Add parallel Print Page Options

13 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,
    koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.

Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,
    koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.

Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,
    koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.

Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,
    koma munthu wakhama adzalemera.

Munthu wolungama amadana ndi zabodza,
    koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.

Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,
    koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.

Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;
    munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.

Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,
    koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.

Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,
    koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.

10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,
    koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.

11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono
    koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.

12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,
    koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.

13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,
    koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.

14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;
    amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.

15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,
    koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.

16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,
    koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.

17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,
    koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.

18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,
    koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.

19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,
    koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.

20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;
    koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.

21 Choyipa chitsata mwini,
    koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.

22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,
    koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.

23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,
    koma anthu opanda chilungamo amachilanda.

24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,
    koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.

25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,
    koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

13 A wise son heeds his father’s instruction,
    but a mocker does not respond to rebukes.(A)

From the fruit of their lips people enjoy good things,(B)
    but the unfaithful have an appetite for violence.

Those who guard their lips(C) preserve their lives,(D)
    but those who speak rashly will come to ruin.(E)

A sluggard’s appetite is never filled,(F)
    but the desires of the diligent are fully satisfied.

The righteous hate what is false,(G)
    but the wicked make themselves a stench
    and bring shame on themselves.

Righteousness guards the person of integrity,
    but wickedness overthrows the sinner.(H)

One person pretends to be rich, yet has nothing;(I)
    another pretends to be poor, yet has great wealth.(J)

A person’s riches may ransom their life,
    but the poor cannot respond to threatening rebukes.(K)

The light of the righteous shines brightly,
    but the lamp of the wicked is snuffed out.(L)

10 Where there is strife, there is pride,
    but wisdom is found in those who take advice.(M)

11 Dishonest money dwindles away,(N)
    but whoever gathers money little by little makes it grow.

12 Hope deferred makes the heart sick,
    but a longing fulfilled is a tree of life.(O)

13 Whoever scorns instruction will pay for it,(P)
    but whoever respects(Q) a command is rewarded.(R)

14 The teaching of the wise is a fountain of life,(S)
    turning a person from the snares of death.(T)

15 Good judgment wins favor,
    but the way of the unfaithful leads to their destruction.[a]

16 All who are prudent act with[b] knowledge,
    but fools expose(U) their folly.(V)

17 A wicked messenger falls into trouble,(W)
    but a trustworthy envoy brings healing.(X)

18 Whoever disregards discipline comes to poverty and shame,(Y)
    but whoever heeds correction is honored.(Z)

19 A longing fulfilled is sweet to the soul,(AA)
    but fools detest turning from evil.

20 Walk with the wise and become wise,
    for a companion of fools suffers harm.(AB)

21 Trouble pursues the sinner,(AC)
    but the righteous(AD) are rewarded with good things.(AE)

22 A good person leaves an inheritance for their children’s children,
    but a sinner’s wealth is stored up for the righteous.(AF)

23 An unplowed field produces food for the poor,
    but injustice sweeps it away.

24 Whoever spares the rod(AG) hates their children,
    but the one who loves their children is careful to discipline(AH) them.(AI)

25 The righteous eat to their hearts’ content,
    but the stomach of the wicked goes hungry.(AJ)

Footnotes

  1. Proverbs 13:15 Septuagint and Syriac; the meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
  2. Proverbs 13:16 Or prudent protect themselves through