Aroma 11
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Aisraeli Otsala
11 Ine ndikufunsa kuti kodi Mulungu anakana anthu ake? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Inenso ndine Mwisraeli, mmodzi mwa zidzukulu za Abrahamu, ndiponso wa fuko la Benjamini. 2 Mulungu sanawakane anthu ake amene Iye anawadziwiratu. Kodi inu simukudziwa zimene Malemba akunena pa ndime imene Eliya akudandaula kwa Mulungu kuneneza Aisraeli? Iye anati, 3 “Ambuye, anthuwa apha aneneri anu ndi kugwetsa maguwa anu ansembe. Ndatsala ine ndekha wamoyo ndipo akufuna kundipha?” 4 Ndipo yankho la Mulungu linali lotani? “Ine ndadzisungira ndekha anthu 7,000 amene sanapembedzepo Baala.” 5 Chimodzimodzinso lero lino, alipo Aisraeli pangʼono osankhidwa mwachisomo. 6 Ndipo ngati ndi mwachisomo, sikungakhalenso mwa ntchito. Ngati zikanatero, chisomo sichikanakhalanso chisomo ayi.
7 Nʼchiyani tsopano? Chimene Aisraeli anachifuna ndi mtima wonse sanachipeze koma osankhidwawo anachipeza. Enawo anawumitsidwa mtima 8 monga kwalembedwa kuti,
“Mulungu anawapatsa mzimu wosatha kumvetsa zinthu,
maso osatha kupenya;
makutu osatha kumva
mpaka lero lino.”
9 Ndipo Davide akuti,
“Maphwando awo asanduke msampha ndi diwa lowakola
ndi chopunthwitsa kuti alandire chilango.
10 Maso awo atsekedwe kuti asaone,
ndi misana yawo ikhale yokhota nthawi zonse.”
Nthambi Zomangiriridwa
11 Ine ndikufunsanso kuti, kodi iwo anapunthwa ndi kugwa kotheratu? Ayi. Ndi pangʼono pomwe! Koma chifukwa cha kulakwa kwawo, chipulumutso chinafika kwa a mitundu ina kuti Aisraeli achite nsanje. 12 Koma ngati kulakwa kwawo kwapindulitsa dziko lapansi ndi kulephera kwawo kwapindulitsa a mitundu ina, nanga kudzakhala kupindula kwakukulu chotani iwo akadzabwera chonse!
13 Ine ndikuyankhula kwa inu a mitundu ina monga ine ndili mtumwi wa kwa a mitundu ina ndipo ndimawunyadira utumiki wangawu. 14 Ine cholinga changa nʼchakuti ndichititse nsanje anthu a mtundu wanga kuti ena mwa iwo apulumutsidwe. 15 Pakuti ngati kukanidwa kwawo kunayanjanitsa anthu a dziko lapansi ndi Mulungu, nanga kudzatani, Iye akadzawalandiranso? Kudzakhala monga ngati anthu akufa akuuka. 16 Ngati chigawo chimodzi cha buledi woperekedwa monga zipatso zoyamba ndi choyera, ndiye kuti zonsezo ndi zoyera. Ngati muzu ndi oyera, nʼchimodzimodzinso nthambi zake.
17 Ngati nthambi zina zinakhadzulidwa ndipo inu, inu ndiye nthambi za olivi wakuthengo, nʼkulumikizidwa pamalo pa nthambi zimenezo, ndipo tsopano mukulandira nawo zakudya zochokera ku mizu ya olivi, 18 musadzitame kunyoza nthambi zinazo. Ngati mutero, ganizirani ichi kuti Inu simugwiriziza mizu, koma muzu ukugwiriziza inu. 19 Tsono mudzati, “Nthambizo zinakhadzulidwa kuti ine ndilumikizidwepo.” 20 Nʼzoona. Koma iwo anakhadzulidwa chifukwa chosakhulupirira ndipo inu mukuyima mwachikhulupiriro. Musadzitukumule, koma muchite mantha. 21 Pakuti ngati Mulungu sanalekerere nthambi zachibadwidwe, Iye sadzakulekererani inunso.
22 Nʼchifukwa chake ganizirani za kukoma mtima ndi za ukali wa Mulungu. Ukali uli kwa iwo amene anagwa koma kukoma mtima kwa inu, malinga ngati musamala kukoma mtima kwakeko kupanda kutero inunso mudzakhadzulidwanso. 23 Ngati iwo asiya kukhala osakhulupirira, adzalumikizidwanso pakuti Mulungu akhoza kuwalumikizanso. 24 Pakuti ngati inu, mwa chilengedwe munali mtengo wa olivi wa kuthengo, Mulungu anakukhadzulani nakulumikizani ku mtengo wa olivi wodzalidwa, zomwe ndi zotsutsana ndi chilengedwe, kodi sikudzakhala kwapafupi kwa Iye kuwalumikizanso mu mtengo wawowawo wa olivi?
Aisraeli Onse Adzapulumuka
25 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa za chinsinsi ichi, kuti mungadziyese nokha anzeru. Kuwuma mtima kumene Aisraeli akuchita ndi kwa kanthawi kufikira chiwerengero cha a mitundu chitalowa. 26 Kotero tsono Aisraeli onse adzapulumuka, monga kwalembedwa kuti,
“Mpulumutsi adzachokera ku Ziyoni;
Iye adzachotsa zoyipa zonse za Yakobo.
27 Ndipo ili lidzakhala pangano langa ndi iwo
pamene Ine ndidzachotsa machimo awo.”
28 Chifukwa cha Uthenga Wabwino, Aisraeli asanduka adani a Mulungu kuti inu mupindule. Koma kunena za kusankhidwa, iwo ndi okondedwa ndi Mulungu chifukwa cha makolo awo aja. 29 Pakuti Mulungu akayitana munthu ndi kumupatsa mphatso sangasinthenso. 30 Monga mmene inu munalili, osamvera Mulungu pa nthawi ina, tsopano mwalandira chifundo chifukwa cha kusamvera kwawo. 31 Chonchonso iwo akhala osamvera tsopano kuti iwonso alandire chifundo chifukwa cha chifundo cha Mulungu kwa inu. 32 Pakuti Mulungu anasandutsa anthu onse a mʼndende ya kusamvera kuti Iye akaonetse chifundo kwa onse.
Kulemekeza Mulungu
33 Aa! Nzeru za Mulungu ndi chidziwitso chake ndi zozama kwambiri!
Ndani angazindikire maweruzidwe ake,
ndipo njira zake angazitulukire ndani?
34 “Kodi wadziwa ndani maganizo a Ambuye?
Kapena ndani anakhalapo mlangizi wake?”
35 “Kodi ndani anapereka mphatso kwa Mulungu,
kuti Mulunguyo amubwezere iye?”
36 Pakuti zinthu zonse nʼzochokera kwa Iye, nʼzolengedwa ndi Iye ndipo zimabweretsa ulemerero kwa Iye.
Kwa Iye kukhale ulemerero mpaka muyaya! Ameni.
Romans 11
English Standard Version
The Remnant of Israel
11 I ask, then, (A)has God rejected his people? By no means! For (B)I myself am an Israelite, a descendant of Abraham,[a] a member of the tribe of Benjamin. 2 (C)God has not rejected his people whom he (D)foreknew. Do you not know what the Scripture says of Elijah, how he appeals to God against Israel? 3 (E)“Lord, they have killed your prophets, they have demolished your altars, and I alone am left, and they seek my life.” 4 But what is God's reply to him? (F)“I have kept for myself seven thousand men who have not bowed the knee to Baal.” 5 So too at the present time there is (G)a remnant, chosen by grace. 6 (H)But if it is by grace, it is no longer on the basis of works; otherwise grace would no longer be grace.
7 What then? (I)Israel failed to obtain what it was seeking. The elect obtained it, but the rest (J)were hardened, 8 as it is written,
(K)“God gave them a spirit of stupor,
(L)eyes that would not see
and ears that would not hear,
down to this very day.”
9 And David says,
(M)“Let their table become a snare and a trap,
a stumbling block and a retribution for them;
10 let their eyes be darkened so that they cannot see,
and bend their backs forever.”
Gentiles Grafted In
11 So I ask, did they stumble in order that they might fall? By no means! Rather, through their trespass (N)salvation has come to the Gentiles, so as to make Israel jealous. 12 Now if their trespass means riches for the world, and if their failure means riches for the Gentiles, how much more will their full inclusion[b] mean!
13 Now I am speaking to you Gentiles. Inasmuch then as (O)I am an apostle to the Gentiles, I magnify my ministry 14 in order somehow to make my fellow Jews jealous, and (P)thus save some of them. 15 For if their rejection means (Q)the reconciliation of the world, what will their acceptance mean but life from the dead? 16 (R)If the dough offered as firstfruits is holy, so is the whole lump, and if the root is holy, so are the branches.
17 But if (S)some of the branches were broken off, and you, (T)although a wild olive shoot, were grafted in among the others and now share in the nourishing root[c] of the olive tree, 18 do not be arrogant toward the branches. If you are, remember it is not you who support the root, but the root that supports you. 19 Then you will say, “Branches were broken off so that I might be grafted in.” 20 That is true. They were broken off because of their unbelief, but you (U)stand fast through faith. So (V)do not become proud, but (W)fear. 21 For if God did not spare the natural branches, neither will he spare you. 22 Note then the kindness and the severity of God: severity toward those who have fallen, but God's kindness to you, (X)provided you continue in his kindness. Otherwise (Y)you too will be cut off. 23 And (Z)even they, if they do not continue in their unbelief, will be grafted in, for God has the power to graft them in again. 24 For if you were cut from what is by nature a wild olive tree, and grafted, contrary to nature, into a cultivated olive tree, how much more will these, the natural branches, be grafted back into their own olive tree.
The Mystery of Israel's Salvation
25 (AA)Lest you be wise in your own sight, I do not want you to be unaware of this mystery, brothers:[d] (AB)a partial hardening has come upon Israel, (AC)until the fullness of the Gentiles has come in. 26 And in this way all Israel will be saved, as it is written,
(AD)“The Deliverer will come (AE)from Zion,
he will banish ungodliness from Jacob”;
27 “and this will be my (AF)covenant with them
(AG)when I take away their sins.”
28 As regards the gospel, they are enemies for your sake. But as regards election, they are (AH)beloved for the sake of their forefathers. 29 For the gifts and (AI)the calling of God are irrevocable. 30 For just as (AJ)you were at one time disobedient to God but now have received mercy because of their disobedience, 31 so they too have now been disobedient in order that by the mercy shown to you they also may now[e] receive mercy. 32 For God (AK)has consigned all to disobedience, that he may have mercy on all.
33 Oh, the depth of the riches and (AL)wisdom and knowledge of God! (AM)How unsearchable are his judgments and how inscrutable his ways!
34 “For (AN)who has known the mind of the Lord,
or (AO)who has been his counselor?”
35 “Or (AP)who has given a gift to him
that he might be repaid?”
36 For (AQ)from him and through him and to him are all things. (AR)To him be glory forever. Amen.
Footnotes
- Romans 11:1 Or one of the offspring of Abraham
- Romans 11:12 Greek their fullness
- Romans 11:17 Greek root of richness; some manuscripts richness
- Romans 11:25 Or brothers and sisters
- Romans 11:31 Some manuscripts omit now
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The ESV® Bible (The Holy Bible, English Standard Version®), © 2001 by Crossway, a publishing ministry of Good News Publishers. ESV Text Edition: 2025.
