Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.

67 Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,
    achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,
    chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.

Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
    mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,
    pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo
    ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
    mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

Nthaka yabereka zokolola zake;
    tidalitseni Mulungu wathu.
Mulungu atidalitse
    kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

Psalm 67[a]

For the director of music. With stringed instruments. A psalm. A song.

May God be gracious to us and bless us
    and make his face shine on us—[b](A)
so that your ways may be known on earth,
    your salvation(B) among all nations.(C)

May the peoples praise you, God;
    may all the peoples praise you.(D)
May the nations be glad and sing for joy,(E)
    for you rule the peoples with equity(F)
    and guide the nations of the earth.(G)
May the peoples praise you, God;
    may all the peoples praise you.

The land yields its harvest;(H)
    God, our God, blesses us.(I)
May God bless us still,
    so that all the ends of the earth(J) will fear him.(K)

Footnotes

  1. Psalm 67:1 In Hebrew texts 67:1-7 is numbered 67:2-8.
  2. Psalm 67:1 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 4.