Add parallel Print Page Options

Akohati

Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni: “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.

“Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri. Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni. Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

“Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse. Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.

“Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta. 10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.

11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.

12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.

13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake. 14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.

15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.

16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”

17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti, 18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi. 19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula. 20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”

Ageresoni

21 Yehova anawuza Mose kuti, 22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo. 23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.

24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi: 25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano, 26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi. 27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira. 28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.

Amerari

29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo. 30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano. 31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde, 32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita. 33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”

Chiwerengero cha Fuko la Levi

34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750. 37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano, 40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630. 41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.

42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano, 44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200. 45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.

46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo. 47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano 48 analipo 8,580. 49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose.

Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.

耶 和 華 曉 諭 摩 西 、 亞 倫 說 :

你 從 利 未 人 中 , 將 哥 轄 子 孫 的 總 數 , 照 他 們 的 家 室 、 宗 族 ,

從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 全 都 計 算 。

哥 轄 子 孫 在 會 幕 搬 運 至 聖 之 物 , 所 辦 的 事 乃 是 這 樣 :

起 營 的 時 候 , 亞 倫 和 他 兒 子 要 進 去 摘 下 遮 掩 櫃 的 幔 子 , 用 以 蒙 蓋 法 櫃 ,

又 用 海 狗 皮 蓋 在 上 頭 , 再 蒙 上 純 藍 色 的 毯 子 , 把 杠 穿 上 。

又 用 藍 色 毯 子 鋪 在 陳 設 餅 的 桌 子 上 , 將 盤 子 、 調 羹 、 奠 酒 的 爵 , 和 杯 擺 在 上 頭 。 桌 子 上 也 必 有 常 設 的 餅 。

在 其 上 又 要 蒙 朱 紅 色 的 毯 子 , 再 蒙 上 海 狗 皮 , 把 杠 穿 上 。

要 拿 藍 色 毯 子 , 把 燈 臺 和 燈 臺 上 所 用 的 燈 盞 、 剪 子 、 蠟 花 盤 , 並 一 切 盛 油 的 器 皿 , 全 都 遮 蓋 。

10 又 要 把 燈 臺 和 燈 臺 的 一 切 器 具 包 在 海 狗 皮 裡 , 放 在 抬 架 上 。

11 在 金 壇 上 要 鋪 藍 色 毯 子 , 蒙 上 海 狗 皮 , 把 杠 穿 上 。

12 又 要 把 聖 所 用 的 一 切 器 具 包 在 藍 色 毯 子 裡 , 用 海 狗 皮 蒙 上 , 放 在 抬 架 上 。

13 要 收 去 壇 上 的 灰 , 把 紫 色 毯 子 鋪 在 壇 上 ;

14 又 要 把 所 用 的 一 切 器 具 , 就 是 火 鼎 、 肉 鍤 子 、 鏟 子 、 盤 子 , 一 切 屬 壇 的 器 具 都 擺 在 壇 上 , 又 蒙 上 海 狗 皮 , 把 杠 穿 上 。

15 將 要 起 營 的 時 候 , 亞 倫 和 他 兒 子 把 聖 所 和 聖 所 的 一 切 器 具 遮 蓋 完 了 , 哥 轄 的 子 孫 就 要 來 抬 , 只 是 不 可 摸 聖 物 , 免 得 他 們 死 亡 。 會 幕 裡 這 些 物 件 是 哥 轄 子 孫 所 當 抬 的 。

16 祭 司 亞 倫 的 兒 子 以 利 亞 撒 所 要 看 守 的 是 點 燈 的 油 與 香 料 , 並 當 獻 的 素 祭 和 膏 油 , 也 要 看 守 全 帳 幕 與 其 中 所 有 的 , 並 聖 所 和 聖 所 的 器 具 。

17 耶 和 華 曉 諭 摩 西 、 亞 倫 說 :

18 你 們 不 可 將 哥 轄 人 的 支 派 從 利 未 人 中 剪 除 。

19 他 們 挨 近 至 聖 物 的 時 候 , 亞 倫 和 他 兒 子 要 進 去 派 他 們 各 人 所 當 辦 的 , 所 當 抬 的 。 這 樣 待 他 們 , 好 使 他 們 活 著 , 不 至 死 亡 。

20 只 是 他 們 連 片 時 不 可 進 去 觀 看 聖 所 , 免 得 他 們 死 亡 。

21 耶 和 華 曉 諭 摩 西 說 :

22 你 要 將 革 順 子 孫 的 總 數 , 照 著 宗 族 、 家 室 ,

23 從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 全 都 數 點 。

24 革 順 人 各 族 所 辦 的 事 、 所 抬 的 物 乃 是 這 樣 :

25 他 們 要 抬 帳 幕 的 幔 子 和 會 幕 , 並 會 幕 的 蓋 與 其 上 的 海 狗 皮 , 和 會 幕 的 門 簾 ,

26 院 子 的 帷 子 和 門 簾 ( 院 子 是 圍 帳 幕 和 壇 的 ) 、 繩 子 , 並 所 用 的 器 具 , 不 論 是 做 甚 麼 用 的 , 他 們 都 要 經 理 。

27 革 順 的 子 孫 在 一 切 抬 物 辦 事 之 上 都 要 憑 亞 倫 和 他 兒 子 的 吩 咐 ; 他 們 所 當 抬 的 , 要 派 他 們 看 守 。

28 這 是 革 順 子 孫 的 各 族 在 會 幕 裡 所 辦 的 事 ; 他 們 所 看 守 的 , 必 在 祭 司 亞 倫 兒 子 以 他 瑪 的 手 下 。

29 至 於 米 拉 利 的 子 孫 , 你 要 照 著 家 室 、 宗 族 把 他 們 數 點 。

30 從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 你 都 要 數 點 。

31 他 們 辦 理 會 幕 的 事 , 就 是 抬 帳 幕 的 板 、 閂 、 柱 子 , 和 帶 卯 的 座 ,

32 院 子 四 圍 的 柱 子 和 其 上 帶 卯 的 座 、 橛 子 、 繩 子 , 並 一 切 使 用 的 器 具 。 他 們 所 抬 的 器 具 , 你 們 要 按 名 指 定 。

33 這 是 米 拉 利 子 孫 各 族 在 會 幕 裡 所 辦 的 事 , 都 在 祭 司 亞 倫 兒 子 以 他 瑪 的 手 下 。

34 摩 西 、 亞 倫 與 會 眾 的 諸 首 領 將 哥 轄 的 子 孫 , 照 著 家 室 、 宗 族 ,

35 從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 都 數 點 了 。

36 被 數 的 共 有 二 千 七 百 五 十 名 。

37 這 是 哥 轄 各 族 中 被 數 的 , 是 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 就 是 摩 西 、 亞 倫 照 耶 和 華 藉 摩 西 所 吩 咐 數 點 的 。

38 革 順 子 孫 被 數 的 , 照 著 家 室 、 宗 族 ,

39 從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 共 有 二 千 六 百 三 十 名 。

40 a

41 這 是 革 順 子 孫 各 族 中 被 數 的 , 是 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 就 是 摩 西 、 亞 倫 照 耶 和 華 藉 摩 西 所 吩 咐 數 點 的 。

42 米 拉 利 子 孫 中 各 族 被 數 的 , 照 著 家 室 、 宗 族 ,

43 從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 辦 事 的 , 共 有 三 千 二 百 名 。

44 a

45 這 是 米 拉 利 子 孫 各 族 中 被 數 的 , 就 是 摩 西 、 亞 倫 照 耶 和 華 藉 摩 西 所 吩 咐 數 點 的 。

46 凡 被 數 的 利 未 人 , 就 是 摩 西 、 亞 倫 並 以 色 列 眾 首 領 , 照 著 家 室 、 宗 族 所 數 點 的 ,

47 從 三 十 歲 直 到 五 十 歲 , 凡 前 來 任 職 、 在 會 幕 裡 做 抬 物 之 工 的 , 共 有 八 千 五 百 八 十 名 。

48 a

49 摩 西 按 他 們 所 辦 的 事 、 所 抬 的 物 , 憑 耶 和 華 的 吩 咐 數 點 他 們 ; 他 們 這 樣 被 摩 西 數 點 , 正 如 耶 和 華 所 吩 咐 他 的 。

And the Lord spake unto Moses and unto Aaron, saying,

Take the sum of the sons of Kohath from among the sons of Levi, after their families, by the house of their fathers,

From thirty years old and upward even until fifty years old, all that enter into the host, to do the work in the tabernacle of the congregation.

This shall be the service of the sons of Kohath in the tabernacle of the congregation, about the most holy things:

And when the camp setteth forward, Aaron shall come, and his sons, and they shall take down the covering vail, and cover the ark of testimony with it:

And shall put thereon the covering of badgers' skins, and shall spread over it a cloth wholly of blue, and shall put in the staves thereof.

And upon the table of shewbread they shall spread a cloth of blue, and put thereon the dishes, and the spoons, and the bowls, and covers to cover withal: and the continual bread shall be thereon:

And they shall spread upon them a cloth of scarlet, and cover the same with a covering of badgers' skins, and shall put in the staves thereof.

And they shall take a cloth of blue, and cover the candlestick of the light, and his lamps, and his tongs, and his snuffdishes, and all the oil vessels thereof, wherewith they minister unto it:

10 And they shall put it and all the vessels thereof within a covering of badgers' skins, and shall put it upon a bar.

11 And upon the golden altar they shall spread a cloth of blue, and cover it with a covering of badgers' skins, and shall put to the staves thereof:

12 And they shall take all the instruments of ministry, wherewith they minister in the sanctuary, and put them in a cloth of blue, and cover them with a covering of badgers' skins, and shall put them on a bar:

13 And they shall take away the ashes from the altar, and spread a purple cloth thereon:

14 And they shall put upon it all the vessels thereof, wherewith they minister about it, even the censers, the fleshhooks, and the shovels, and the basons, all the vessels of the altar; and they shall spread upon it a covering of badgers' skins, and put to the staves of it.

15 And when Aaron and his sons have made an end of covering the sanctuary, and all the vessels of the sanctuary, as the camp is to set forward; after that, the sons of Kohath shall come to bear it: but they shall not touch any holy thing, lest they die. These things are the burden of the sons of Kohath in the tabernacle of the congregation.

16 And to the office of Eleazar the son of Aaron the priest pertaineth the oil for the light, and the sweet incense, and the daily meat offering, and the anointing oil, and the oversight of all the tabernacle, and of all that therein is, in the sanctuary, and in the vessels thereof.

17 And the Lord spake unto Moses and unto Aaron saying,

18 Cut ye not off the tribe of the families of the Kohathites from among the Levites:

19 But thus do unto them, that they may live, and not die, when they approach unto the most holy things: Aaron and his sons shall go in, and appoint them every one to his service and to his burden:

20 But they shall not go in to see when the holy things are covered, lest they die.

21 And the Lord spake unto Moses, saying,

22 Take also the sum of the sons of Gershon, throughout the houses of their fathers, by their families;

23 From thirty years old and upward until fifty years old shalt thou number them; all that enter in to perform the service, to do the work in the tabernacle of the congregation.

24 This is the service of the families of the Gershonites, to serve, and for burdens:

25 And they shall bear the curtains of the tabernacle, and the tabernacle of the congregation, his covering, and the covering of the badgers' skins that is above upon it, and the hanging for the door of the tabernacle of the congregation,

26 And the hangings of the court, and the hanging for the door of the gate of the court, which is by the tabernacle and by the altar round about, and their cords, and all the instruments of their service, and all that is made for them: so shall they serve.

27 At the appointment of Aaron and his sons shall be all the service of the sons of the Gershonites, in all their burdens, and in all their service: and ye shall appoint unto them in charge all their burdens.

28 This is the service of the families of the sons of Gershon in the tabernacle of the congregation: and their charge shall be under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.

29 As for the sons of Merari, thou shalt number them after their families, by the house of their fathers;

30 From thirty years old and upward even unto fifty years old shalt thou number them, every one that entereth into the service, to do the work of the tabernacle of the congregation.

31 And this is the charge of their burden, according to all their service in the tabernacle of the congregation; the boards of the tabernacle, and the bars thereof, and the pillars thereof, and sockets thereof,

32 And the pillars of the court round about, and their sockets, and their pins, and their cords, with all their instruments, and with all their service: and by name ye shall reckon the instruments of the charge of their burden.

33 This is the service of the families of the sons of Merari, according to all their service, in the tabernacle of the congregation, under the hand of Ithamar the son of Aaron the priest.

34 And Moses and Aaron and the chief of the congregation numbered the sons of the Kohathites after their families, and after the house of their fathers,

35 From thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entereth into the service, for the work in the tabernacle of the congregation:

36 And those that were numbered of them by their families were two thousand seven hundred and fifty.

37 These were they that were numbered of the families of the Kohathites, all that might do service in the tabernacle of the congregation, which Moses and Aaron did number according to the commandment of the Lord by the hand of Moses.

38 And those that were numbered of the sons of Gershon, throughout their families, and by the house of their fathers,

39 From thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entereth into the service, for the work in the tabernacle of the congregation,

40 Even those that were numbered of them, throughout their families, by the house of their fathers, were two thousand and six hundred and thirty.

41 These are they that were numbered of the families of the sons of Gershon, of all that might do service in the tabernacle of the congregation, whom Moses and Aaron did number according to the commandment of the Lord.

42 And those that were numbered of the families of the sons of Merari, throughout their families, by the house of their fathers,

43 From thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that entereth into the service, for the work in the tabernacle of the congregation,

44 Even those that were numbered of them after their families, were three thousand and two hundred.

45 These be those that were numbered of the families of the sons of Merari, whom Moses and Aaron numbered according to the word of the Lord by the hand of Moses.

46 All those that were numbered of the Levites, whom Moses and Aaron and the chief of Israel numbered, after their families, and after the house of their fathers,

47 From thirty years old and upward even unto fifty years old, every one that came to do the service of the ministry, and the service of the burden in the tabernacle of the congregation.

48 Even those that were numbered of them, were eight thousand and five hundred and fourscore,

49 According to the commandment of the Lord they were numbered by the hand of Moses, every one according to his service, and according to his burden: thus were they numbered of him, as the Lord commanded Moses.