Add parallel Print Page Options

Uthenga Wonena za Afilisti

47 Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:

Yehova akuti,

“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;
    adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.
Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,
    mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.
Anthu adzafuwula;
    anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,
    phokoso la magaleta ake
    ndi kulira kwa mikombero yake.
Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;
    manja awo adzangoti khoba.
Pakuti tsiku lafika
    lowononga Afilisti onse
ndi kupha onse otsala,
    onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.
Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,
    otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
Anthu a ku Gaza ameta mipala;
    anthu a ku Asikeloni akhala chete.
Inu otsala a ku chigwa,
    mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?

“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,
    kodi udzapumula liti?
Bwerera mʼmalo ako;
    ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
Koma lupangalo lidzapumula bwanji
    pamene Yehova walilamulira
kuti lithire nkhondo
    Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”