Miyambo 23
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
23 Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira,
uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 ngati ndiwe munthu wadyera
udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Usasirire zakudya zake,
pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma,
ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo.
Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi
ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Usadye chakudya cha munthu waumbombo,
usalakalake zakudya zake zokoma;
7 paja iye ndi munthu amene
nthawi zonse amaganizira za mtengo wake
ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,”
koma sakondweretsedwa nawe.
8 Udzasanza zimene wadyazo
ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Usayankhule munthu wopusa akumva,
pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale
kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;
iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Mtima wako uzikhala pa malangizo
ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Usaleke kumulangiza mwana;
ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Ukamukwapula ndi tsatsa
udzapulumutsa moyo wake.
15 Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru,
inenso mtima wanga udzakondwera.
16 Mtima wanga udzakondwera
pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa,
koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Ndithu za mʼtsogolo zilipo
ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru,
mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera
kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi
ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Mvera abambo ako amene anakubala,
usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Gula choonadi ndipo usachigulitse;
ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu;
Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Abambo ndi amayi ako asangalale;
amene anakubereka akondwere!
26 Mwana wanga, undikhulupirire
ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama;
ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Amabisala ngati mbala yachifwamba,
ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni?
Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo?
Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 Ndi amene amakhalitsa pa mowa,
amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo,
pamene akuwira mʼchikho
pamene akumweka bwino!
32 Potsiriza pake amaluma ngati njoka,
ndipo amajompha ngati mphiri.
33 Maso ako adzaona zinthu zachilendo
ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja,
kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe!
Andimenya koma sindinamve kanthu!
Kodi ndidzuka nthawi yanji?
Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”
Proverbs 23
New International Version
Saying 7
23 When you sit to dine with a ruler,
note well what[a] is before you,
2 and put a knife to your throat
if you are given to gluttony.
3 Do not crave his delicacies,(A)
for that food is deceptive.
Saying 8
4 Do not wear yourself out to get rich;
do not trust your own cleverness.
5 Cast but a glance at riches, and they are gone,(B)
for they will surely sprout wings
and fly off to the sky like an eagle.(C)
Saying 9
6 Do not eat the food of a begrudging host,
do not crave his delicacies;(D)
7 for he is the kind of person
who is always thinking about the cost.[b]
“Eat and drink,” he says to you,
but his heart is not with you.
8 You will vomit up the little you have eaten
and will have wasted your compliments.
Saying 10
9 Do not speak to fools,
for they will scorn your prudent words.(E)
Saying 11
10 Do not move an ancient boundary stone(F)
or encroach on the fields of the fatherless,
11 for their Defender(G) is strong;(H)
he will take up their case against you.(I)
Saying 12
12 Apply your heart to instruction(J)
and your ears to words of knowledge.
Saying 13
13 Do not withhold discipline from a child;
if you punish them with the rod, they will not die.
14 Punish them with the rod
and save them from death.(K)
Saying 14
15 My son, if your heart is wise,
then my heart will be glad indeed;
16 my inmost being will rejoice
when your lips speak what is right.(L)
Saying 15
17 Do not let your heart envy(M) sinners,
but always be zealous for the fear of the Lord.
18 There is surely a future hope for you,
and your hope will not be cut off.(N)
Saying 16
19 Listen, my son,(O) and be wise,
and set your heart on the right path:
20 Do not join those who drink too much wine(P)
or gorge themselves on meat,
21 for drunkards and gluttons become poor,(Q)
and drowsiness clothes them in rags.
Saying 17
22 Listen to your father, who gave you life,
and do not despise your mother when she is old.(R)
23 Buy the truth and do not sell it—
wisdom, instruction and insight as well.(S)
24 The father of a righteous child has great joy;
a man who fathers a wise son rejoices in him.(T)
25 May your father and mother rejoice;
may she who gave you birth be joyful!(U)
Saying 18
26 My son,(V) give me your heart
and let your eyes delight in my ways,(W)
27 for an adulterous woman is a deep pit,(X)
and a wayward wife is a narrow well.
28 Like a bandit she lies in wait(Y)
and multiplies the unfaithful among men.
Saying 19
29 Who has woe? Who has sorrow?
Who has strife? Who has complaints?
Who has needless bruises? Who has bloodshot eyes?
30 Those who linger over wine,(Z)
who go to sample bowls of mixed wine.
31 Do not gaze at wine when it is red,
when it sparkles in the cup,
when it goes down smoothly!
32 In the end it bites like a snake
and poisons like a viper.
33 Your eyes will see strange sights,
and your mind will imagine confusing things.
34 You will be like one sleeping on the high seas,
lying on top of the rigging.
35 “They hit me,” you will say, “but I’m not hurt!
They beat me, but I don’t feel it!
When will I wake up
so I can find another drink?”(AA)
Footnotes
- Proverbs 23:1 Or who
- Proverbs 23:7 Or for as he thinks within himself, / so he is; or for as he puts on a feast, / so he is
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.