Add parallel Print Page Options

Za Lilime

Abale anga, ambiri musakhale aphunzitsi chifukwa mumadziwa kuti aphunzitsife tidzaweruzidwa mowuma kuposa anthu ena onse. Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.

Tikayika tizitsulo mʼkamwa mwa akavalo kuti atimvere, timatha kuwongolera thupi lake lonse. Taonani sitima zapamadzi. Ngakhale ndi zazikulu kwambiri ndipo zimakankhidwa ndi mphepo yamphamvu, zimawongoleredwa ndi tsigiro lalingʼono kulikonse kumene woyendetsayo akufuna kupita. Momwemonso, lilime ndi kachiwalo kakangʼono ka thupi koma limadzitama kuti nʼkuchita zikuluzikulu. Tangoganizirani za nkhalango yayikulu imene ingapse ndi kalawi kamoto koyamba mochepa. Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena.

Mitundu yonse ya nyama, ya mbalame, ya zokwawa ndi ya zolengedwa za mʼnyanja, zikuwetedwa ndipo munthu wakhala akuziweta, koma palibe munthu amene angaweta lilime. Lilime ndipo silitha kupuma, ndi lodzaza ndi ululu wakupha.

Ndi lilime lomwelo timatamanda Ambuye ndi Atate athu, komanso ndi lilime lomwelo timalalatira anthu, amene anapangidwa mʼchifanizo cha Mulungu. 10 Mʼkamwa momwemo mutuluka matamando ndi kulalata. Abale anga, zisamatero ayi. 11 Kodi madzi abwino ndi a mchere angatuluke pa kasupe mmodzi? 12 Abale anga, kodi mtengo wa mkuyu nʼkubala mphesa, kapena mtengo wampesa nʼkubala nkhuyu? Kasupe wa madzi a mchere sangatulutsenso madzi abwino.

Mitundu Iwiri ya Nzeru

13 Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake 14 Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi. 15 “Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda. 16 Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.

17 Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima. 18 Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.

Taming the Tongue

Not many of you should become teachers,(A) my fellow believers, because you know that we who teach will be judged(B) more strictly.(C) We all stumble(D) in many ways. Anyone who is never at fault in what they say(E) is perfect,(F) able to keep their whole body in check.(G)

When we put bits into the mouths of horses to make them obey us, we can turn the whole animal.(H) Or take ships as an example. Although they are so large and are driven by strong winds, they are steered by a very small rudder wherever the pilot wants to go. Likewise, the tongue is a small part of the body, but it makes great boasts.(I) Consider what a great forest is set on fire by a small spark. The tongue also is a fire,(J) a world of evil among the parts of the body. It corrupts the whole body,(K) sets the whole course of one’s life on fire, and is itself set on fire by hell.(L)

All kinds of animals, birds, reptiles and sea creatures are being tamed and have been tamed by mankind, but no human being can tame the tongue. It is a restless evil, full of deadly poison.(M)

With the tongue we praise our Lord and Father, and with it we curse human beings, who have been made in God’s likeness.(N) 10 Out of the same mouth come praise and cursing. My brothers and sisters, this should not be. 11 Can both fresh water and salt water flow from the same spring? 12 My brothers and sisters, can a fig tree bear olives, or a grapevine bear figs?(O) Neither can a salt spring produce fresh water.

Two Kinds of Wisdom

13 Who is wise and understanding among you? Let them show it(P) by their good life, by deeds(Q) done in the humility that comes from wisdom. 14 But if you harbor bitter envy and selfish ambition(R) in your hearts, do not boast about it or deny the truth.(S) 15 Such “wisdom” does not come down from heaven(T) but is earthly, unspiritual, demonic.(U) 16 For where you have envy and selfish ambition,(V) there you find disorder and every evil practice.

17 But the wisdom that comes from heaven(W) is first of all pure; then peace-loving,(X) considerate, submissive, full of mercy(Y) and good fruit, impartial and sincere.(Z) 18 Peacemakers(AA) who sow in peace reap a harvest of righteousness.(AB)