Masalimo 67
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.
67 Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,
achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,
chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,
pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo
ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6 Nthaka yabereka zokolola zake;
tidalitseni Mulungu wathu.
7 Mulungu atidalitse
kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Psalm 67
New International Version
Psalm 67[a]
For the director of music. With stringed instruments. A psalm. A song.
1 May God be gracious to us and bless us
and make his face shine on us—[b](A)
2 so that your ways may be known on earth,
your salvation(B) among all nations.(C)
Footnotes
- Psalm 67:1 In Hebrew texts 67:1-7 is numbered 67:2-8.
- Psalm 67:1 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 4.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.