Masalimo 14
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
14 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
“Kulibe Mulungu.”
Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa;
palibe amene amachita zabwino.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi,
kuyangʼana anthu onse
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
amene amafunafuna Mulungu.
3 Onse atembenukira kumbali,
onse pamodzi asanduka oyipa;
palibe amene amachita zabwino,
palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse?
Akudya anthu anga ngati chakudya chawo
ndipo satamanda Yehova?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu,
pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka,
koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni!
Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake,
Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
詩篇 14
Chinese Union Version Modern Punctuation (Traditional)
人之愚頑及罪惡
14 大衛的詩,交於伶長。
1 愚頑人心裡說:「沒有神!」他們都是邪惡,行了可憎惡的事,沒有一個人行善。
2 耶和華從天上垂看世人,要看有明白的沒有,有尋求神的沒有。
3 他們都偏離正路,一同變為汙穢;並沒有行善的,連一個也沒有。
4 作孽的都沒有知識嗎?他們吞吃我的百姓,如同吃飯一樣,並不求告耶和華。
5 他們在那裡大大地害怕,因為神在義人的族類中。
6 你們叫困苦人的謀算變為羞辱,然而耶和華是他的避難所。
7 但願以色列的救恩從錫安而出!耶和華救回他被擄的子民,那時雅各要快樂,以色列要歡喜。
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Copyright © 2011 by Global Bible Initiative
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.