Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

24 Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo,
    dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja
    ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.

Ndani angakwere phiri la Yehova?
    Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera,
    amene sapereka moyo wake kwa fano
    kapena kulumbira mwachinyengo.
Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova
    ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova;
    amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo.
            Sela

Tukulani mitu yanu inu zipata;
    tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
    kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
    Yehova Wamphamvuzonse,
    Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Tukulani mitu yanu, inu zipata;
    tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
    kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
    Yehova Wamphamvuzonse,
    Iye ndiye Mfumu yaulemerero.
            Sela

The King of Glory and His Kingdom

A Psalm of David.

24 The (A)earth is the Lord’s, and all its fullness,
The world and those who dwell therein.
For He has (B)founded it upon the seas,
And established it upon the [a]waters.

(C)Who may ascend into the hill of the Lord?
Or who may stand in His holy place?
He who has (D)clean hands and (E)a pure heart,
Who has not lifted up his soul to an idol,
Nor (F)sworn deceitfully.
He shall receive blessing from the Lord,
And righteousness from the God of his salvation.
This is Jacob, the generation of those who (G)seek Him,
Who seek Your face. Selah

(H)Lift up your heads, O you gates!
And be lifted up, you everlasting doors!
(I)And the King of glory shall come in.
Who is this King of glory?
The Lord strong and mighty,
The Lord mighty in (J)battle.
Lift up your heads, O you gates!
Lift up, you everlasting doors!
And the King of glory shall come in.
10 Who is this King of glory?
The Lord of hosts,
He is the King of glory. Selah

Footnotes

  1. Psalm 24:2 Lit. rivers