Miyambo 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Ubwino Wanzeru
2 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga
ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru
ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu
inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva
ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;
ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,
ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.
Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.
Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,
kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,
kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;
kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,
kwa anthu amabodza,
13 amene amasiya njira zolungama
namayenda mʼnjira zamdima,
14 amene amakondwera pochita zoyipa
namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,
ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;
kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake
ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;
njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera
kapena kupezanso njira zamoyo.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,
uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko
ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,
ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Proverbs 2
New International Version
Moral Benefits of Wisdom
2 My son,(A) if you accept my words
and store up my commands within you,
2 turning your ear to wisdom
and applying your heart to understanding(B)—
3 indeed, if you call out for insight(C)
and cry aloud for understanding,
4 and if you look for it as for silver
and search for it as for hidden treasure,(D)
5 then you will understand the fear of the Lord
and find the knowledge of God.(E)
6 For the Lord gives wisdom;(F)
from his mouth come knowledge and understanding.(G)
7 He holds success in store for the upright,
he is a shield(H) to those whose walk is blameless,(I)
8 for he guards the course of the just
and protects the way of his faithful ones.(J)
9 Then you will understand(K) what is right and just
and fair—every good path.
10 For wisdom will enter your heart,(L)
and knowledge will be pleasant to your soul.
11 Discretion will protect you,
and understanding will guard you.(M)
12 Wisdom will save(N) you from the ways of wicked men,
from men whose words are perverse,
13 who have left the straight paths
to walk in dark ways,(O)
14 who delight in doing wrong
and rejoice in the perverseness of evil,(P)
15 whose paths are crooked(Q)
and who are devious in their ways.(R)
16 Wisdom will save you also from the adulterous woman,(S)
from the wayward woman with her seductive words,
17 who has left the partner of her youth
and ignored the covenant she made before God.[a](T)
18 Surely her house leads down to death
and her paths to the spirits of the dead.(U)
19 None who go to her return
or attain the paths of life.(V)
Footnotes
- Proverbs 2:17 Or covenant of her God
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.