Add parallel Print Page Options
'耶 利 米 書 1 ' not found for the version: Chinese New Testament: Easy-to-Read Version.

Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini. Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda. Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.

Kuyitanidwa kwa Yeremiya

Yehova anayankhula nane kuti,

“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale,
    iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale;
    ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”

Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”

Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira. Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako. 10 Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”

11 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”

12 Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”

13 Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”

14 Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto. 15 Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova.

“Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu
    polowera pa zipata za Yerusalemu;
iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake
    ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo
    chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine.
Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina,
    ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.

17 “Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona. 18 Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo. 19 Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

The words of Jeremiah,(A) the son of Hilkiah, one of the priests living in Anathoth(B) in the territory of Benjamin. The word of the Lord came to him in the thirteenth year of the reign of Josiah(C) son of Amon, king of Judah. It also came throughout the days of Jehoiakim(D) son of Josiah, king of Judah, until the fifth month of the eleventh year of Zedekiah(E) son of Josiah, king of Judah, when the people of Jerusalem went into exile.

The Call of Jeremiah

The word of the Lord came to me:

I chose you before I formed you in the womb;
I set you apart before you were born.(F)
I appointed you a prophet to the nations.(G)

But I protested, “Oh no, Lord, God! Look, I don’t know how to speak(H) since I am only a youth.”(I)

Then the Lord said to me:

Do not say, “I am only a youth,”(J)
for you will go to everyone I send you to
and speak whatever I tell you.(K)
Do not be afraid of anyone,(L)
for I will be with you to deliver you.(M)
This is the Lord’s declaration.

Then the Lord reached out His hand, touched my mouth,(N) and told me:

I have now filled your mouth with My words.(O)
10 See, I have appointed you today
over nations and kingdoms
to uproot and tear down,
to destroy and demolish,(P)
to build and plant.(Q)

Two Visions

11 Then the word of the Lord came to me, asking, “What do you see, Jeremiah?”(R)

I replied, “I see a branch of an almond tree.”

12 The Lord said to me, “You have seen correctly, for I watch over My word to accomplish it.”(S) 13 Again the word of the Lord came to me inquiring, “What do you see?”

And I replied, “I see a boiling pot,(T) its lip tilted from the north to the south.”

14 Then the Lord said to me, “Disaster will be poured out[a] from the north(U) on all who live in the land. 15 Indeed, I am about to summon all the clans and kingdoms of the north.”(V)

This is the Lord’s declaration.

They will come, and each king will set up his throne
at the entrance to Jerusalem’s gates.
They will attack all her surrounding walls
and all the other cities of Judah.

16 “I will pronounce My judgments against them for all the evil they did when they abandoned Me to burn incense to other gods and to worship the works of their own hands.(W)

17 “Now, get ready. Stand up and tell them everything that I command you. Do not be intimidated by them(X) or I will cause you to cower before them. 18 Today, I am the One who has made you a fortified city,(Y) an iron pillar, and bronze walls(Z) against the whole land—against the kings of Judah, its officials, its priests, and the population. 19 They will fight against you but never prevail over you,(AA) since I am with you to rescue you.”(AB)

This is the Lord’s declaration.

Footnotes

  1. Jeremiah 1:14 LXX reads will boil