Numeri 29
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Chikondwerero cha Malipenga
29 “ ‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga. 2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova. 3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri. 4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi. 5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. 6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
Tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo
7 “ ‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito. 8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema. 9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri; 10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo. 11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
Chikondwerero cha Misasa
12 “ ‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri. 13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri. 15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi. 16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 “ ‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema. 18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 “ ‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 “ ‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 “ ‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 “ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 “ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 “ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 “ ‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’ ”
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
Numbers 29
King James Version
29 And in the seventh month, on the first day of the month, ye shall have an holy convocation; ye shall do no servile work: it is a day of blowing the trumpets unto you.
2 And ye shall offer a burnt offering for a sweet savour unto the Lord; one young bullock, one ram, and seven lambs of the first year without blemish:
3 And their meat offering shall be of flour mingled with oil, three tenth deals for a bullock, and two tenth deals for a ram,
4 And one tenth deal for one lamb, throughout the seven lambs:
5 And one kid of the goats for a sin offering, to make an atonement for you:
6 Beside the burnt offering of the month, and his meat offering, and the daily burnt offering, and his meat offering, and their drink offerings, according unto their manner, for a sweet savour, a sacrifice made by fire unto the Lord.
7 And ye shall have on the tenth day of this seventh month an holy convocation; and ye shall afflict your souls: ye shall not do any work therein:
8 But ye shall offer a burnt offering unto the Lord for a sweet savour; one young bullock, one ram, and seven lambs of the first year; they shall be unto you without blemish:
9 And their meat offering shall be of flour mingled with oil, three tenth deals to a bullock, and two tenth deals to one ram,
10 A several tenth deal for one lamb, throughout the seven lambs:
11 One kid of the goats for a sin offering; beside the sin offering of atonement, and the continual burnt offering, and the meat offering of it, and their drink offerings.
12 And on the fifteenth day of the seventh month ye shall have an holy convocation; ye shall do no servile work, and ye shall keep a feast unto the Lord seven days:
13 And ye shall offer a burnt offering, a sacrifice made by fire, of a sweet savour unto the Lord; thirteen young bullocks, two rams, and fourteen lambs of the first year; they shall be without blemish:
14 And their meat offering shall be of flour mingled with oil, three tenth deals unto every bullock of the thirteen bullocks, two tenth deals to each ram of the two rams,
15 And a several tenth deal to each lamb of the fourteen lambs:
16 And one kid of the goats for a sin offering; beside the continual burnt offering, his meat offering, and his drink offering.
17 And on the second day ye shall offer twelve young bullocks, two rams, fourteen lambs of the first year without spot:
18 And their meat offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
19 And one kid of the goats for a sin offering; beside the continual burnt offering, and the meat offering thereof, and their drink offerings.
20 And on the third day eleven bullocks, two rams, fourteen lambs of the first year without blemish;
21 And their meat offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
22 And one goat for a sin offering; beside the continual burnt offering, and his meat offering, and his drink offering.
23 And on the fourth day ten bullocks, two rams, and fourteen lambs of the first year without blemish:
24 Their meat offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
25 And one kid of the goats for a sin offering; beside the continual burnt offering, his meat offering, and his drink offering.
26 And on the fifth day nine bullocks, two rams, and fourteen lambs of the first year without spot:
27 And their meat offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
28 And one goat for a sin offering; beside the continual burnt offering, and his meat offering, and his drink offering.
29 And on the sixth day eight bullocks, two rams, and fourteen lambs of the first year without blemish:
30 And their meat offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
31 And one goat for a sin offering; beside the continual burnt offering, his meat offering, and his drink offering.
32 And on the seventh day seven bullocks, two rams, and fourteen lambs of the first year without blemish:
33 And their meat offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
34 And one goat for a sin offering; beside the continual burnt offering, his meat offering, and his drink offering.
35 On the eighth day ye shall have a solemn assembly: ye shall do no servile work therein:
36 But ye shall offer a burnt offering, a sacrifice made by fire, of a sweet savour unto the Lord: one bullock, one ram, seven lambs of the first year without blemish:
37 Their meat offering and their drink offerings for the bullock, for the ram, and for the lambs, shall be according to their number, after the manner:
38 And one goat for a sin offering; beside the continual burnt offering, and his meat offering, and his drink offering.
39 These things ye shall do unto the Lord in your set feasts, beside your vows, and your freewill offerings, for your burnt offerings, and for your meat offerings, and for your drink offerings, and for your peace offerings.
40 And Moses told the children of Israel according to all that the Lord commanded Moses.
Numbers 29
Legacy Standard Bible
The Various Offerings of the Seventh Month
29 ‘(A)Now in the seventh month, on the first day of the month, you shall also have a holy convocation; (B)you shall do no laborious work. It will be to you a day for blowing trumpets. 2 And you shall offer a burnt offering as a soothing aroma to Yahweh: one bull from the herd, one ram, and seven male lambs one year old without blemish; 3 also their grain offering, fine flour mixed with oil: three-tenths of an [a]ephah for the bull, two-tenths for the ram, 4 and one-tenth for [b]each of the seven lambs. 5 And offer one male goat for a sin offering, to make atonement for you, 6 (C)besides the burnt offering of the new moon and its grain offering, and the (D)continual burnt offering and its grain offering, and their drink offerings, according to their legal judgment, for a soothing aroma, an offering by fire to Yahweh.
7 ‘Then on (E)the tenth day of this seventh month you shall have a holy convocation, and you shall humble yourselves; you shall not do any work. 8 And you shall bring near a burnt offering to Yahweh as a soothing aroma: one bull from the herd, one ram, seven male lambs one year old, (F)having them without blemish; 9 and their grain offering, fine flour mixed with oil: three-tenths of an [c]ephah for the bull, two-tenths for the one ram, 10 a tenth for each of the seven lambs; 11 one male goat for a sin offering, besides (G)the sin offering of atonement and (H)the continual burnt offering and its grain offering and their drink offerings.
12 ‘Then on (I)the fifteenth day of the seventh month you shall have a holy convocation; you (J)shall do no laborious work, and you shall celebrate a feast to Yahweh for seven days. 13 And you shall bring near a burnt offering, an offering by fire as a soothing aroma to Yahweh: thirteen bulls from the herd, two rams, fourteen male lambs one year old, which are without blemish; 14 and their grain offering, fine flour mixed with oil: three-tenths of an [d]ephah for [e]each of the thirteen bulls, two-tenths for [f]each of the two rams, 15 and a tenth for each of the fourteen lambs; 16 and one male goat for a sin offering, (K)besides the continual burnt offering, its grain offering, and its drink offering.
17 ‘Then on (L)the second day: twelve bulls from the herd, two rams, fourteen male lambs one year old without blemish; 18 and their grain offering and their drink offerings for the bulls, for the rams and for the lambs, by their number (M)according to the legal judgment; 19 and one male goat for a sin offering, (N)besides the continual burnt offering and its grain offering and their drink offerings.
20 ‘Then on the third day: eleven bulls, two rams, fourteen male lambs one year old without blemish; 21 and their grain offering and their drink offerings for the bulls, for the rams and for the lambs, by their number according to the legal judgment; 22 and one male goat for a sin offering, besides the continual burnt offering and its grain offering and its drink offering.
23 ‘Then on the fourth day: ten bulls, two rams, fourteen male lambs one year old without blemish; 24 their grain offering and their drink offerings for the bulls, for the rams and for the lambs, by their number according to the legal judgment; 25 and one male goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, its grain offering and its drink offering.
26 ‘Then on the fifth day: nine bulls, two rams, fourteen male lambs one year old (O)without blemish; 27 and their grain offering and their drink offerings for the bulls, for the rams and for the lambs, by their number according to the legal judgment; 28 and one male goat for a sin offering, besides the continual burnt offering and its grain offering and its drink offering.
29 ‘Then on the sixth day: eight bulls, two rams, fourteen male lambs one year old without blemish; 30 and their grain offering and their drink offerings for the bulls, for the rams and for the lambs, by their number according to the legal judgment; 31 and one male goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, its grain offering and its drink offerings.
32 ‘Then on the seventh day: seven bulls, two rams, fourteen male lambs one year old without blemish; 33 and their grain offering and their drink offerings for the bulls, for the rams and for the lambs, by their number according to the legal judgment; 34 and one male goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, its grain offering and its drink offering.
35 ‘(P)On the eighth day you shall have a solemn assembly; you shall do no laborious work. 36 But you shall bring near a burnt offering, an offering by fire, as a soothing aroma to Yahweh: one bull, one ram, seven male lambs one year old without blemish; 37 their grain offering and their drink offerings for the bull, for the ram and for the lambs, by their number according to the legal judgment; 38 and one male goat for a sin offering, besides the continual burnt offering and its grain offering and its drink offering.
39 ‘You shall offer these to Yahweh at your (Q)appointed times, besides your [g]votive offerings and your freewill offerings, for your burnt offerings and for your grain offerings and for your drink offerings and for your peace offerings.’” 40 [h]And Moses spoke to the sons of Israel according to all that Yahweh had commanded Moses.
Footnotes
- Numbers 29:3 An ephah was approx. 21 qt. or 23 l
- Numbers 29:4 Lit each lamb, so in ch
- Numbers 29:9 An ephah was approx. 21 qt. or 23 l
- Numbers 29:14 An ephah was approx. 21 qt. or 23 l
- Numbers 29:14 Lit each bull
- Numbers 29:14 Lit each ram
- Numbers 29:39 Lit vows
- Numbers 29:40 Ch 30:1 in Heb
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Legacy Standard Bible Copyright ©2021 by The Lockman Foundation. All rights reserved. Managed in partnership with Three Sixteen Publishing Inc. LSBible.org For Permission to Quote Information visit https://www.LSBible.org.