Add parallel Print Page Options

149 Tamandani Yehova.

Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
    matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.

Israeli asangalale mwa mlengi wake;
    anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.
Atamande dzina lake povina
    ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.
Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake;
    Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.
Oyera mtima asangalale mu ulemu wake
    ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.

Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo,
    ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,
kubwezera chilango anthu a mitundu ina,
    ndi kulanga anthu a mitundu yonse,
kumanga mafumu awo ndi zingwe,
    anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,
kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo
    Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.

Tamandani Yehova.

149 Tamandani Yehova.

Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,
    matamando ake mu msonkhano wa oyera mtima.

Israeli asangalale mwa mlengi wake;
    anthu a ku Ziyoni akondwere mwa Mfumu yawo.
Atamande dzina lake povina
    ndi kuyimbira Iye nyimbo ndi tambolini ndi pangwe.
Pakuti Yehova amakondwera ndi anthu ake;
    Iye amaveka chipulumutso odzichepetsa.
Oyera mtima asangalale mu ulemu wake
    ndi kuyimba mwachimwemwe pa mabedi awo.

Matamando a Mulungu akhale pakamwa pawo,
    ndi lupanga lakuthwa konsekonse mʼmanja mwawo,
kubwezera chilango anthu a mitundu ina,
    ndi kulanga anthu a mitundu yonse,
kumanga mafumu awo ndi zingwe,
    anthu awo otchuka ndi unyolo wachitsulo,
kuchita zimene zinalembedwa zotsutsana nawo
    Uwu ndi ulemerero wa oyera mtima ake onse.

Tamandani Yehova.