Masalimo 7
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.
7 Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;
pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 mwina angandikadzule ngati mkango,
ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Inu Yehova Mulungu wanga,
ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,
kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,
lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi
ndipo mundigoneke pa fumbi.
Sela
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;
nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.
Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.
Alamulireni muli kumwambako;
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.
Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,
monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Inu Mulungu wolungama,
amene mumasanthula maganizo ndi mitima,
thetsani chiwawa cha anthu oyipa
ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,
amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mulungu amaweruza molungama,
Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Ngati munthu satembenuka,
Mulungu adzanola lupanga lake,
Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa;
Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.
Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa
amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;
chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;
ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Tehillim 7
Orthodox Jewish Bible
7 (Shiggayon of Dovid, which he sang unto Hashem, regarding Kush of Binyamin) Hashem Elohai, in Thee do I seek refuge; hoshieini (save me) from all them that persecute me, and deliver me;
2 (3) Lest he tear my nefesh like a lion, rending it in pieces, while there is none to rescue.
3 (4) Hashem Elohai, if I have done this; if there be guilt in my hands;
4 (5) If I have recompensed with evil him that held out shalom unto me; or, without cause plundered my opposers,
5 (6) Then let the enemy persecute my nefesh, and take it; yea, let him tread down my life to the earth, and lay mine kavod to sleep in the dust. Selah.
6 (7) Arise, Hashem, in Thine anger, lift up Thyself because of the rage of mine enemies; awake, o my El, to the mishpat Thou hast decreed.
7 (8) So let the Adat l’Umim surround Thee; and over it return Thou on high [to judge].
8 (9) Hashem shall judge the people; judge me, Hashem, according to my tzedek, and according to mine integrity that is in me.
9 (10) Oh let the wickedness of the resha’im come to an end; but make the tzaddik secure; for the Elohim Tzaddik trieth the minds and hearts.
10 (11) My mogen (shield) is Elohim, Moshi’a of the upright in heart.
11 (12) Elohim is a Shofet Tzaddik, and El expresses wrath kol yom.
12 (13) If He relent not, He will sharpen His cherev; He hath bent His keshet (bow) and made it ready.
13 (14) He hath also prepared for Him the instruments of mavet; He ordaineth His flaming khitzim (arrows).
14 (15) Hinei, he [an evil person] travaileth with iniquity, and hath conceived trouble, and brought forth falsehood.
15 (16) He makes a pit, and digs it, and is fallen into the shachat (pit) which he made.
16 (17) His trouble shall return upon his own rosh, and his chamas shall come down upon his own kodkod (crown of the head).
17 (18) I will give thanks to Hashem according to His tzedek; and will sing praise to the Shem of Hashem Elyon.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Copyright © 2002, 2003, 2008, 2010, 2011 by Artists for Israel International