Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
    onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
    mvetserani mawu a pakamwa panga.

Alendo akundithira nkhondo;
    anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
    anthu amene salabadira za Mulungu.

Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
    Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
    mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
    ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
    pakuti ndi labwino.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
    ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

54 Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
    onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
    mvetserani mawu a pakamwa panga.

Alendo akundithira nkhondo;
    anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
    anthu amene salabadira za Mulungu.

Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
    Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
    mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
    ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
    pakuti ndi labwino.
Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
    ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.