Add parallel Print Page Options

149 Tamandani Yehova.

Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
    matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.

Israeli asangalale mwa mlengi wake;
    anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.
Atamande dzina lake povina
    ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.
Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake;
    Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.
Oyera mtima asangalale mu ulemu wake
    ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.

Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo,
    ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,
kubwezera chilango anthu a mitundu ina,
    ndi kulanga anthu a mitundu yonse,
kumanga mafumu awo ndi zingwe,
    anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,
kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo
    Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.

Tamandani Yehova.