Masalimo 25
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Davide.
25 Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Ndimadalira Inu Mulungu wanga.
Musalole kuti ndichite manyazi
kapena kuti adani anga andipambane.
3 Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye
sadzachititsidwa manyazi
koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi
ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova,
phunzitseni mayendedwe anu;
5 tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa,
pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga,
ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu,
pakuti ndi zakalekale.
7 Musakumbukire machimo a ubwana wanga
ndi makhalidwe anga owukira;
molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine,
pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama;
choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama
ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika
kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova,
khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova?
Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse,
ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa;
amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse,
pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima,
pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira;
masuleni ku zowawa zanga.
18 Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga
ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Onani mmene adani anga achulukira
ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa;
musalole kuti ndichite manyazi,
pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze,
chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Wombolani Israeli Inu Mulungu,
ku mavuto ake onse!
Psalm 25
New King James Version
A Plea for Deliverance and Forgiveness
A Psalm of David.
25 To (A)You, O Lord, I lift up my soul.
2 O my God, I (B)trust in You;
Let me not be ashamed;
(C)Let not my enemies triumph over me.
3 Indeed, let no one who [a]waits on You be ashamed;
Let those be ashamed who deal treacherously without cause.
4 (D)Show me Your ways, O Lord;
Teach me Your paths.
5 Lead me in Your truth and teach me,
For You are the God of my salvation;
On You I wait all the day.
6 Remember, O Lord, (E)Your tender mercies and Your lovingkindnesses,
For they are from of old.
7 Do not remember (F)the sins of my youth, nor my transgressions;
(G)According to Your mercy remember me,
For Your goodness’ sake, O Lord.
8 Good and upright is the Lord;
Therefore He teaches sinners in the way.
9 The humble He guides in justice,
And the humble He teaches His way.
10 All the paths of the Lord are mercy and truth,
To such as keep His covenant and His testimonies.
11 (H)For Your name’s sake, O Lord,
Pardon my iniquity, for it is great.
12 Who is the man that fears the Lord?
(I)Him shall [b]He teach in the way He chooses.
13 (J)He himself shall dwell in [c]prosperity,
And (K)his descendants shall inherit the earth.
14 (L)The secret of the Lord is with those who fear Him,
And He will show them His covenant.
15 (M)My eyes are ever toward the Lord,
For He shall [d]pluck my feet out of the net.
16 (N)Turn Yourself to me, and have mercy on me,
For I am [e]desolate and afflicted.
17 The troubles of my heart have enlarged;
Bring me out of my distresses!
18 (O)Look on my affliction and my pain,
And forgive all my sins.
19 Consider my enemies, for they are many;
And they hate me with [f]cruel hatred.
20 Keep my soul, and deliver me;
Let me not be ashamed, for I put my trust in You.
21 Let integrity and uprightness preserve me,
For I wait for You.
22 (P)Redeem Israel, O God,
Out of all their troubles!
Footnotes
- Psalm 25:3 Waits for You in faith
- Psalm 25:12 Or he
- Psalm 25:13 Lit. goodness
- Psalm 25:15 Lit. bring out
- Psalm 25:16 lonely
- Psalm 25:19 violent hatred
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.