Psalm 4
King James Version
4 Hear me when I call, O God of my righteousness: thou hast enlarged me when I was in distress; have mercy upon me, and hear my prayer.
2 O ye sons of men, how long will ye turn my glory into shame? how long will ye love vanity, and seek after leasing? Selah.
3 But know that the Lord hath set apart him that is godly for himself: the Lord will hear when I call unto him.
4 Stand in awe, and sin not: commune with your own heart upon your bed, and be still. Selah.
5 Offer the sacrifices of righteousness, and put your trust in the Lord.
6 There be many that say, Who will shew us any good? Lord, lift thou up the light of thy countenance upon us.
7 Thou hast put gladness in my heart, more than in the time that their corn and their wine increased.
8 I will both lay me down in peace, and sleep: for thou, Lord, only makest me dwell in safety.
Masalimo 4
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide.
4 Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu,
    Inu Mulungu wa chilungamo changa.
Pumulitseni ku zowawa zanga;
    chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi?
    Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza?
            Sela.
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika;
    Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 Kwiyani koma musachimwe;
    pamene muli pa mabedi anu,
    santhulani mitima yanu ndi kukhala chete.
            Sela
5 Perekani nsembe zolungama
    ndipo dalirani Yehova.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?”
    Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu
    kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere,
    pakuti Inu nokha, Inu Yehova,
    mumandisamalira bwino.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.