Mateyu 9
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Munthu Wakufa Ziwalo wa ku Kaperenawo
9 Yesu analowa mʼbwato nawoloka, ndipo anabwera ku mudzi wa kwawo. 2 Amuna ena anabwera ndi munthu wakufa ziwalo kwa Iye atamugoneka pa mphasa. Yesu ataona chikhulupiriro chawo anati kwa wakufa ziwaloyo, “Limba mtima mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”
3 Pamenepo aphunzitsi ena amalamulo anaganiza mu mtima mwawo kuti, “Munthu uyu akuchitira Mulungu mwano.”
4 Ndipo podziwa maganizo awo Yesu anati, “Bwanji mukuganiza zoyipa mʼmitima mwanu? 5 Chapafupi ndi chiti kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa’ kapena kunena kuti, ‘Imirira ndipo yenda?’ 6 Tsono kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko wokhululuka machimo, pamenepo anati kwa wakufa ziwaloyo, ‘Imirira, tenga mphasa yako kazipita kwanu.’ ” 7 Ndipo munthuyo anayimirira napita kwawo. 8 Gulu la anthu litaona izi, linadzazidwa ndi mantha ndipo linalemekeza Mulungu amene anapereka ulamuliro kwa anthu.
Kuyitanidwa kwa Mateyu
9 Ndipo Yesu atachoka kumeneko, anaona munthu wina dzina lake Mateyu, atakhala mʼnyumba ya msonkho. Anati kwa iye, “Nditsate Ine.” Ndipo iye ananyamuka namutsata.
10 Ndipo pamene Iye ankadya mʼnyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anabwera nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake. 11 Ndipo Afarisi poona izi, anati kwa ophunzira ake, “Nʼchifukwa chiyani Aphunzitsi anu akudya pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
12 Yesu atamva, anati, “Munthu wamoyo safuna singʼanga ayi, koma wodwala. 13 Koma pitani kaphunzireni tanthauzo la mawu awa: ‘Ndimafuna chifundo osati nsembe ayi.’ Pakuti sindinabwere kudzayitana olungama koma ochimwa.”
Za Kusala Kudya
14 Ndipo ophunzira a Yohane anabwera namufunsa Iye kuti, “Bwanji ife ndi Afarisi timasala kudya koma ophunzira anu sasala kudya?”
15 Yesu anayankha kuti, “Kodi oyitanidwa ku ukwati angamalire bwanji pamene mkwati ali naye pamodzi? Nthawi idzafika pamene mkwatiyo adzachotsedwa ndi pamene adzasala kudya.”
16 Ndipo palibe munthu amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale chifukwa chigambacho chidzachoka ndipo chibowocho chidzakula kuposa kale. 17 Kapena sathira vinyo watsopano mʼmatumba akale; akatero, matumba akalewo adzaphulika ndipo vinyoyo adzatayika, matumbawo adzawonongeka; satero ayi. Amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso ndipo zonse zimasungika.
Za Mwana Wamkazi wa Yairo ndi Mayi Wokhudza Chovala cha Yesu
18 Pamene ankanena zimenezi, mkulu wa sunagoge anabwera namugwadira Iye nati, “Mwana wanga wamkazi wamwalira posachedwapa koma tiyeni mukasanjike dzanja lanu pa iye ndipo adzakhala ndi moyo.” 19 Yesu ndi ophunzira ake ananyamuka napita naye pamodzi.
20 Panali mayi wina amene ankadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri ndipo anadza mʼmbuyo mwake nakhudza mkanjo wake. 21 Iyeyo anati mwa iye yekha, “Nditangokhudza kasonga ka mkanjo wake, ine ndidzachiritsidwa.”
22 Ndipo Yesu anatembenuka namuona mayiyo nati, “Limbani mtima mayi iwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.” Nthawi yomweyo mayiyo anachiritsidwa.
23 Yesu atalowa mʼnyumba ya mkulu wa sunagoge ndi kuona oyimba zitoliro ndi gulu la anthu ochita phokoso, 24 anati, “Tulukani, mtsikanayu sanafe koma ali mtulo.” Koma anamuseka Iye. 25 Atangowatulutsa anthuwo, analowa mʼnyumba ndipo anagwira dzanja la mtsikanayo ndipo anauka. 26 Mbiriyi inamveka mʼdera lonse.
Yesu Achiritsa Osaona ndi Osayankhula
27 Yesu atapitirira ulendo wake, amuna awiri osaona anamutsatira Iye, akufuwula kuti, “Tichitireni chifundo, Mwana wa Davide!”
28 Atalowa mʼnyumba, amuna awiri osaonawo anabwera kwa Iye ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukhulupirira kuti ndikhoza kukuchiritsani?”
Iwo anayankha kuti, “Inde Ambuye.”
29 Pomwepo anakhudza maso awo nati, “Zichitike kwa inu monga mwachikhulupiriro chanu.” 30 Ndipo anayamba kuona. Yesu anawachenjeza kwambiri nati, “Onani, wina aliyense asadziwe za zimenezi.” 31 Koma iwo anatuluka mʼnyumbamo nafalitsa za Iye mʼchigawo chonse.
32 Pamene iwo ankatuluka kunja, anthu anabwera kwa Iye ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wosayankhula. 33 Ndipo atatulutsa mzimuwo, munthuyo anayankhula. Gulu la anthuwo linadabwa ndipo linati, “Zinthu zotere sizinaonekepo mu Israeli.”
34 Koma Afarisi anati, “Akutulutsa mizimu yoyipa ndi mphamvu ya mkulu wa ziwanda.”
Antchito ndi Ochepa
35 Yesu anayendayenda mʼmizinda yonse ndi mʼmidzi, kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa nthenda zawo zonse ndi zofowoka za mʼmatupi mwawo. 36 Ataona maguluwo, anagwidwa ndi chisoni chifukwa anali ozunzika ndi osowa chithandizo ngati nkhosa zopanda mʼbusa. 37 Pamenepo anati kwa ophunzira ake, “Zokolola ndi zambiri koma antchito ndi ochepa. 38 Nʼchifukwa chake, pemphani Ambuye mwini zokolola kuti atumize antchito ku munda wake.”
Matthew 9
Christian Standard Bible
The Son of Man Forgives and Heals
9 So he got into a boat, crossed over, and came to his own town.(A) 2 Just then(B) some men[a] brought to him a paralytic lying on a stretcher. Seeing their faith, Jesus told the paralytic, “Have courage, son, your sins are forgiven.”(C)
3 At this, some of the scribes said to themselves, “He’s blaspheming!” (D)
4 Perceiving their thoughts,(E) Jesus said, “Why are you thinking evil things in your hearts?[b] 5 For which is easier: to say, ‘Your sins are forgiven,’ or to say, ‘Get up and walk’? 6 But so that you may know that the Son of Man has authority on earth to forgive sins”—then he told the paralytic, “Get up, take your stretcher, and go home.” 7 So he got up and went home. 8 When the crowds saw this, they were awestruck[c][d] and gave glory(F) to God, who had given such authority to men.
The Call of Matthew
9 As Jesus went on from there,(G) he saw a man named Matthew sitting at the tax office, and he said to him, “Follow me,” and he got up and followed him.(H)
10 While he was reclining at the table in the house, many tax collectors and sinners came to eat with Jesus and his disciples.(I) 11 When the Pharisees saw this, they asked his disciples, “Why does your teacher eat with tax collectors and sinners?” (J)
12 Now when he heard this, he said, “It is not those who are well who need a doctor, but those who are sick.(K) 13 Go and learn what this means: I desire mercy and not sacrifice.[e](L) For I didn’t come to call the righteous, but sinners.”[f]
A Question about Fasting
14 Then John’s disciples came to him, saying, “Why do we and the Pharisees fast often, but your disciples do not fast?” (M)
15 Jesus said to them, “Can the wedding guests[g] be sad while the groom is with them? The time[h] will come when the groom will be taken away from them, and then they will fast. 16 No one patches an old garment with unshrunk cloth, because the patch pulls away from the garment and makes the tear worse. 17 And no one puts[i] new wine into old wineskins. Otherwise, the skins burst, the wine spills out, and the skins are ruined. No, they put new wine into fresh wineskins, and both are preserved.”
A Girl Restored and a Woman Healed
18 As he was telling them these things,(N) suddenly one of the leaders came and knelt down before him, saying, “My daughter just died,[j] but come and lay your hand on her, and she will live.”(O) 19 So Jesus and his disciples got up and followed(P) him.
20 Just then, a woman who had suffered from bleeding for twelve years approached from behind and touched the end of his robe,(Q) 21 for she said to herself, “If I can just touch his robe, I’ll be made well.”[k](R)
22 Jesus turned and saw her. “Have courage, daughter,” he said. “Your faith has saved you.”[l](S) And the woman was made well from that moment.[m]
23 When Jesus came to the leader’s house, he saw the flute players and a crowd lamenting loudly.(T) 24 “Leave,” he said, “because the girl is not dead but asleep.”(U) And they laughed at him. 25 After the crowd had been put outside, he went in and took her by the hand, and the girl got up.(V) 26 Then news of this spread throughout that whole area.(W)
Healing the Blind
27 As Jesus went on from there, two blind men followed him, calling out, “Have mercy on us, Son of David!” (X)
28 When he entered the house, the blind men approached him, and Jesus said to them, “Do you believe(Y) that I can do this?”
They said to him, “Yes, Lord.”
29 Then he touched their eyes, saying, “Let it be done for you according to your faith.” 30 And their eyes were opened. Then Jesus warned them sternly, “Be sure that no one finds out.”(Z) 31 But they went out and spread the news about him throughout that whole area.
Driving Out a Demon
32 Just as they were going out, a demon-possessed man who was unable to speak was brought to him.(AA) 33 When the demon had been driven out, the man who had been mute spoke, and the crowds were amazed, saying, “Nothing like this has ever been seen in Israel!”
34 But the Pharisees said, “He drives out demons by the ruler of the demons.”(AB)
The Lord of the Harvest
35 Jesus continued going around to all the towns and villages, teaching in their synagogues, preaching the good news of the kingdom,(AC) and healing every[n] disease and every sickness.[o][p] 36 When he saw the crowds, he felt compassion for them, because they were distressed and dejected,(AD) like sheep without a shepherd.(AE) 37 Then he said to his disciples,(AF) “The harvest is abundant, but the workers are few. 38 Therefore, pray to the Lord of the harvest to send out workers into his harvest.”
Footnotes
- 9:2 Lit then they
- 9:4 Or minds
- 9:8 Other mss read amazed
- 9:8 Lit afraid
- 9:13 Hs 6:6
- 9:13 Other mss add to repentance
- 9:15 Lit the sons of the bridal chamber
- 9:15 Lit days
- 9:17 Lit And they do not put
- 9:18 Lit daughter has now come to the end
- 9:21 Or be saved
- 9:22 Or has made you well
- 9:22 Lit hour
- 9:35 Or every kind of
- 9:35 Other mss add among the people
- 9:35 Or physical ailment
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The Christian Standard Bible. Copyright © 2017 by Holman Bible Publishers. Used by permission. Christian Standard Bible®, and CSB® are federally registered trademarks of Holman Bible Publishers, all rights reserved.