Mika 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa
3 Ndipo ine ndinati,
“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,
inu olamulira nyumba ya Israeli.
Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;
inu amene mumasenda khungu la anthu anga,
ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
3 inu amene mumadya anthu anga,
mumasenda khungu lawo
ndi kuphwanya mafupa awo;
inu amene mumawadula nthulinthuli
ngati nyama yokaphika?”
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova,
koma Iye sadzawayankha.
Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake
chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
5 Yehova akuti,
“Aneneri amene
amasocheretsa anthu anga,
ngati munthu wina awapatsa chakudya
amamufunira ‘mtendere;’
ngati munthu wina sawapatsa zakudya
amamulosera zoyipa.
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani,
simudzaonanso masomphenya,
mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.
Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
7 Alosi adzachita manyazi
ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.
Onse adzaphimba nkhope zawo
chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,
ndi Mzimu wa Yehova,
ndi kulungama, ndi kulimba mtima,
kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,
kwa Israeli za tchimo lake.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,
inu olamulira nyumba ya Israeli,
inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;
ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,
ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,
ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,
ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.
Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,
“Kodi Yehova sali pakati pathu?
Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
12 Choncho chifukwa cha inu,
Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,
Yerusalemu adzasanduka bwinja,
ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
Michoh 3
Orthodox Jewish Bible
3 And I said, Hear, O Rashei Ya’akov, and ye Ketzinim of Bais Yisroel. Is it not for you to have da’as of Mishpat (Justice)?
2 Who hate the tov, and love the rah; who tear off their skin from off them, and their flesh from off their atzamot (bones);
3 Who also eat the flesh of Ami, and flay their skin from off them; and they break their atzamot, and chop them in pieces, like for the pot, and like the basar within the caldron.
4 Then shall they cry unto Hashem, but He will not hear them; He will even hide His face from them at that time, because of the evil way they behaved themselves in their doings.
5 Thus saith Hashem concerning the nevi’im that make Ami err, leading them astray, the nevi’im that bite with their teeth, and preach, Shalom! And whoever putteth nothing into their mouths, v’kiddeshu milchamah (they sanctify war) against him.
6 Therefore lailah shall be unto you, because of the chazon; and choshech shall come upon you because of the soothsaying, the divination; and the shemesh shall go down over the nevi’im, and hayom shall be dark over them.
7 Then shall the chozim (seers) be ashamed, and the kosemim (diviners) blush in bushah; yea, they shall all cover their safam (mustache, i.e., their lips); ki ein ma’aneh Elohim (for there is no answer of G-d).
8 But truly I am full of ko’ach by the Ruach [Hakodesh] of Hashem, and of mishpat, and of gevurah (might), to preach unto Ya’akov his peysha, and to Yisroel his chattat. [Yeshayah 53:5,8,12]
9 Hear this, I pray you, ye Rashei Bais Ya’akov, and Ketzinim of Bais Yisroel, that abhor mishpat, and twist kol haYesharah (all the right, the straight).
10 Boneh Tziyon b’damim (they build up Tziyon with blood), and Yerushalayim with avlah (iniquity).
11 Her Rashim judge for a bribe, and her kohanim play the hireling moreh (teacher), and her nevi’im are fortunetellers for kesef; yet will they lean upon Hashem? And say, Is not Hashem among us? No ra’ah will come upon us.
12 Therefore because of you, Tziyon shall be plowed as a sadeh, and Yerushalayim shall become a rubble heap, and the Har HaBeis (HaMikdash, i.e., the Temple Mount) shall become a mound of scrubs. [T.N. fulfilled 586, B.C.E., 70 C.E.]
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Copyright © 2002, 2003, 2008, 2010, 2011 by Artists for Israel International