Esaú, descubriré sus escondrijos, y no podrá esconderse: será destruída su simiente, y sus hermanos, y sus vecinos; y no será.

11 Deja tus huérfanos, yo los criaré; y en mí se confiarán tus viudas.

12 Porque así ha dicho Jehová: He aquí que los que no estaban condenados á beber del cáliz, beberán ciertamente; ¿y serás tú absuelto del todo? No serás absuelto, sino que de cierto beberás.

13 Porque por mí he jurado, dice Jehová, que en asolamiento, en oprobio, en soledad, y en maldición, será Bosra; y todas su ciudades serán en asolamientos perpetuos.

14 La fama oí, que de Jehová había sido enviado mensajero á las gentes, diciendo: Juntaos, y venid contra ella, y levantaos á la batalla.

15 Porque he aquí que pequeño te he puesto entre las gentes, menospreciado entre los hombres.

16 Tu arrogancia te engañó, y la soberbia de tu corazón, tú que habitas en cavernas de peñas, que tienes la altura del monte: aunque alces como águila tu nido, de allí te haré descender, dice Jehová.

17 Y será Edom en asolamiento: todo aquel que pasare por ella se espantará, y silbará sobre todas sus plagas.

18 Como el trastornamiento de Sodoma y de Gomorra, y de sus ciudades vecinas, dice Jehová, no morará allí nadie, ni la habitará hijo de hombre.

19 He aquí que como león subirá de la hinchazón del Jordán contra la bella y robusta; porque muy pronto harélo correr de sobre ella, y al que fuere escogido la encargaré; porque ¿quién es semejante á mí? ¿y quién me emplazará? ¿y quién será aquel pastor que me podrá resistir?

20 Por tanto, oíd el consejo de Jehová, que ha acordado sobre Edom; y sus pensamientos, que ha resuelto sobre los moradores de Temán. Ciertamente los más pequeños del hato los arrastrarán, y destruirán sus moradas con ellos.

21 Del estruendo de la caída de ellos la tierra tembló, y el grito de su voz se oyó en el mar Bermejo.

22 He aquí que como águila subirá y volará, y extenderá sus alas sobre Bosra: y el corazón de los valientes de Edom será en aquel día como el corazón de mujer en angustias.

23 Acerca de Damasco. Confundióse Hamath, y Arphad, porque oyeron malas nuevas: derritiéronse en aguas de desmayo, no pueden sosegarse.

24 Desmayóse Damasco, volvióse para huir, y tomóle temblor: angustia y dolores le tomaron, como de mujer que está de parto.

25 Cómo dejaron á la ciudad de alabanza, ciudad de mi gozo!

26 Por tanto, sus mancebos caerán en sus plazas, y todos los hombres de guerra morirán en aquel día, ha dicho Jehová de los ejércitos.

27 Y haré encender fuego en el muro de Damasco, y consumirá las casas de Ben-hadad.

28 De Cedar y de los reinos de Hasor, los cuales hirió Nabucodonosor rey de Babilonia. Así ha dicho Jehová: Levantaos, subid contra Cedar, y destruid los hijos de oriente.

29 Sus tiendas y su ganados tomarán: sus cortinas, y todos sus vasos, y sus camellos, tomarán para sí; y llamarán contra ellos miedo alrededor.

30 Huid, trasponeos muy lejos, meteos en simas para estar, oh moradores de Hasor, dice Jehová; porque tomó consejo contra vosotros Nabucodonosor rey de Babilonia, y contra vosotros ha formado designio.

31 Levantaos, subid á gente pacífica, que vive confiadamente, dice Jehová, que ni tienen puertas ni cerrojos, que viven solitarios.

32 Y serán sus camellos por presa, y la multitud de sus ganados por despojo; y esparcirélos por todos vientos, echados hasta el postrer rincón; y de todos sus lados les traeré su ruina, dice Jehová.

33 Y Hasor será morada de chacales, soledad para siempre: ninguno morará allí, ni la habitará hijo de hombre.

34 Palabra de Jehová que fué á Jeremías profeta acerca de Elam, en el principio del reinado de Sedechîas rey de Judá, diciendo:

35 Así ha dicho Jehová de los ejércitos: He aquí que yo quiebro el arco de Elam, principio de su fortaleza.

36 Y traeré sobre Elam los cuatro vientos de los cuatro puntos del cielo, y aventarélos á todos estos vientos; ni habrá gente adonde no vengan extranjeros de Elam.

37 Y haré que Elam se intimide delante de sus enemigos, y delante de los que buscan su alma; y traeré sobre ellos mal, y el furor de mi enojo, dice Jehová; y enviaré en pos de ellos espada hasta que los acabe.

38 Y pondré mi silla en Elam, y destruiré de allí rey y príncipe, dice Jehová.

39 Mas acontecerá en lo postrero de los días, que haré tornar la cautividad de Elam, dice Jehová.