Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

139 Inu Yehova, mwandisanthula
    ndipo mukundidziwa.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka;
    mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga;
    mumadziwa njira zanga zonse.
Mawu asanatuluke pa lilime langa
    mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.

Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe;
    mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga,
    ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.

Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu?
    Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko;
    ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko.
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa,
    ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,
    dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.

11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu
    ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu;
    usiku udzawala ngati masana,
    pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.

13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga;
    munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa;
    ntchito zanu ndi zodabwitsa,
    zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu
    pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi,
pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe.
    Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu
    asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.

17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu,
    ndi zosawerengeka ndithu!
18 Ndikanaziwerenga,
    zikanakhala zochuluka kuposa mchenga;
    pamene ndadzuka, ndili nanube.

19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu!
    Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa;
    adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova?
    Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 Ndimadana nawo kwathunthu;
    ndi adani anga.

23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga;
    Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine,
    ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.

Psalm 139

For the director of music. Of David. A psalm.

You have searched me,(A) Lord,
    and you know(B) me.
You know when I sit and when I rise;(C)
    you perceive my thoughts(D) from afar.
You discern my going out(E) and my lying down;
    you are familiar with all my ways.(F)
Before a word is on my tongue
    you, Lord, know it completely.(G)
You hem me in(H) behind and before,
    and you lay your hand upon me.
Such knowledge is too wonderful for me,(I)
    too lofty(J) for me to attain.

Where can I go from your Spirit?
    Where can I flee(K) from your presence?
If I go up to the heavens,(L) you are there;
    if I make my bed(M) in the depths, you are there.
If I rise on the wings of the dawn,
    if I settle on the far side of the sea,
10 even there your hand will guide me,(N)
    your right hand(O) will hold me fast.
11 If I say, “Surely the darkness will hide me
    and the light become night around me,”
12 even the darkness will not be dark(P) to you;
    the night will shine like the day,
    for darkness is as light to you.

13 For you created my inmost being;(Q)
    you knit me together(R) in my mother’s womb.(S)
14 I praise you(T) because I am fearfully and wonderfully made;
    your works are wonderful,(U)
    I know that full well.
15 My frame was not hidden from you
    when I was made(V) in the secret place,
    when I was woven together(W) in the depths of the earth.(X)
16 Your eyes saw my unformed body;
    all the days ordained(Y) for me were written in your book
    before one of them came to be.
17 How precious to me are your thoughts,[a](Z) God!(AA)
    How vast is the sum of them!
18 Were I to count them,(AB)
    they would outnumber the grains of sand(AC)
    when I awake,(AD) I am still with you.

19 If only you, God, would slay the wicked!(AE)
    Away from me,(AF) you who are bloodthirsty!(AG)
20 They speak of you with evil intent;
    your adversaries(AH) misuse your name.(AI)
21 Do I not hate those(AJ) who hate you, Lord,
    and abhor(AK) those who are in rebellion against you?
22 I have nothing but hatred for them;
    I count them my enemies.(AL)
23 Search me,(AM) God, and know my heart;(AN)
    test me and know my anxious thoughts.
24 See if there is any offensive way(AO) in me,
    and lead me(AP) in the way everlasting.

Footnotes

  1. Psalm 139:17 Or How amazing are your thoughts concerning me