Add parallel Print Page Options

Yesu Ayesedwa Mʼchipululu

Pambuyo pake Yesu anatsogozedwa ndi Mzimu Woyera kupita ku chipululu kukayesedwa ndi mdierekezi. Ndipo atasala kudya masiku makumi anayi usana ndi usiku, anamva njala. Woyesayo anadza kwa Iye nati, “Ngati ndinu mwana wa Mulungu, sandutsani miyala iyi kuti ikhale buledi.”

Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa, ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha, koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Mulungu.’ ”

Pamenepo mdierekezi anapita naye ku mzinda woyera namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu, dziponyeni nokha pansi. Pakuti kwalembedwa:

“ ‘Adzalamulira angelo ake za iwe,
    ndipo adzakunyamula ndi manja awo
    kuti phazi lako lisagunde pa mwala.’ ”

Yesu anamuyankha kuti, “Kwalembedwanso: ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’ ”

Kenaka mdierekezi anamutengera Yesu ku phiri lalitali kwambiri namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi ndi ulemerero wawo. Ndipo anati kwa Iye, “Zonsezi ndidzakupatsani ngati mutandiweramira ndi kundipembedza ine.”

10 Yesu anati kwa iye, “Choka Satana! Zalembedwa, ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’ ”

11 Pamenepo mdierekezi anamusiya ndipo angelo anamutumikira Iye.

Yesu Ayamba Kulalikira

12 Yesu atamva kuti Yohane anamutsekera mʼndende, anabwerera ku Galileya. 13 Ndipo atachoka ku Nazareti anapita ku Kaperenawo ndi kukhala mʼmbali mwa nyanja, mʼdera la Zebuloni ndi Nafutali; 14 pokwaniritsa zimene zinanenedwa kudzera mwa mneneri Yesaya kuti,

15 “Dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafutali,
    njira ya ku nyanja, kutsidya lija la Yorodani,
    Galileya wa anthu a mitundu ina,
16 anthu okhala mu mdima
    awona kuwala kwakukulu;
ndi kwa iwo okhala mʼdziko la mthunzi wa imfa
    kuwunika kwawafikira.”

17 Kuyambira nthawi imeneyo, Yesu anayamba kulalikira nati, “Tembenukani mtima ufumu wakumwamba wayandikira.”

Yesu Ayitana Ophunzira ake Oyamba

18 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona abale awiri, Simoni wotchedwa Petro ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja popeza anali asodzi. 19 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.” 20 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.

21 Atapita patsogolo, anaona abale ena awiri, Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo. Iwowa anali mʼbwato ndi abambo awo, Zebedayo, akukonza makoka awo ndipo Yesu anawayitana. 22 Nthawi yomweyo anasiya bwato ndi abambo awo namutsata Iye.

Yesu Achiritsa Odwala

23 Yesu anayendayenda mu Galileya kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa matenda onse pakati pa anthu. 24 Mbiri yake yonse inawanda ku Siriya konse ndipo anthu anabweretsa kwa Iye onse amene anali odwala nthenda zosiyanasiyana, womva maululu aakulu, ogwidwa ndi ziwanda, odwala matenda akugwa ndi olumala ndipo Iye anawachiritsa. 25 Magulu ambiri a anthu anachokera ku Galileya, Dekapoli, Yerusalemu, Yudeya ndi ku madera a kutsidya la mtsinje wa Yorodani namutsata Iye.

Satan Tempts Jesus(A)

Then (B)Jesus was led up by (C)the Spirit into the wilderness to be tempted by the devil. And when He had fasted forty days and forty nights, afterward He was hungry. Now when the tempter came to Him, he said, “If You are the Son of God, command that these stones become bread.”

But He answered and said, “It is written, (D)‘Man shall not live by bread alone, but by every word that proceeds from the mouth of God.’

Then the devil took Him up (E)into the holy city, set Him on the pinnacle of the temple, and said to Him, “If You are the Son of God, throw Yourself down. For it is written:

(F)‘He shall give His angels charge over you,’

and,

(G)‘In their hands they shall bear you up,
Lest you dash your foot against a stone.’

Jesus said to him, “It is written again, (H)‘You shall not [a]tempt the Lord your God.’

Again, the devil took Him up on an exceedingly high mountain, and (I)showed Him all the kingdoms of the world and their glory. And he said to Him, “All these things I will give You if You will fall down and worship me.”

10 Then Jesus said to him, [b]“Away with you, Satan! For it is written, (J)‘You shall worship the Lord your God, and Him only you shall serve.’

11 Then the devil (K)left Him, and behold, (L)angels came and ministered to Him.

Jesus Begins His Galilean Ministry(M)

12 (N)Now when Jesus heard that John had been put in prison, He departed to Galilee. 13 And leaving Nazareth, He came and dwelt in Capernaum, which is by the sea, in the regions of Zebulun and Naphtali, 14 that it might be fulfilled which was spoken by Isaiah the prophet, saying:

15 “The(O) land of Zebulun and the land of Naphtali,
By the way of the sea, beyond the Jordan,
Galilee of the Gentiles:
16 (P)The people who sat in darkness have seen a great light,
And upon those who sat in the region and shadow of death
Light has dawned.”

17 (Q)From that time Jesus began to preach and to say, (R)“Repent, for the kingdom of heaven [c]is at hand.”

Four Fishermen Called as Disciples(S)

18 (T)And Jesus, walking by the Sea of Galilee, saw two brothers, Simon (U)called Peter, and Andrew his brother, casting a net into the sea; for they were fishermen. 19 Then He said to them, “Follow Me, and (V)I will make you fishers of men.” 20 (W)They immediately left their nets and followed Him.

21 (X)Going on from there, He saw two other brothers, James the son of Zebedee, and John his brother, in the boat with Zebedee their father, mending their nets. He called them, 22 and immediately they left the boat and their father, and followed Him.

Jesus Heals a Great Multitude(Y)

23 And Jesus went about all Galilee, (Z)teaching in their synagogues, preaching (AA)the gospel of the kingdom, (AB)and healing all kinds of sickness and all kinds of disease among the people. 24 Then [d]His fame went throughout all Syria; and they (AC)brought to Him all sick people who were afflicted with various diseases and torments, and those who were demon-possessed, epileptics, and paralytics; and He healed them. 25 (AD)Great multitudes followed Him—from Galilee, and from [e]Decapolis, Jerusalem, Judea, and beyond the Jordan.

Footnotes

  1. Matthew 4:7 test
  2. Matthew 4:10 M Get behind Me
  3. Matthew 4:17 has drawn near
  4. Matthew 4:24 Lit. the report of Him
  5. Matthew 4:25 Lit. Ten Cities