Add parallel Print Page Options

Ubwino Wanzeru

Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga
    ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru
    ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
ngati upempha kuti uzindikire zinthu
    inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva
    ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;
    ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,
    ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.
    Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.
    Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,
    kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,
    kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;
    kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,
    kwa anthu amabodza,
13 amene amasiya njira zolungama
    namayenda mʼnjira zamdima,
14 amene amakondwera pochita zoyipa
    namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,
    ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;
    kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake
    ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;
    njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera
    kapena kupezanso njira zamoyo.

20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,
    uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko
    ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,
    ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

Moral Benefits of Wisdom

My son,(A) if you accept my words
    and store up my commands within you,
turning your ear to wisdom
    and applying your heart to understanding(B)
indeed, if you call out for insight(C)
    and cry aloud for understanding,
and if you look for it as for silver
    and search for it as for hidden treasure,(D)
then you will understand the fear of the Lord
    and find the knowledge of God.(E)
For the Lord gives wisdom;(F)
    from his mouth come knowledge and understanding.(G)
He holds success in store for the upright,
    he is a shield(H) to those whose walk is blameless,(I)
for he guards the course of the just
    and protects the way of his faithful ones.(J)

Then you will understand(K) what is right and just
    and fair—every good path.
10 For wisdom will enter your heart,(L)
    and knowledge will be pleasant to your soul.
11 Discretion will protect you,
    and understanding will guard you.(M)

12 Wisdom will save(N) you from the ways of wicked men,
    from men whose words are perverse,
13 who have left the straight paths
    to walk in dark ways,(O)
14 who delight in doing wrong
    and rejoice in the perverseness of evil,(P)
15 whose paths are crooked(Q)
    and who are devious in their ways.(R)

16 Wisdom will save you also from the adulterous woman,(S)
    from the wayward woman with her seductive words,
17 who has left the partner of her youth
    and ignored the covenant she made before God.[a](T)
18 Surely her house leads down to death
    and her paths to the spirits of the dead.(U)
19 None who go to her return
    or attain the paths of life.(V)

20 Thus you will walk in the ways of the good
    and keep to the paths of the righteous.
21 For the upright will live in the land,(W)
    and the blameless will remain in it;
22 but the wicked(X) will be cut off from the land,(Y)
    and the unfaithful will be torn from it.(Z)

Footnotes

  1. Proverbs 2:17 Or covenant of her God