Mateyu 27
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Yudasi Adzimangirira
27 Mmamawa, akulu a ansembe onse ndi akuluakulu anavomerezana kuti aphe Yesu. 2 Anamumanga, napita naye kukamupereka kwa bwanamkubwa Pilato.
3 Yudasi, amene anamupereka Iye, ataona kuti Yesu waweruzidwa kuti akaphedwe, anatsutsika mu mtima mwake nakabweza ndalama zamasiliva makumi atatu zija kwa akulu a ansembe ndi kwa akuluakulu. 4 Iye anati, “Ndachimwa pakuti ndapereka munthu wosalakwa.”
Iwo anayankha nati, “Ife tilibe nazo kanthu izo ndi zako.”
5 Pamenepo Yudasi anaponya ndalamazo mʼNyumba ya Mulungu nachoka. Kenaka anapita nakadzimangirira.
6 Akulu a ansembe anatola ndalamazo nati, “Sikololedwa ndi lamulo kuti ndalamazi tiziyike mosungira chuma cha Mulungu, popeza ndi ndalama za magazi.” 7 Choncho anagwirizana kuti ndalamazo azigwiritse ntchito pogulira munda wa wowumba mbiya kuti ukhale manda alendo. 8 Ndi chifukwa chake umatchedwa munda wamagazi mpaka lero lino. 9 Pamenepo zimene anayankhula mneneri Yeremiya zinakwaniritsidwa kuti, “Anatenga ndalama zamasiliva makumi atatu mtengo umene anamuyikira Iye anthu a Israeli. 10 Ndipo anazigwiritsa ntchito kugula munda wa wowumba mbiya monga mmene Ambuye anandilamulira ine.”
Yesu kwa Pilato
11 Pa nthawi yomweyo Yesu anayimirira pamaso pa bwanamkubwa ndipo bwanamkubwayo anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndiwe Mfumu ya Ayuda?”
Koma Yesu anayankha kuti, “Mwanena ndinu.”
12 Pamene akulu a ansembe ndi akuluakulu ankamuneneza, sanayankhe kanthu. 13 Kenaka Pilato anamufunsa Iye kuti, “Kodi sukumva zinthu zimene akukunenerazi?” 14 Koma Yesu sanayankhe ngakhale mawu amodzi mpaka bwanamkubwa anadabwa kwambiri.
15 Pa nthawiyi chinali chizolowezi cha bwanamkubwa kuti pachikondwerero cha Paska amamasula wamʼndende wosankhidwa ndi anthu. 16 Pa nthawiyo anali ndi wamʼndende woyipa kwambiri dzina lake Baraba. 17 Gulu la anthu litasonkhana, Pilato anawafunsa kuti, “Ndi ndani amene mufuna kuti ndikumasulireni; Baraba kapena Yesu wotchedwa Khristu?” 18 Pakuti anadziwa kuti anamupereka Yesu chifukwa cha kaduka.
19 Pamene Pilato anakhala pa mpando woweruza, mkazi wake anamutumizira uthenga uwu, “Musachite kanthu ndi munthuyo, ndi wosalakwa pakuti ndavutika kwambiri lero mʼmaloto chifukwa cha munthuyo.”
20 Koma akulu a ansembe ndi akuluakulu ananyengerera gulu la anthu kuti apemphe Baraba ndi kuti Yesu aphedwe.
21 Bwanamkubwayo anafunsa kuti, “Ndi ndani mwa awiriwa amene mufuna ine ndikumasulireni?”
Iwo anayankha kuti, “Baraba.”
22 Pilato anafunsa kuti, “Nanga ndichite chiyani ndi Yesu wotchedwa Khristu?”
Onse anayankha kuti “Mpachikeni!”
23 Pilato anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani? Wachita choyipa chotani?”
Koma anachita phokoso nafuwula kwambiri kuti, “Mpachikeni!”
24 Pilato ataona kuti samaphulapo kanthu, koma mʼmalo mwake chiwawa chimayambika, anatenga madzi nasamba mʼmanja mwake pamaso pa gulu la anthu. Iye anati “Ine ndilibe chifukwa ndi magazi a munthu uyu, ndipo uwu ndi udindo wanu!”
25 Anthu onse anayankha nati, “Magazi ake akhale pa ife ndi pa ana athu!”
26 Pamenepo anawamasulira Baraba koma analamula kuti Yesu akakwapulidwe, ndipo anamupereka kuti akapachikidwe.
Asilikali Amuchita Chipongwe Yesu
27 Pamenepo asilikali abwanamkubwayo anamutenga nalowa naye ku bwalo la milandu ndipo anasonkhanitsa gulu lonse la asilikali namuzungulira Iye. 28 Anamuvula malaya ake namuveka Iye malaya ofiira aufumu. 29 Ndipo kenaka analuka chipewa chaminga nachiyika pa mutu pake. Anamugwiritsa ndodo mʼdzanja lake lamanja nagwada pamaso pake namuchitira chipongwe nati, “Tikulonjereni Mfumu ya Ayuda.” 30 Anamuthira malovu ndipo anatenga ndodo namumenya nayo pa mutu mobwerezabwereza. 31 Atamaliza kumuchitira chipongwe, anamuvula malaya aja namuveka malaya ake aja napita naye kokamupachika.
Amupachika Yesu
32 Pamene gululi linkatuluka ndi Yesu, anakumana ndi munthu wochokera ku Kurene dzina lake Simoni ndipo anamuwumiriza kunyamula mtanda. 33 Anafika ku malo wotchedwa Gologota amene atanthauza kuti malo a bade la mutu. 34 Pamenepo anamupatsa vinyo wosakaniza ndi ndulu kuti amwe; koma atalawa anakana kumwa. 35 Atamupachika Iye, anagawana zovala zake pochita maere. 36 Ndipo anakhala pansi namulonda Iye. 37 Pamwamba pa mutu wake analembapo mawu osonyeza mlandu wake akuti, “uyu ndi yesu, mfumu ya ayuda.” 38 Achifwamba awiri anapachikidwa pamodzi ndi Iye, mmodzi kudzanja lamanja wina kudzanja lamanzere. 39 Ndipo amene amadutsa anamunenera mawu a chipongwe, akupukusa mitu yawo. 40 Ndipo anati, “Iwe amene ungapasule Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanga masiku atatu, dzipulumutse wekha! Tsika pa mtandapo ngati ndiwe Mwana wa Mulungu!”
41 Chimodzimodzinso akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anamuchitira chipongwe. 42 Iwo anati, “Anapulumutsa ena koma sangathe kudzipulumutsa yekha! Ndi mfumu ya Israeli! Mulekeni atsike pa mtanda ndipo tidzamukhulupirira Iye. 43 Amadalira Mulungu, mulekeni Mulunguyo amupulumutse tsopano ngati akumufuna pakuti anati, ‘Ndine Mwana wa Mulungu.’ ” 44 Momwemonso mbala zimene zinapachikidwa naye pamodzi zinamuneneranso zachipongwe.
Kufa kwa Yesu
45 Kuyambira 12 koloko masana mpaka 3 koloko, kunachita mdima pa dziko lonse. 46 Ndipo nthawi ili ngati 3 koloko, Yesu analira mofuwula nati, “Eloi, Eloi, lama sabakitani!” Kutanthauza kuti, “Mulungu Wanga, Mulungu Wanga, mwandisiyiranji Ine?”
47 Ena a oyimirira pamalopo atamva izi anati, “Akuyitana Eliya.”
48 Mmodzi wa iwo anathamanga natenga chinkhupule. Anachidzaza ndi vinyo wosasa, nachizika ku mtengo namupatsa Yesu kuti amwe. 49 Koma ena onse anati, “Mulekeni tiyeni tione ngati Eliyayo abwere kudzamupulutsa.”
50 Ndipo pamene Yesu analiranso mofuwula, anapereka mzimu wake.
51 Pa nthawi imeneyo chinsalu chotchinga cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati kuyambira pamwamba mpaka pansi. Dziko linagwedezeka ndipo miyala inangʼambika. 52 Manda anatsekuka ndipo mitembo yambiri ya anthu oyera mtima amene anafa inaukitsidwa. 53 Anatuluka mʼmanda mwawo, ndipo chitachitika chiukitso cha Yesu, anapita mu mzinda woyera naonekera kwa anthu ambiri.
54 Mkulu wa asilikali ndi amene ankalondera Yesu ataona chivomerezi ndi zonse zinachitika, anachita mantha, ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali Mwana wa Mulungu!”
55 Amayi ambirimbiri amene ankasamalira Yesu ankaonerera ali patali. Iwo anamutsatira Yesu kuchokera ku Galileya. 56 Pakati pawo panali Mariya wa ku Magadala, Mariya amayi ake Yakobo ndi Yosefe ndi amayi a ana a Zebedayo.
Yesu Ayikidwa Mʼmanda
57 Pamene kumada, kunabwera munthu wolemera wa ku Arimateyu dzina lake Yosefe amene anali wophunzira wa Yesu. 58 Anapita kwa Pilato kukapempha mtembo wa Yesu, ndipo Pilato analamula kuti uperekedwe kwa iye. 59 Yosefe anatenga mtembowo, nawukulunga nsalu yabafuta. 60 Ndipo anawuyika mʼmanda ake atsopano amene anasema mu thanthwe, natsekapo ndi mwala waukulu pa khomo la mandawo nachokapo. 61 Mariya wa Magadala ndi Mariya wina anakhala pansi moyangʼanizana ndi mandawo.
Alonda a pa Manda
62 Litapita tsiku lokonzekera Sabata, mmawa mwake, akulu a ansembe ndi Afarisi anapita kwa Pilato. 63 Iwo anati, “Bwana takumbukira kuti munthu wonyenga uja akanali ndi moyo anati, ‘Pakatha masiku atatu ndidzauka.’ 64 Choncho lamulirani kuti manda ake atetezedwe mpaka pa tsiku lachitatu. Chifukwa tikapanda kutero, ophunzira ake angabwere kudzaba mtembo wake ndipo angawuze anthu kuti waukitsidwa kwa akufa. Ndipo chinyengo chomalizachi chidzakhala choyipa kwambiri kusiyana ndi choyamba chija.”
65 Pilato anayankha kuti, “Tengani mlonda kalondereni monga mudziwira.” 66 Tsono anapita nakatseka manda kolimba ndi kuyikapo chizindikiro ndipo anayikapo mlonda.
Matthew 27
New King James Version
Jesus Handed Over to Pontius Pilate(A)
27 When morning came, (B)all the chief priests and elders of the people plotted against Jesus to put Him to death. 2 And when they had bound Him, they led Him away and (C)delivered Him to [a]Pontius Pilate the governor.
Judas Hangs Himself(D)
3 (E)Then Judas, His betrayer, seeing that He had been condemned, was remorseful and brought back the thirty (F)pieces of silver to the chief priests and elders, 4 saying, “I have sinned by betraying innocent blood.”
And they said, “What is that to us? You see to it!”
5 Then he threw down the pieces of silver in the temple and (G)departed, and went and hanged himself.
6 But the chief priests took the silver pieces and said, “It is not lawful to put them into the treasury, because they are the price of blood.” 7 And they consulted together and bought with them the potter’s field, to bury strangers in. 8 Therefore that field has been called (H)the Field of Blood to this day.
9 Then was fulfilled what was spoken by Jeremiah the prophet, saying, (I)“And they took the thirty pieces of silver, the value of Him who was priced, whom they of the children of Israel priced, 10 and (J)gave them for the potter’s field, as the Lord directed me.”
Jesus Faces Pilate(K)
11 Now Jesus stood before the governor. (L)And the governor asked Him, saying, “Are You the King of the Jews?”
Jesus said to him, (M)“It is as you say.” 12 And while He was being accused by the chief priests and elders, (N)He answered nothing.
13 Then Pilate said to Him, (O)“Do You not hear how many things they testify against You?” 14 But He answered him not one word, so that the governor marveled greatly.
Taking the Place of Barabbas(P)
15 (Q)Now at the feast the governor was accustomed to releasing to the multitude one prisoner whom they wished. 16 And at that time they had a notorious prisoner called [b]Barabbas. 17 Therefore, when they had gathered together, Pilate said to them, “Whom do you want me to release to you? Barabbas, or Jesus who is called Christ?” 18 For he knew that they had handed Him over because of (R)envy.
19 While he was sitting on the judgment seat, his wife sent to him, saying, “Have nothing to do with that just Man, for I have suffered many things today in a dream because of Him.”
20 (S)But the chief priests and elders persuaded the multitudes that they should ask for Barabbas and destroy Jesus. 21 The governor answered and said to them, “Which of the two do you want me to release to you?”
They said, (T)“Barabbas!”
22 Pilate said to them, “What then shall I do with Jesus who is called Christ?”
They all said to him, “Let Him be crucified!”
23 Then the governor said, (U)“Why, what evil has He done?”
But they cried out all the more, saying, “Let Him be crucified!”
24 When Pilate saw that he could not prevail at all, but rather that a [c]tumult was rising, he (V)took water and washed his hands before the multitude, saying, “I am innocent of the blood of this [d]just Person. You see to it.”
25 And all the people answered and said, (W)“His blood be on us and on our children.”
26 Then he released Barabbas to them; and when (X)he had [e]scourged Jesus, he delivered Him to be crucified.
The Soldiers Mock Jesus(Y)
27 (Z)Then the soldiers of the governor took Jesus into the [f]Praetorium and gathered the whole [g]garrison around Him. 28 And they (AA)stripped Him and (AB)put a scarlet robe on Him. 29 (AC)When they had [h]twisted a crown of thorns, they put it on His head, and a reed in His right hand. And they bowed the knee before Him and mocked Him, saying, “Hail, King of the Jews!” 30 Then (AD)they spat on Him, and took the reed and struck Him on the head. 31 And when they had mocked Him, they took the robe off Him, put His own clothes on Him, (AE)and led Him away to be crucified.
The King on a Cross(AF)
32 (AG)Now as they came out, (AH)they found a man of Cyrene, Simon by name. Him they compelled to bear His cross. 33 (AI)And when they had come to a place called Golgotha, that is to say, Place of a Skull, 34 (AJ)they gave Him [i]sour wine mingled with gall to drink. But when He had tasted it, He would not drink.
35 (AK)Then they crucified Him, and divided His garments, casting lots, [j]that it might be fulfilled which was spoken by the prophet:
(AL)“They divided My garments among them,
And for My clothing they cast lots.”
36 (AM)Sitting down, they kept watch over Him there. 37 And they (AN)put up over His head the accusation written against Him:
THIS IS JESUS THE KING OF THE JEWS.
38 (AO)Then two robbers were crucified with Him, one on the right and another on the left.
39 And (AP)those who passed by blasphemed Him, wagging their heads 40 and saying, (AQ)“You who destroy the temple and build it in three days, save Yourself! (AR)If You are the Son of God, come down from the cross.”
41 Likewise the chief priests also, mocking with the [k]scribes and elders, said, 42 “He (AS)saved others; Himself He cannot save. [l]If He is the King of Israel, let Him now come down from the cross, and we will believe [m]Him. 43 (AT)He trusted in God; let Him deliver Him now if He will have Him; for He said, ‘I am the Son of God.’ ”
44 (AU)Even the robbers who were crucified with Him reviled Him with the same thing.
Jesus Dies on the Cross(AV)
45 (AW)Now from the sixth hour until the ninth hour there was darkness over all the land. 46 And about the ninth hour (AX)Jesus cried out with a loud voice, saying, “Eli, Eli, lama sabachthani?” that is, (AY)“My God, My God, why have You forsaken Me?”
47 Some of those who stood there, when they heard that, said, “This Man is calling for Elijah!” 48 Immediately one of them ran and took a sponge, (AZ)filled it with sour wine and put it on a reed, and offered it to Him to drink.
49 The rest said, “Let Him alone; let us see if Elijah will come to save Him.”
50 And Jesus (BA)cried out again with a loud voice, and (BB)yielded up His spirit.
51 Then, behold, (BC)the veil of the temple was torn in two from top to bottom; and the earth quaked, and the rocks were split, 52 and the graves were opened; and many bodies of the saints who had fallen asleep were raised; 53 and coming out of the graves after His resurrection, they went into the holy city and appeared to many.
54 (BD)So when the centurion and those with him, who were guarding Jesus, saw the earthquake and the things that had happened, they feared greatly, saying, (BE)“Truly this was the Son of God!”
55 And many women (BF)who followed Jesus from Galilee, ministering to Him, were there looking on from afar, 56 (BG)among whom were Mary Magdalene, Mary the mother of James and [n]Joses, and the mother of Zebedee’s sons.
Jesus Buried in Joseph’s Tomb(BH)
57 Now (BI)when evening had come, there came a rich man from Arimathea, named Joseph, who himself had also become a disciple of Jesus. 58 This man went to Pilate and asked for the body of Jesus. Then Pilate commanded the body to be given to him. 59 When Joseph had taken the body, he wrapped it in a clean linen cloth, 60 and (BJ)laid it in his new tomb which he had hewn out of the rock; and he rolled a large stone against the door of the tomb, and departed. 61 And Mary Magdalene was there, and the other Mary, sitting [o]opposite the tomb.
Pilate Sets a Guard
62 On the next day, which followed the Day of Preparation, the chief priests and Pharisees gathered together to Pilate, 63 saying, “Sir, we remember, while He was still alive, how that deceiver said, (BK)‘After three days I will rise.’ 64 Therefore command that the tomb be made secure until the third day, lest His disciples come [p]by night and steal Him away, and say to the people, ‘He has risen from the dead.’ So the last deception will be worse than the first.”
65 Pilate said to them, “You have a guard; go your way, make it as secure as you know how.” 66 So they went and made the tomb secure, (BL)sealing the stone and setting the guard.
Footnotes
- Matthew 27:2 NU omits Pontius
- Matthew 27:16 NU Jesus Barabbas
- Matthew 27:24 an uproar
- Matthew 27:24 NU omits just
- Matthew 27:26 flogged with a Roman scourge
- Matthew 27:27 The governor’s headquarters
- Matthew 27:27 cohort
- Matthew 27:29 Lit. woven
- Matthew 27:34 NU omits sour
- Matthew 27:35 NU, M omit the rest of v. 35.
- Matthew 27:41 M scribes, the Pharisees, and the elders
- Matthew 27:42 NU omits If
- Matthew 27:42 NU, M in Him
- Matthew 27:56 NU Joseph
- Matthew 27:61 in front of
- Matthew 27:64 NU omits by night
Matthew 27
King James Version
27 When the morning was come, all the chief priests and elders of the people took counsel against Jesus to put him to death:
2 And when they had bound him, they led him away, and delivered him to Pontius Pilate the governor.
3 Then Judas, which had betrayed him, when he saw that he was condemned, repented himself, and brought again the thirty pieces of silver to the chief priests and elders,
4 Saying, I have sinned in that I have betrayed the innocent blood. And they said, What is that to us? see thou to that.
5 And he cast down the pieces of silver in the temple, and departed, and went and hanged himself.
6 And the chief priests took the silver pieces, and said, It is not lawful for to put them into the treasury, because it is the price of blood.
7 And they took counsel, and bought with them the potter's field, to bury strangers in.
8 Wherefore that field was called, The field of blood, unto this day.
9 Then was fulfilled that which was spoken by Jeremy the prophet, saying, And they took the thirty pieces of silver, the price of him that was valued, whom they of the children of Israel did value;
10 And gave them for the potter's field, as the Lord appointed me.
11 And Jesus stood before the governor: and the governor asked him, saying, Art thou the King of the Jews? And Jesus said unto him, Thou sayest.
12 And when he was accused of the chief priests and elders, he answered nothing.
13 Then said Pilate unto him, Hearest thou not how many things they witness against thee?
14 And he answered him to never a word; insomuch that the governor marvelled greatly.
15 Now at that feast the governor was wont to release unto the people a prisoner, whom they would.
16 And they had then a notable prisoner, called Barabbas.
17 Therefore when they were gathered together, Pilate said unto them, Whom will ye that I release unto you? Barabbas, or Jesus which is called Christ?
18 For he knew that for envy they had delivered him.
19 When he was set down on the judgment seat, his wife sent unto him, saying, Have thou nothing to do with that just man: for I have suffered many things this day in a dream because of him.
20 But the chief priests and elders persuaded the multitude that they should ask Barabbas, and destroy Jesus.
21 The governor answered and said unto them, Whether of the twain will ye that I release unto you? They said, Barabbas.
22 Pilate saith unto them, What shall I do then with Jesus which is called Christ? They all say unto him, Let him be crucified.
23 And the governor said, Why, what evil hath he done? But they cried out the more, saying, Let him be crucified.
24 When Pilate saw that he could prevail nothing, but that rather a tumult was made, he took water, and washed his hands before the multitude, saying, I am innocent of the blood of this just person: see ye to it.
25 Then answered all the people, and said, His blood be on us, and on our children.
26 Then released he Barabbas unto them: and when he had scourged Jesus, he delivered him to be crucified.
27 Then the soldiers of the governor took Jesus into the common hall, and gathered unto him the whole band of soldiers.
28 And they stripped him, and put on him a scarlet robe.
29 And when they had platted a crown of thorns, they put it upon his head, and a reed in his right hand: and they bowed the knee before him, and mocked him, saying, Hail, King of the Jews!
30 And they spit upon him, and took the reed, and smote him on the head.
31 And after that they had mocked him, they took the robe off from him, and put his own raiment on him, and led him away to crucify him.
32 And as they came out, they found a man of Cyrene, Simon by name: him they compelled to bear his cross.
33 And when they were come unto a place called Golgotha, that is to say, a place of a skull,
34 They gave him vinegar to drink mingled with gall: and when he had tasted thereof, he would not drink.
35 And they crucified him, and parted his garments, casting lots: that it might be fulfilled which was spoken by the prophet, They parted my garments among them, and upon my vesture did they cast lots.
36 And sitting down they watched him there;
37 And set up over his head his accusation written, This Is Jesus The King Of The Jews.
38 Then were there two thieves crucified with him, one on the right hand, and another on the left.
39 And they that passed by reviled him, wagging their heads,
40 And saying, Thou that destroyest the temple, and buildest it in three days, save thyself. If thou be the Son of God, come down from the cross.
41 Likewise also the chief priests mocking him, with the scribes and elders, said,
42 He saved others; himself he cannot save. If he be the King of Israel, let him now come down from the cross, and we will believe him.
43 He trusted in God; let him deliver him now, if he will have him: for he said, I am the Son of God.
44 The thieves also, which were crucified with him, cast the same in his teeth.
45 Now from the sixth hour there was darkness over all the land unto the ninth hour.
46 And about the ninth hour Jesus cried with a loud voice, saying, Eli, Eli, lama sabachthani? that is to say, My God, my God, why hast thou forsaken me?
47 Some of them that stood there, when they heard that, said, This man calleth for Elias.
48 And straightway one of them ran, and took a spunge, and filled it with vinegar, and put it on a reed, and gave him to drink.
49 The rest said, Let be, let us see whether Elias will come to save him.
50 Jesus, when he had cried again with a loud voice, yielded up the ghost.
51 And, behold, the veil of the temple was rent in twain from the top to the bottom; and the earth did quake, and the rocks rent;
52 And the graves were opened; and many bodies of the saints which slept arose,
53 And came out of the graves after his resurrection, and went into the holy city, and appeared unto many.
54 Now when the centurion, and they that were with him, watching Jesus, saw the earthquake, and those things that were done, they feared greatly, saying, Truly this was the Son of God.
55 And many women were there beholding afar off, which followed Jesus from Galilee, ministering unto him:
56 Among which was Mary Magdalene, and Mary the mother of James and Joses, and the mother of Zebedees children.
57 When the even was come, there came a rich man of Arimathaea, named Joseph, who also himself was Jesus' disciple:
58 He went to Pilate, and begged the body of Jesus. Then Pilate commanded the body to be delivered.
59 And when Joseph had taken the body, he wrapped it in a clean linen cloth,
60 And laid it in his own new tomb, which he had hewn out in the rock: and he rolled a great stone to the door of the sepulchre, and departed.
61 And there was Mary Magdalene, and the other Mary, sitting over against the sepulchre.
62 Now the next day, that followed the day of the preparation, the chief priests and Pharisees came together unto Pilate,
63 Saying, Sir, we remember that that deceiver said, while he was yet alive, After three days I will rise again.
64 Command therefore that the sepulchre be made sure until the third day, lest his disciples come by night, and steal him away, and say unto the people, He is risen from the dead: so the last error shall be worse than the first.
65 Pilate said unto them, Ye have a watch: go your way, make it as sure as ye can.
66 So they went, and made the sepulchre sure, sealing the stone, and setting a watch.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.
