Add parallel Print Page Options

Lamba Womanga Mʼchiwuno

13 Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.” Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.

Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti, “Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.” Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.

Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.” Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.

Pamenepo Yehova anandiwuza kuti, “Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 10 Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu. 11 Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.

Zikopa Zothiramo Vinyo

12 “Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’ 13 Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu. 14 Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’ ”

Yuda Adzapita ku Ukapolo

15 Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu,
    musadzitukumule,
    pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.
16 Lemekezani Yehova Mulungu wanu
    asanagwetse mdima,
mapazi anu asanayambe kupunthwa
    mʼchisisira chamʼmapiri.
Asanasandutse kuwala
    mukuyembekezerako kukhala
    mdima wandiweyani.
17 Koma ngati simumvera,
    ndidzalira kwambiri
    chifukwa cha kunyada kwanu.
Mʼmaso mwanga
    mwadzaza ndi misozi yowawa
    chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.

18 Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti,
    “Tsikani pa mipando yaufumuyo,
pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo
    zagwa pansi.”
19 Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa
    ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula.
Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo,
    watengedwa yense ukapolo.

20 Tukula maso ako kuti uwone
    amene akubwera kuchokera kumpoto.
Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti,
    nkhosa zanu zokongola zija?
21 Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira
    anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira?
Kodi sudzamva zowawa
    ngati za mayi pa nthawi yake yochira?
22 Ndipo ngati udzadzifunsa kuti,
    “Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?”
Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri
    kuti zovala zanu zingʼambike
    ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.
23 Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake,
    kapena kambuku kusintha mawanga ake?
Inunso amene munazolowera kuchita
    zoyipa simungathe kusintha.

24 “Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu
    amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.
25 Limeneli ndiye gawo lanu,
    chilango chimene ndakukonzerani
chifukwa chondiyiwala Ine
    ndi kutumikira milungu yabodza,
            akutero Yehova.
26 Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso
    kuti umaliseche wanu uwonekere.
27 Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu
    ndi ziwerewere zanu,
zochitika pa mapiri ndi mʼminda.
    Tsoka iwe Yerusalemu!
Udzakhala wosayeretsedwa
    pa zachipembedzo mpaka liti?”

A Linen Belt

13 This is what the Lord said to me: “Go and buy a linen belt and put it around your waist, but do not let it touch water.” So I bought a belt, as the Lord directed, and put it around my waist.

Then the word of the Lord came to me a second time:(A) “Take the belt you bought and are wearing around your waist, and go now to Perath[a](B) and hide it there in a crevice in the rocks.” So I went and hid it at Perath, as the Lord told me.(C)

Many days later the Lord said to me, “Go now to Perath and get the belt I told you to hide there.” So I went to Perath and dug up the belt and took it from the place where I had hidden it, but now it was ruined and completely useless.

Then the word of the Lord came to me: “This is what the Lord says: ‘In the same way I will ruin the pride of Judah and the great pride(D) of Jerusalem. 10 These wicked people, who refuse to listen(E) to my words, who follow the stubbornness of their hearts(F) and go after other gods(G) to serve and worship them,(H) will be like this belt—completely useless!(I) 11 For as a belt is bound around the waist, so I bound all the people of Israel and all the people of Judah to me,’ declares the Lord, ‘to be my people for my renown(J) and praise and honor.(K) But they have not listened.’(L)

Wineskins

12 “Say to them: ‘This is what the Lord, the God of Israel, says: Every wineskin should be filled with wine.’ And if they say to you, ‘Don’t we know that every wineskin should be filled with wine?’ 13 then tell them, ‘This is what the Lord says: I am going to fill with drunkenness(M) all who live in this land, including the kings who sit on David’s throne, the priests, the prophets and all those living in Jerusalem. 14 I will smash them one against the other, parents and children alike, declares the Lord. I will allow no pity(N) or mercy or compassion(O) to keep me from destroying(P) them.’”

Threat of Captivity

15 Hear and pay attention,
    do not be arrogant,
    for the Lord has spoken.(Q)
16 Give glory(R) to the Lord your God
    before he brings the darkness,
before your feet stumble(S)
    on the darkening hills.
You hope for light,
    but he will turn it to utter darkness
    and change it to deep gloom.(T)
17 If you do not listen,(U)
    I will weep in secret
    because of your pride;
my eyes will weep bitterly,
    overflowing with tears,(V)
    because the Lord’s flock(W) will be taken captive.(X)

18 Say to the king(Y) and to the queen mother,(Z)
    “Come down from your thrones,
for your glorious crowns(AA)
    will fall from your heads.”
19 The cities in the Negev will be shut up,
    and there will be no one to open them.
All Judah(AB) will be carried into exile,
    carried completely away.

20 Look up and see
    those who are coming from the north.(AC)
Where is the flock(AD) that was entrusted to you,
    the sheep of which you boasted?
21 What will you say when the Lord sets over you
    those you cultivated as your special allies?(AE)
Will not pain grip you
    like that of a woman in labor?(AF)
22 And if you ask yourself,
    “Why has this happened to me?”(AG)
it is because of your many sins(AH)
    that your skirts have been torn off(AI)
    and your body mistreated.(AJ)
23 Can an Ethiopian[b] change his skin
    or a leopard its spots?
Neither can you do good
    who are accustomed to doing evil.(AK)

24 “I will scatter you like chaff(AL)
    driven by the desert wind.(AM)
25 This is your lot,
    the portion(AN) I have decreed for you,”
declares the Lord,
“because you have forgotten(AO) me
    and trusted in false gods.(AP)
26 I will pull up your skirts over your face
    that your shame may be seen(AQ)
27 your adulteries and lustful neighings,
    your shameless prostitution!(AR)
I have seen your detestable acts
    on the hills and in the fields.(AS)
Woe to you, Jerusalem!
    How long will you be unclean?”(AT)

Footnotes

  1. Jeremiah 13:4 Or possibly to the Euphrates; similarly in verses 5-7
  2. Jeremiah 13:23 Hebrew Cushite (probably a person from the upper Nile region)