Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

39 Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga
    ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;
ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero
    nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
Koma pamene ndinali chete
    osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino
    mavuto anga anachulukirabe.
Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,
    ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;
    kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga
    ndi chiwerengero cha masiku anga;
    mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,
    kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;
    moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.
            Sela
Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:
    Iye amangovutika koma popanda phindu;
    amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?
    Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;
    musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga
    pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine;
    ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;
    mumawononga chuma chawo monga njenjete;
    munthu aliyense ali ngati mpweya.
            Sela

12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova,
    mverani kulira kwanga kopempha thandizo;
    musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,
popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;
    monga anachitira makolo anga onse.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala
    ndisanafe ndi kuyiwalika.”

Psalm 39[a]

For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.

I said, “I will watch my ways(A)
    and keep my tongue from sin;(B)
I will put a muzzle on my mouth(C)
    while in the presence of the wicked.”
So I remained utterly silent,(D)
    not even saying anything good.
But my anguish(E) increased;
    my heart grew hot(F) within me.
While I meditated,(G) the fire(H) burned;
    then I spoke with my tongue:

“Show me, Lord, my life’s end
    and the number of my days;(I)
    let me know how fleeting(J) my life is.(K)
You have made my days(L) a mere handbreadth;
    the span of my years is as nothing before you.
Everyone is but a breath,(M)
    even those who seem secure.[b]

“Surely everyone goes around(N) like a mere phantom;(O)
    in vain they rush about,(P) heaping up wealth(Q)
    without knowing whose it will finally be.(R)

“But now, Lord, what do I look for?
    My hope is in you.(S)
Save me(T) from all my transgressions;(U)
    do not make me the scorn(V) of fools.
I was silent;(W) I would not open my mouth,(X)
    for you are the one who has done this.(Y)
10 Remove your scourge from me;
    I am overcome by the blow(Z) of your hand.(AA)
11 When you rebuke(AB) and discipline(AC) anyone for their sin,
    you consume(AD) their wealth like a moth(AE)
    surely everyone is but a breath.(AF)

12 “Hear my prayer, Lord,
    listen to my cry for help;(AG)
    do not be deaf(AH) to my weeping.(AI)
I dwell with you as a foreigner,(AJ)
    a stranger,(AK) as all my ancestors were.(AL)
13 Look away from me, that I may enjoy life again
    before I depart and am no more.”(AM)

Footnotes

  1. Psalm 39:1 In Hebrew texts 39:1-13 is numbered 39:2-14.
  2. Psalm 39:5 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 11.