Miyambo 6:6-11
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
6 Pita kwa nyerere, mlesi iwe;
kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
7 Zilibe mfumu,
zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
8 komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe
ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.
9 Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe?
Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono
ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 umphawi udzakugwira ngati mbala
ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.