Add parallel Print Page Options

Abwenzi

Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,
    kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?
Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti
    kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,
    ku timinda ta zokometsera zakudya,
akukadyetsa ziweto zake ku minda,
    ndiponso akuthyola maluwa okongola.
Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;
    amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

Mwamuna

Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,
    wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,
    ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
Usandipenyetsetse;
    pakuti maso ako amanditenga mtima.
Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi
    zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Mano ako ali ngati gulu la nkhosa
    zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,
iliyonse ili ndi ana amapasa,
    palibe imene ili yokha.
Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,
    masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,
    ndi azikazi 80,
    ndi anamwali osawerengeka;
koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;
    mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,
    mwana wapamtima wa amene anamubereka.
Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;
    akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.

Abwenzi

10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,
    wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,
    wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?

Mwamuna

11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi
    kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,
kukaona ngati mpesa waphukira
    kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
12 Ndisanazindikire kanthu,
    ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.

Abwenzi

13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;
    bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!

Mwamuna

Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,
    pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

Friends

Where has your beloved(A) gone,
    most beautiful of women?(B)
Which way did your beloved turn,
    that we may look for him with you?

She

My beloved has gone(C) down to his garden,(D)
    to the beds of spices,(E)
to browse in the gardens
    and to gather lilies.
I am my beloved’s and my beloved is mine;(F)
    he browses among the lilies.(G)

He

You are as beautiful as Tirzah,(H) my darling,
    as lovely as Jerusalem,(I)
    as majestic as troops with banners.(J)
Turn your eyes from me;
    they overwhelm me.
Your hair is like a flock of goats
    descending from Gilead.(K)
Your teeth are like a flock of sheep
    coming up from the washing.
Each has its twin,
    not one of them is missing.(L)
Your temples behind your veil(M)
    are like the halves of a pomegranate.(N)
Sixty queens(O) there may be,
    and eighty concubines,(P)
    and virgins beyond number;
but my dove,(Q) my perfect one,(R) is unique,
    the only daughter of her mother,
    the favorite of the one who bore her.(S)
The young women saw her and called her blessed;
    the queens and concubines praised her.

Friends

10 Who is this that appears like the dawn,
    fair as the moon, bright as the sun,
    majestic as the stars in procession?

He

11 I went down to the grove of nut trees
    to look at the new growth in the valley,
to see if the vines had budded
    or the pomegranates were in bloom.(T)
12 Before I realized it,
    my desire set me among the royal chariots of my people.[a]

Friends

13 Come back, come back, O Shulammite;
    come back, come back, that we may gaze on you!

He

Why would you gaze on the Shulammite
    as on the dance(U) of Mahanaim?[b]

Footnotes

  1. Song of Songs 6:12 Or among the chariots of Amminadab; or among the chariots of the people of the prince
  2. Song of Songs 6:13 In Hebrew texts this verse (6:13) is numbered 7:1.