Nyimbo ya Solomoni 6
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Abwenzi
6 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?
Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti
kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
Mkazi
2 Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,
ku timinda ta zokometsera zakudya,
akukadyetsa ziweto zake ku minda,
ndiponso akuthyola maluwa okongola.
3 Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;
amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
Mwamuna
4 Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,
wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,
ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
5 Usandipenyetsetse;
pakuti maso ako amanditenga mtima.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
6 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa
zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,
iliyonse ili ndi ana amapasa,
palibe imene ili yokha.
7 Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,
masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
8 Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,
ndi azikazi 80,
ndi anamwali osawerengeka;
9 koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;
mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,
mwana wapamtima wa amene anamubereka.
Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;
akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
Abwenzi
10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,
wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,
wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
Mwamuna
11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi
kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,
kukaona ngati mpesa waphukira
kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
12 Ndisanazindikire kanthu,
ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
Abwenzi
13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;
bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!
Mwamuna
Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,
pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?
Song of Songs 6
New International Version
Friends
6 Where has your beloved(A) gone,
most beautiful of women?(B)
Which way did your beloved turn,
that we may look for him with you?
She
2 My beloved has gone(C) down to his garden,(D)
to the beds of spices,(E)
to browse in the gardens
and to gather lilies.
3 I am my beloved’s and my beloved is mine;(F)
he browses among the lilies.(G)
He
4 You are as beautiful as Tirzah,(H) my darling,
as lovely as Jerusalem,(I)
as majestic as troops with banners.(J)
5 Turn your eyes from me;
they overwhelm me.
Your hair is like a flock of goats
descending from Gilead.(K)
6 Your teeth are like a flock of sheep
coming up from the washing.
Each has its twin,
not one of them is missing.(L)
7 Your temples behind your veil(M)
are like the halves of a pomegranate.(N)
8 Sixty queens(O) there may be,
and eighty concubines,(P)
and virgins beyond number;
9 but my dove,(Q) my perfect one,(R) is unique,
the only daughter of her mother,
the favorite of the one who bore her.(S)
The young women saw her and called her blessed;
the queens and concubines praised her.
Friends
10 Who is this that appears like the dawn,
fair as the moon, bright as the sun,
majestic as the stars in procession?
He
11 I went down to the grove of nut trees
to look at the new growth in the valley,
to see if the vines had budded
or the pomegranates were in bloom.(T)
12 Before I realized it,
my desire set me among the royal chariots of my people.[a]
Friends
13 Come back, come back, O Shulammite;
come back, come back, that we may gaze on you!
He
Footnotes
- Song of Songs 6:12 Or among the chariots of Amminadab; or among the chariots of the people of the prince
- Song of Songs 6:13 In Hebrew texts this verse (6:13) is numbered 7:1.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.