Masalimo 39
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.
39 Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga
ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;
ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero
nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”
2 Koma pamene ndinali chete
osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino
mavuto anga anachulukirabe.
3 Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,
ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;
kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:
4 “Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga
ndi chiwerengero cha masiku anga;
mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.
5 Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,
kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;
moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.
Sela
6 Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:
Iye amangovutika koma popanda phindu;
amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.
7 “Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?
Chiyembekezo changa chili mwa Inu.
8 Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;
musandisandutse chonyozeka kwa opusa.
9 Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga
pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.
10 Chotsani mkwapulo wanu pa ine;
ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.
11 Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;
mumawononga chuma chawo monga njenjete;
munthu aliyense ali ngati mpweya.
Sela
12 “Imvani pemphero langa Inu Yehova,
mverani kulira kwanga kopempha thandizo;
musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,
popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;
monga anachitira makolo anga onse.
13 Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala
ndisanafe ndi kuyiwalika.”
Psalm 39
New International Version
Psalm 39[a]
For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.
1 I said, “I will watch my ways(A)
and keep my tongue from sin;(B)
I will put a muzzle on my mouth(C)
while in the presence of the wicked.”
2 So I remained utterly silent,(D)
not even saying anything good.
But my anguish(E) increased;
3 my heart grew hot(F) within me.
While I meditated,(G) the fire(H) burned;
then I spoke with my tongue:
4 “Show me, Lord, my life’s end
and the number of my days;(I)
let me know how fleeting(J) my life is.(K)
5 You have made my days(L) a mere handbreadth;
the span of my years is as nothing before you.
Everyone is but a breath,(M)
even those who seem secure.[b]
6 “Surely everyone goes around(N) like a mere phantom;(O)
in vain they rush about,(P) heaping up wealth(Q)
without knowing whose it will finally be.(R)
7 “But now, Lord, what do I look for?
My hope is in you.(S)
8 Save me(T) from all my transgressions;(U)
do not make me the scorn(V) of fools.
9 I was silent;(W) I would not open my mouth,(X)
for you are the one who has done this.(Y)
10 Remove your scourge from me;
I am overcome by the blow(Z) of your hand.(AA)
11 When you rebuke(AB) and discipline(AC) anyone for their sin,
you consume(AD) their wealth like a moth(AE)—
surely everyone is but a breath.(AF)
Footnotes
- Psalm 39:1 In Hebrew texts 39:1-13 is numbered 39:2-14.
- Psalm 39:5 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 11.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.