Miyambo 28
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
28 Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,
koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,
koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake
ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,
koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,
koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Munthu wosauka wa makhalidwe abwino
aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,
koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka
amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Wokana kumvera malamulo
ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa
adzagwera mu msampha wake womwe,
koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,
koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;
koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,
koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,
koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa
ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza
koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu
adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;
wina aliyense asamuthandize.
18 Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa
koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,
koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,
koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 Kukondera si kwabwino,
ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera
koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake
mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Amene amabera abambo ake kapena amayi ake
namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”
ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Munthu wadyera amayambitsa mikangano,
koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,
koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,
koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,
koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.
Proverbs 28
New King James Version
The Righteous Are Bold as a Lion
28 The (A)wicked flee when no one pursues,
But the righteous are bold as a lion.
2 Because of the transgression of a land, many are its princes;
But by a man of understanding and knowledge
Right will be prolonged.
6 Better is the poor who walks in his integrity
Than one perverse in his ways, though he be rich.
7 Whoever keeps the law is a discerning son,
But a companion of gluttons shames his father.
8 One who increases his possessions by usury and extortion
Gathers it for him who will pity the poor.
9 One who turns away his ear from hearing the law,
(G)Even his prayer is an abomination.
10 (H)Whoever causes the upright to go astray in an evil way,
He himself will fall into his own pit;
(I)But the blameless will inherit good.
11 The rich man is wise in his own eyes,
But the poor who has understanding searches him out.
12 When the righteous rejoice, there is great (J)glory;
But when the wicked arise, men [b]hide themselves.
13 (K)He who covers his sins will not prosper,
But whoever confesses and forsakes them will have mercy.
14 Happy is the man who is always reverent,
But he who hardens his heart will fall into calamity.
16 A ruler who lacks understanding is a great (N)oppressor,
But he who hates covetousness will prolong his days.
17 (O)A man burdened with bloodshed will flee into a pit;
Let no one help him.
18 Whoever walks blamelessly will be [c]saved,
But he who is perverse in his ways will suddenly fall.
19 (P)He who tills his land will have plenty of bread,
But he who follows frivolity will have poverty enough!
20 A faithful man will abound with blessings,
(Q)But he who hastens to be rich will not go unpunished.
22 A man with an evil eye hastens after riches,
And does not consider that (T)poverty will come upon him.
23 (U)He who rebukes a man will find more favor afterward
Than he who flatters with the tongue.
24 Whoever robs his father or his mother,
And says, “It is no transgression,”
The same (V)is companion to a destroyer.
25 (W)He who is of a proud heart stirs up strife,
(X)But he who trusts in the Lord will be prospered.
26 He who (Y)trusts in his own heart is a fool,
But whoever walks wisely will be delivered.
27 (Z)He who gives to the poor will not lack,
But he who hides his eyes will have many curses.
28 When the wicked arise, (AA)men hide themselves;
But when they perish, the righteous increase.
Footnotes
- Proverbs 28:3 Lit. and there is no bread
- Proverbs 28:12 Lit. will be searched for
- Proverbs 28:18 delivered
- Proverbs 28:21 Lit. recognize faces
Proverbs 28
New International Version
2 When a country is rebellious, it has many rulers,
but a ruler with discernment and knowledge maintains order.
3 A ruler[a] who oppresses the poor
is like a driving rain that leaves no crops.
4 Those who forsake instruction praise the wicked,
but those who heed it resist them.
5 Evildoers do not understand what is right,
but those who seek the Lord understand it fully.
6 Better the poor whose walk is blameless
than the rich whose ways are perverse.(D)
7 A discerning son heeds instruction,
but a companion of gluttons disgraces his father.(E)
8 Whoever increases wealth by taking interest(F) or profit from the poor
amasses it for another,(G) who will be kind to the poor.(H)
9 If anyone turns a deaf ear to my instruction,
even their prayers are detestable.(I)
10 Whoever leads the upright along an evil path
will fall into their own trap,(J)
but the blameless will receive a good inheritance.
11 The rich are wise in their own eyes;
one who is poor and discerning sees how deluded they are.
12 When the righteous triumph, there is great elation;(K)
but when the wicked rise to power, people go into hiding.(L)
13 Whoever conceals their sins(M) does not prosper,
but the one who confesses(N) and renounces them finds mercy.(O)
14 Blessed is the one who always trembles before God,
but whoever hardens their heart falls into trouble.
15 Like a roaring lion or a charging bear
is a wicked ruler over a helpless people.
16 A tyrannical ruler practices extortion,
but one who hates ill-gotten gain will enjoy a long reign.
17 Anyone tormented by the guilt of murder
will seek refuge(P) in the grave;
let no one hold them back.
18 The one whose walk is blameless is kept safe,(Q)
but the one whose ways are perverse will fall(R) into the pit.[b]
19 Those who work their land will have abundant food,
but those who chase fantasies will have their fill of poverty.(S)
20 A faithful person will be richly blessed,
but one eager to get rich will not go unpunished.(T)
22 The stingy are eager to get rich
and are unaware that poverty awaits them.(X)
23 Whoever rebukes a person will in the end gain favor
rather than one who has a flattering tongue.(Y)
24 Whoever robs their father or mother(Z)
and says, “It’s not wrong,”
is partner to one who destroys.(AA)
27 Those who give to the poor will lack nothing,(AF)
but those who close their eyes to them receive many curses.(AG)
28 When the wicked rise to power, people go into hiding;(AH)
but when the wicked perish, the righteous thrive.
Footnotes
- Proverbs 28:3 Or A poor person
- Proverbs 28:18 Syriac (see Septuagint); Hebrew into one
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.

