Add parallel Print Page Options

14 Mkazi wanzeru amamanga banja lake,
    koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.

Amene amayenda molungama amaopa Yehova,
    koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.

Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana,
    koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.

Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya,
    koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.

Mboni yokhulupirika sinama,
    koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.

Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza,
    koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.

Khala kutali ndi munthu wopusa
    chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.

Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake.
    Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.

Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo,
    koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.

10 Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake,
    ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.

11 Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka,
    koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.

12 Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu,
    koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.

13 Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa,
    ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.

14 Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake,
    koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.

15 Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse,
    koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.

16 Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa,
    koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.

17 Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru,
    ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.

18 Anthu opusa amalandira uchitsiru,
    koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.

19 Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino,
    ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.

20 Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda,
    koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.

21 Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa
    koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.

22 Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera?
    Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.

23 Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu,
    koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.

24 Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe,
    koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.

25 Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo,
    koma mboni yabodza imaphetsa.

26 Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira
    ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.

27 Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo,
    kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.

28 Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu,
    koma popanda anthu kalonga amawonongeka.

29 Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri,
    koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.

30 Mtima wodekha umapatsa thupi moyo,
    koma nsanje imawoletsa mafupa.

31 Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake,
    koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.

32 Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe,
    koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.

33 Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu,
    koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.

34 Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu,
    koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.

35 Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru,
    koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

14 The wise woman builds her house,(A)
    but with her own hands the foolish one tears hers down.

Whoever fears the Lord walks uprightly,
    but those who despise him are devious in their ways.

A fool’s mouth lashes out with pride,(B)
    but the lips of the wise protect them.(C)

Where there are no oxen, the manger is empty,
    but from the strength of an ox(D) come abundant harvests.

An honest witness does not deceive,
    but a false witness pours out lies.(E)

The mocker seeks wisdom and finds none,
    but knowledge comes easily to the discerning.(F)

Stay away from a fool,
    for you will not find knowledge on their lips.

The wisdom of the prudent is to give thought to their ways,(G)
    but the folly of fools is deception.(H)

Fools mock at making amends for sin,
    but goodwill is found among the upright.

10 Each heart knows its own bitterness,
    and no one else can share its joy.

11 The house of the wicked will be destroyed,(I)
    but the tent of the upright will flourish.(J)

12 There is a way that appears to be right,(K)
    but in the end it leads to death.(L)

13 Even in laughter(M) the heart may ache,
    and rejoicing may end in grief.

14 The faithless will be fully repaid for their ways,(N)
    and the good rewarded for theirs.(O)

15 The simple believe anything,
    but the prudent give thought to their steps.(P)

16 The wise fear the Lord and shun evil,(Q)
    but a fool(R) is hotheaded and yet feels secure.

17 A quick-tempered person(S) does foolish things,(T)
    and the one who devises evil schemes is hated.(U)

18 The simple inherit folly,
    but the prudent are crowned with knowledge.

19 Evildoers will bow down in the presence of the good,
    and the wicked at the gates of the righteous.(V)

20 The poor are shunned even by their neighbors,
    but the rich have many friends.(W)

21 It is a sin to despise one’s neighbor,(X)
    but blessed is the one who is kind to the needy.(Y)

22 Do not those who plot evil go astray?(Z)
    But those who plan what is good find[a] love and faithfulness.

23 All hard work brings a profit,
    but mere talk leads only to poverty.

24 The wealth of the wise is their crown,
    but the folly of fools yields folly.(AA)

25 A truthful witness saves lives,
    but a false witness is deceitful.(AB)

26 Whoever fears the Lord has a secure fortress,(AC)
    and for their children it will be a refuge.(AD)

27 The fear of the Lord is a fountain of life,(AE)
    turning a person from the snares of death.(AF)

28 A large population is a king’s glory,
    but without subjects a prince is ruined.(AG)

29 Whoever is patient has great understanding,(AH)
    but one who is quick-tempered displays folly.(AI)

30 A heart at peace gives life to the body,
    but envy rots the bones.(AJ)

31 Whoever oppresses the poor shows contempt for their Maker,(AK)
    but whoever is kind to the needy honors God.(AL)

32 When calamity comes, the wicked are brought down,(AM)
    but even in death the righteous seek refuge in God.(AN)

33 Wisdom reposes in the heart of the discerning(AO)
    and even among fools she lets herself be known.[b]

34 Righteousness exalts a nation,(AP)
    but sin condemns any people.

35 A king delights in a wise servant,
    but a shameful servant arouses his fury.(AQ)

Footnotes

  1. Proverbs 14:22 Or show
  2. Proverbs 14:33 Hebrew; Septuagint and Syriac discerning / but in the heart of fools she is not known