Masalimo 138
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Davide.
138 Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;
ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera
ndipo ndidzayamika dzina lanu
chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,
pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu
kupambana zinthu zonse.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha;
munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,
pamene amva mawu a pakamwa panu.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova,
pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,
koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,
mumasunga moyo wanga;
mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,
mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;
chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha
musasiye ntchito ya manja anu.
Psalm 138
New International Version
Psalm 138
Of David.
1 I will praise you, Lord, with all my heart;
before the “gods”(A) I will sing(B) your praise.
2 I will bow down toward your holy temple(C)
and will praise your name(D)
for your unfailing love and your faithfulness,(E)
for you have so exalted your solemn decree
that it surpasses your fame.(F)
3 When I called,(G) you answered me;(H)
you greatly emboldened(I) me.
4 May all the kings of the earth(J) praise you, Lord,
when they hear what you have decreed.
5 May they sing(K) of the ways of the Lord,
for the glory of the Lord(L) is great.
6 Though the Lord is exalted, he looks kindly on the lowly;(M)
though lofty, he sees them(N) from afar.
7 Though I walk(O) in the midst of trouble,
you preserve my life.(P)
You stretch out your hand(Q) against the anger of my foes;(R)
with your right hand(S) you save me.(T)
8 The Lord will vindicate(U) me;
your love, Lord, endures forever(V)—
do not abandon(W) the works of your hands.(X)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.