Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide.

53 Chitsiru chimati mu mtima mwake,
    “Kulibe Mulungu.”
Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa;
    palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.

Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano
    pa ana a anthu
kuti aone ngati alipo wina wanzeru,
    wofunafuna Mulungu.
Aliyense wabwerera,
    iwo onse pamodzi akhala oyipa;
palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino,
    ngakhale mmodzi.

Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi;
    anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi,
    ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu
    pamene panalibe kanthu kochititsa mantha.
Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo;
    inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.

Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni!
    Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake,
    lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!