Add parallel Print Page Options

Za Mkazi Wachigololo

Mwana wanga, mvera mawu anga;
    usunge bwino malamulo angawa.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo;
    samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako,
    ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,”
    ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo
    ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.

Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga
    ndinasuzumira pa zenera.
Ndinaona pakati pa anthu opusa,
    pakati pa anyamata,
    mnyamata wina wopanda nzeru.
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo,
    kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
Inali nthawi yachisisira madzulo,
    nthawi ya usiku, kuli mdima.

10 Ndipo mkaziyo anadzakumana naye,
    atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 (Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve,
    iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika,
    ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona
    ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,

14 “Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano.
    Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Choncho ndinabwera kudzakumana nawe;
    ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Pa bedi panga ndayalapo
    nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira
    za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa;
    tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako;
    wapita ulendo wautali:
20 Anatenga thumba la ndalama
    ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”

21 Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo;
    amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo
    ngati ngʼombe yopita kukaphedwa,
monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23     mpaka muvi utalasa chiwindi chake,
chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe,
    osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.

24 Tsono ana inu, ndimvereni;
    mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu;
    musasochere potsata njira zake.
26 Paja iye anagwetsa anthu ambiri;
    wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Nyumba yake ndi njira yopita ku manda,
    yotsikira ku malo a anthu akufa.

Warning Against the Adulterous Woman

My son,(A) keep my words
    and store up my commands within you.
Keep my commands and you will live;(B)
    guard my teachings as the apple of your eye.
Bind them on your fingers;
    write them on the tablet of your heart.(C)
Say to wisdom, “You are my sister,”
    and to insight, “You are my relative.”
They will keep you from the adulterous woman,
    from the wayward woman with her seductive words.(D)

At the window of my house
    I looked down through the lattice.
I saw among the simple,
    I noticed among the young men,
    a youth who had no sense.(E)
He was going down the street near her corner,
    walking along in the direction of her house
at twilight,(F) as the day was fading,
    as the dark of night set in.

10 Then out came a woman to meet him,
    dressed like a prostitute and with crafty intent.
11 (She is unruly(G) and defiant,
    her feet never stay at home;
12 now in the street, now in the squares,
    at every corner she lurks.)(H)
13 She took hold of him(I) and kissed him
    and with a brazen face she said:(J)

14 “Today I fulfilled my vows,
    and I have food from my fellowship offering(K) at home.
15 So I came out to meet you;
    I looked for you and have found you!
16 I have covered my bed
    with colored linens from Egypt.
17 I have perfumed my bed(L)
    with myrrh,(M) aloes and cinnamon.
18 Come, let’s drink deeply of love till morning;
    let’s enjoy ourselves with love!(N)
19 My husband is not at home;
    he has gone on a long journey.
20 He took his purse filled with money
    and will not be home till full moon.”

21 With persuasive words she led him astray;
    she seduced him with her smooth talk.(O)
22 All at once he followed her
    like an ox going to the slaughter,
like a deer[a] stepping into a noose[b](P)
23     till an arrow pierces(Q) his liver,
like a bird darting into a snare,
    little knowing it will cost him his life.(R)

24 Now then, my sons, listen(S) to me;
    pay attention to what I say.
25 Do not let your heart turn to her ways
    or stray into her paths.(T)
26 Many are the victims she has brought down;
    her slain are a mighty throng.
27 Her house is a highway to the grave,
    leading down to the chambers of death.(U)

Footnotes

  1. Proverbs 7:22 Syriac (see also Septuagint); Hebrew fool
  2. Proverbs 7:22 The meaning of the Hebrew for this line is uncertain.