Add parallel Print Page Options

33 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,
    nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe;
    muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Muyimbireni nyimbo yatsopano;
    imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.

Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;
    Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;
    dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.

Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,
    zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;
    amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Dziko lonse lapansi liope Yehova;
    anthu onse amulemekeze Iye.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;
    Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;
    Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,
    zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.

12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,
    anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi
    ndi kuona anthu onse;
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira
    onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse,
    amaona zonse zimene akuchita.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;
    palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,
    ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;
    amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 kuwawombola iwo ku imfa
    ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.

20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;
    Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera,
    pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Chikondi chanu chosatha
    chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

Psalm 33

Sing joyfully(A) to the Lord, you righteous;
    it is fitting(B) for the upright(C) to praise him.
Praise the Lord with the harp;(D)
    make music to him on the ten-stringed lyre.(E)
Sing to him a new song;(F)
    play skillfully, and shout for joy.(G)

For the word of the Lord is right(H) and true;(I)
    he is faithful(J) in all he does.
The Lord loves righteousness and justice;(K)
    the earth is full of his unfailing love.(L)

By the word(M) of the Lord the heavens were made,(N)
    their starry host(O) by the breath of his mouth.
He gathers the waters(P) of the sea into jars[a];(Q)
    he puts the deep into storehouses.
Let all the earth fear the Lord;(R)
    let all the people of the world(S) revere him.(T)
For he spoke, and it came to be;
    he commanded,(U) and it stood firm.

10 The Lord foils(V) the plans(W) of the nations;(X)
    he thwarts the purposes of the peoples.
11 But the plans of the Lord stand firm(Y) forever,
    the purposes(Z) of his heart through all generations.

12 Blessed is the nation whose God is the Lord,(AA)
    the people he chose(AB) for his inheritance.(AC)
13 From heaven the Lord looks down(AD)
    and sees all mankind;(AE)
14 from his dwelling place(AF) he watches
    all who live on earth—
15 he who forms(AG) the hearts of all,
    who considers everything they do.(AH)

16 No king is saved by the size of his army;(AI)
    no warrior escapes by his great strength.
17 A horse(AJ) is a vain hope for deliverance;
    despite all its great strength it cannot save.
18 But the eyes(AK) of the Lord are on those who fear him,
    on those whose hope is in his unfailing love,(AL)
19 to deliver them from death(AM)
    and keep them alive in famine.(AN)

20 We wait(AO) in hope for the Lord;
    he is our help and our shield.
21 In him our hearts rejoice,(AP)
    for we trust in his holy name.(AQ)
22 May your unfailing love(AR) be with us, Lord,
    even as we put our hope in you.

Footnotes

  1. Psalm 33:7 Or sea as into a heap