Miyambo 13
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
13 Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,
koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,
koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,
koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,
koma munthu wakhama adzalemera.
5 Munthu wolungama amadana ndi zabodza,
koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,
koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;
munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,
koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,
koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,
koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono
koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,
koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,
koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;
amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,
koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,
koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,
koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,
koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,
koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;
koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Choyipa chitsata mwini,
koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,
koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,
koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,
koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,
koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.
Proverbs 13
Holman Christian Standard Bible
13 A wise son responds to his father’s discipline,
but a mocker doesn’t listen to rebuke.
2 From the words of his mouth,
a man will enjoy good things,(A)
but treacherous people have an appetite for violence.(B)
3 The one who guards his mouth protects his life;(C)
the one who opens his lips invites his own ruin.(D)
4 The slacker craves, yet has nothing,
but the diligent is fully satisfied.(E)
5 The righteous hate lying,
but the wicked act disgustingly and disgracefully.
7 One man pretends to be rich but has nothing;(G)
another pretends to be poor but has great wealth.(H)
8 Riches are a ransom for a man’s life,(I)
but a poor man hears no threat.
10 Arrogance leads to nothing but strife,(L)
but wisdom is gained by those who take advice.
11 Wealth obtained by fraud will dwindle,(M)
but whoever earns it through labor[b] will multiply it.(N)
12 Delayed hope makes the heart sick,
but fulfilled desire is a tree of life.(O)
13 The one who has contempt for instruction will pay the penalty,(P)
but the one who respects a command will be rewarded.(Q)
14 A wise man’s instruction is a fountain of life,(R)
turning people away from the snares of death.(S)
16 Every sensible person acts knowledgeably,
but a fool displays his stupidity.(U)
17 A wicked messenger falls into trouble,
but a trustworthy courier brings healing.(V)
18 Poverty and disgrace come to those
who ignore discipline,
but the one who accepts correction will be honored.(W)
19 Desire fulfilled is sweet to the taste,
but to turn from evil(X)
is an abomination to fools.
20 The one who walks with the wise will become wise,
but a companion of fools will suffer harm.
21 Disaster pursues sinners,
but good rewards the righteous.(Y)
22 A good man leaves an inheritance to his[d] grandchildren,
but the sinner’s wealth is stored up for the righteous.(Z)
23 The uncultivated field of the poor yields abundant food,
but without justice, it is swept away.
24 The one who will not use the rod hates his son,(AA)
but the one who loves him disciplines him diligently.(AB)
25 A righteous man eats until he is satisfied,
but the stomach of the wicked is empty.(AC)
Footnotes
- Proverbs 13:6 Lit guards integrity of way
- Proverbs 13:11 Lit whoever gathers upon [his] hand
- Proverbs 13:15 LXX, Syr, Tg read treacherous will perish
- Proverbs 13:22 Or inheritance: his
Proverbios 13
Dios Habla Hoy
13 El hijo sabio acepta la corrección del padre;
el insolente no hace caso de reprensiones.
2 Cada uno recoge el fruto de lo que dice,
pero los traidores tienen hambre de violencia.
3 Cuidar las palabras es cuidarse uno mismo;
el que habla mucho se arruina solo.
4 El perezoso desea y no consigue;
el que trabaja, prospera.
5 El hombre justo odia la mentira;
el malvado es motivo de vergüenza y deshonra.
6 La rectitud protege al hombre intachable;
la maldad destruye al pecador.
7 Hay quienes no tienen nada y presumen de ricos,
y hay quienes todo lo tienen y aparentan ser pobres.
8 La riqueza del rico le salva la vida;
el pobre jamás escucha amenazas.
9 Los justos son como una luz brillante;
los malvados, como lámpara que se apaga.
10 El orgullo sólo provoca peleas;
la sabiduría está con los humildes.
11 La riqueza ilusoria, disminuye;
el que la junta poco a poco, la aumenta.
12 Esperanza frustrada, corazón afligido,
pero el deseo cumplido es como un árbol de vida.
13 El que desatiende una orden, lo lamentará;
el que respeta el mandato será recompensado.
14 La enseñanza del sabio es fuente de vida
y libra de los lazos de la muerte.
15 El buen juicio se gana el aprecio,
pero los traidores marchan a su ruina.
16 El que es prudente actúa con inteligencia,
pero el necio hace gala de su necedad.
17 El mensajero malvado acarrea problemas,
pero el mensajero fiel los alivia.
18 Pobreza y deshonra tendrá quien desprecia el consejo;
grandes honores, quien atiende la corrección.
19 El deseo cumplido es causa de alegría.
Los necios no soportan alejarse del mal.
20 Júntate con sabios y obtendrás sabiduría;
júntate con necios y te echarás a perder.
21 Los pecadores son perseguidos por el mal;
los justos, recompensados con el bien.
22 El hombre bueno deja herencia a sus nietos;
el pecador amasa fortunas que serán del justo.
23 En el campo del pobre hay comida abundante,
pero mucho se pierde donde no hay justicia.
24 Quien no corrige a su hijo, no lo quiere;
el que lo ama, lo corrige.
25 El justo come hasta estar satisfecho,
pero el malvado se queda con hambre.
Proverbs 13
King James Version
13 A wise son heareth his father's instruction: but a scorner heareth not rebuke.
2 A man shall eat good by the fruit of his mouth: but the soul of the transgressors shall eat violence.
3 He that keepeth his mouth keepeth his life: but he that openeth wide his lips shall have destruction.
4 The soul of the sluggard desireth, and hath nothing: but the soul of the diligent shall be made fat.
5 A righteous man hateth lying: but a wicked man is loathsome, and cometh to shame.
6 Righteousness keepeth him that is upright in the way: but wickedness overthroweth the sinner.
7 There is that maketh himself rich, yet hath nothing: there is that maketh himself poor, yet hath great riches.
8 The ransom of a man's life are his riches: but the poor heareth not rebuke.
9 The light of the righteous rejoiceth: but the lamp of the wicked shall be put out.
10 Only by pride cometh contention: but with the well advised is wisdom.
11 Wealth gotten by vanity shall be diminished: but he that gathereth by labour shall increase.
12 Hope deferred maketh the heart sick: but when the desire cometh, it is a tree of life.
13 Whoso despiseth the word shall be destroyed: but he that feareth the commandment shall be rewarded.
14 The law of the wise is a fountain of life, to depart from the snares of death.
15 Good understanding giveth favour: but the way of transgressors is hard.
16 Every prudent man dealeth with knowledge: but a fool layeth open his folly.
17 A wicked messenger falleth into mischief: but a faithful ambassador is health.
18 Poverty and shame shall be to him that refuseth instruction: but he that regardeth reproof shall be honoured.
19 The desire accomplished is sweet to the soul: but it is abomination to fools to depart from evil.
20 He that walketh with wise men shall be wise: but a companion of fools shall be destroyed.
21 Evil pursueth sinners: but to the righteous good shall be repayed.
22 A good man leaveth an inheritance to his children's children: and the wealth of the sinner is laid up for the just.
23 Much food is in the tillage of the poor: but there is that is destroyed for want of judgment.
24 He that spareth his rod hateth his son: but he that loveth him chasteneth him betimes.
25 The righteous eateth to the satisfying of his soul: but the belly of the wicked shall want.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Copyright © 1999, 2000, 2002, 2003, 2009 by Holman Bible Publishers, Nashville Tennessee. All rights reserved.
Dios habla hoy ®, © Sociedades Bíblicas Unidas, 1966, 1970, 1979, 1983, 1996.