Add parallel Print Page Options

Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.

Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse:

Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Ntchito ya Tito ku Krete

Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira. Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera. Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo. Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo. Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.

Kudzudzula Olephera Kuchita Bwino

10 Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo. 11 Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo. 12 Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.” 13 Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona, 14 kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi. 15 Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa. 16 Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

Paul says ‘Hello’ to Titus

This letter is from me, Paul. I am God's servant and an apostle of Jesus Christ. God has sent me to help the people that he has chosen. I teach them to understand his true message and to trust him. As a result they will live in a way that pleases God. They will also be sure that they will live with God for ever. Before the world began, God promised that his people would have life with him. And God never tells lies. God is the one who saves us. Now, at the proper time, he has made his message clear. He has given his message to me so that I can tell it to people. That is what he has told me to do.

I am writing to you, Titus. I told you the message about Jesus and now we both believe in him. So you are like my own child.

I pray that God, the Father, and Christ Jesus, our Saviour, will continue to help you. I pray that they will give you peace in your mind.

Titus's work in Crete

I left you in Crete so that you could finish certain things. You should make right some things that were wrong. And you should choose leaders of the believers in every town, as I told you.

This is what a leader in the church must be like. Nobody should have a reason to say that he has done something wrong. He must be the husband of only one wife. He must have children who respect him. Nobody should say that they enjoy bad things or that they do not obey their parents.[a] A leader in the church serves the believers on God's behalf. Because of that, nobody should have a reason to say that the leader has done anything wrong. A leader must not be proud. He must not become angry easily. He should not like to drink too much wine. He must not be someone who likes to fight. He must not want to get a lot of money for himself. Instead, he must be happy to have visitors in his home. He must want to do good things. He must be careful in how he lives. He must do what is right. He must want to serve God well. He must control himself well.

A leader in the church must continue to believe the true message very well. That is the message which we have taught. Then he will be able to teach people what is true and right. He will also show that people who speak against the true message are wrong.

10 I say this because there are many people who refuse to obey their leaders. They speak about useless things and they deceive people. Many of them want the believers to obey all the Jewish rules.[b] 11 You must stop those people from teaching false things like that. They are causing whole families to believe their lies. They teach things that they should not teach. They deceive people because they want people to give them money. 12 Many years ago, there was a certain man who lived on Crete. The people there called him their prophet. Even he said, ‘People who live on Crete are always telling lies and doing wicked things. They are lazy and they eat too much food.’

13 What that man said is true. So you must warn the people there. Help them to believe the true message about Jesus more and more. 14 They must not listen to Jewish stories that are not true, or to human rules. Those things are the ideas of people who refuse to obey God's true message.

15 If someone is clean and good inside, everything is clean and good for them to enjoy. But if someone is not a believer and has an unclean mind, nothing is clean or good for that person. Their minds no longer think properly. They no longer feel guilty when they do something wrong. 16 People like that say that they know God. But they do disgusting things. This shows that they do not know him. They are completely bad. They refuse to obey God. They are not able to do anything good.

Footnotes

  1. 1:6 ‘children who respect him’ or: ‘children who are believers’.
  2. 1:10 Some Jewish Christians taught that the Christians must obey the Jews' rules. This group may have told everyone to be circumcised.