Mateyu 19
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Za Kuthetsa Ukwati
19 Yesu atatsiriza kunena zinthu zimenezi, anachoka ku Galileya ndi kupita ku chigawo cha Yudeya mbali ina ya mtsinje wa Yorodani. 2 Magulu akulu a anthu anamutsatira Iye, ndipo iwo anachiritsidwa pomwepo.
3 Afarisi ena anabwera kwa Iye kudzamuyesa. Anamufunsa Iye nati, “Kodi ndikololedwa kuti mwamuna amuleke mkazi wake pa chifukwa china chilichonse?”
4 Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge kuti pachiyambi Mulungu analenga iwo, ‘mwamuna ndi mkazi?’ 5 Ndipo anati, ‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ 6 Motero salinso awiri ayi koma mmodzi. Nʼchifukwa chake chimene Mulungu wachimanga pamodzi munthu wina asachilekanitse.”
7 Ndipo iwo anamufunsa nati, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mose analamula kuti mwamuna azipatsa mkazi wake kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa?”
8 Yesu anayankha kuti, “Mose anakulolezani kuti muzisudzula akazi anu chifukwa cha kuwuma mitima kwanu. Koma sizinali chotere kuyambira pachiyambi. 9 Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake, osati chifukwa cha chiwerewere nakakwatira mkazi wina, achita chigololo.”
10 Ophunzira ake anati kwa Iye, “Ngati umu ndi mmene zilili pa mwamuna ndi mkazi, kuli bwino kusakwatira.”
11 Yesu anayankha kuti, “Si aliyense amene angavomere chiphunzitso ichi, koma kwa okhawo amene achimvetsetsa. 12 Pakuti ena ndi akuti sangakwatire chifukwa anabadwa motero, ena ali motero chifukwa chofulidwa ndi anthu ndipo ena anawukana ukwati chifukwa cha ufumu wakumwamba. Iye amene angalandire ichi alandire.”
Yesu Adalitsa Ana
13 Pamenepo anabwera nawo ana kwa Yesu kuti awasanjike manja ndi kuwapempherera. Koma ophunzira ake anadzudzula amene anabweretsa anawo.
14 Yesu anati, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse pakuti ufumu wakumwamba ndi wa iwo onga anawa.” 15 Atasanjika manja ake pa anawo, anachokapo.
Mnyamata Wolemera ndi Ufumu wa Mulungu
16 Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?”
17 Yesu anayankha kuti, “Ukundifunsiranji Ine za chinthu chimene ndi chabwino? Pali mmodzi yekha amene ndi wabwino. Ngati ukufuna kulowa mʼmoyo wosatha mvera malamulo.”
18 Mnyamatayo anamufunsa kuti, “Ndi ati?”
Yesu anayankha kuti, “Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni onama, 19 lemekeza abambo ako ndi amayi ako ndipo konda mnansi wako monga iwe mwini.”
20 Mnyamatayo anati, “Zonsezi ndimazisunga, nanga chatsala ndi chiyani?”
21 Yesu anayankha kuti, “Ngati ukufuna kukhala wangwiro, pita kagulitse katundu wako ndi kupereka kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ukakachita zimenezi, ukabwere udzanditsate Ine.”
22 Mnyamatayo atamva zimenezi, anachoka mokhumudwa, chifukwa anali ndi chuma chambiri.
23 Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti nʼkovuta kuti olemera akalowe mu ufumu wakumwamba. 24 Komanso ndikuwuzani kuti, nʼkwapafupi kuti ngamira idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi kuti wolemera akalowe mu ufumu wa Mulungu.”
25 Ophunzira atamva zimenezi, anadabwa kwambiri ndipo anamufunsa kuti, “Nanga angapulumuke ndani?”
26 Yesu anawayangʼana iwo nati, “Ndi anthu, izi nʼzosatheka, koma ndi Mulungu zinthu zonse zimatheka.”
27 Petro anamuyankha Iye kuti, “Ife tinasiya zonse ndi kukutsatirani Inu! Nanga tsono ife tidzalandira chiyani?”
28 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti pa nthawi yokonzanso zinthu zonse, pamene Mwana wa Munthu adzakhala pa mpando wake waufumu mu ulemerero wake kumwamba, inu amene mwanditsata Ine mudzakhalanso pa mipando khumi ndi iwiri yaufumu, kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli. 29 Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. 30 Koma ambiri amene ali oyambirira adzakhala omalizira, ndipo ambiri amene ndi omalizira adzakhala oyambirira.”
Matthew 19
Living Bible
19 After Jesus had finished this address, he left Galilee and circled back to Judea from across the Jordan River. 2 Vast crowds followed him, and he healed their sick. 3 Some Pharisees came to interview him and tried to trap him into saying something that would ruin him.
“Do you permit divorce?” they asked.
4 “Don’t you read the Scriptures?” he replied. “In them it is written that at the beginning God created man and woman, 5-6 and that a man should leave his father and mother, and be forever united to his wife. The two shall become one—no longer two, but one! And no man may divorce what God has joined together.”
7 “Then, why,” they asked, “did Moses say a man may divorce his wife by merely writing her a letter of dismissal?”
8 Jesus replied, “Moses did that in recognition of your hard and evil hearts, but it was not what God had originally intended. 9 And I tell you this, that anyone who divorces his wife, except for fornication, and marries another, commits adultery.”[a]
10 Jesus’ disciples then said to him, “If that is how it is, it is better not to marry!”
11 “Not everyone can accept this statement,” Jesus said. “Only those whom God helps. 12 Some are born without the ability to marry,[b] and some are disabled by men, and some refuse to marry for the sake of the Kingdom of Heaven. Let anyone who can, accept my statement.”
13 Little children were brought for Jesus to lay his hands on them and pray. But the disciples scolded those who brought them. “Don’t bother him,” they said.
14 But Jesus said, “Let the little children come to me, and don’t prevent them. For of such is the Kingdom of Heaven.” 15 And he put his hands on their heads and blessed them before he left.
16 Someone came to Jesus with this question: “Good master, what must I do to have eternal life?”
17 “When you call me good you are calling me God,” Jesus replied, “for God alone is truly good.[c] But to answer your question, you can get to heaven if you keep the commandments.”
18 “Which ones?” the man asked.
And Jesus replied, “Don’t kill, don’t commit adultery, don’t steal, don’t lie, 19 honor your father and mother, and love your neighbor as yourself!”
20 “I’ve always obeyed every one of them,” the youth replied. “What else must I do?”
21 Jesus told him, “If you want to be perfect, go and sell everything you have and give the money to the poor, and you will have treasure in heaven; and come, follow me.” 22 But when the young man heard this, he went away sadly, for he was very rich.
23 Then Jesus said to his disciples, “It is almost impossible for a rich man to get into the Kingdom of Heaven. 24 I say it again—it is easier for a camel to go through the eye of a needle than for a rich man to enter the Kingdom of God!”
25 This remark confounded the disciples. “Then who in the world can be saved?” they asked.
26 Jesus looked at them intently and said, “Humanly speaking, no one. But with God, everything is possible.”
27 Then Peter said to him, “We left everything to follow you. What will we get out of it?”
28 And Jesus replied, “When I, the Messiah,[d] shall sit upon my glorious throne in the Kingdom, you my disciples shall certainly sit on twelve thrones judging the twelve tribes of Israel. 29 And anyone who gives up his home, brothers, sisters, father, mother, wife,[e] children, or property, to follow me, shall receive a hundred times as much in return, and shall have eternal life. 30 But many who are first now will be last then; and some who are last now will be first then.”
Footnotes
- Matthew 19:9 “And the man who marries a divorced woman commits adultery.” This sentence is added in some ancient manuscripts.
- Matthew 19:12 born without the ability to marry, literally, “born eunuchs,” or “born emasculated.”
- Matthew 19:17 for God alone is truly good, implied from Luke 18:19.
- Matthew 19:28 the Messiah, literally, “the Son of Man.” in the Kingdom, literally, “in the regeneration.”
- Matthew 19:29 wife, omitted here in many manuscripts but included in Luke 18:29.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The Living Bible copyright © 1971 by Tyndale House Foundation. Used by permission of Tyndale House Publishers Inc., Carol Stream, Illinois 60188. All rights reserved.