Add parallel Print Page Options

Pita kwa nyerere, mlesi iwe;
    kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!
Zilibe mfumu,
    zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,
komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe
    ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.

Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe?
    Kodi tulo tako tidzatha liti?
10 Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono
    ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,
11 umphawi udzakugwira ngati mbala
    ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.

Read full chapter