Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

138 Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse;
    ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera
    ndipo ndidzayamika dzina lanu
    chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu,
pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu
    kupambana zinthu zonse.
Pamene ndinayitana, munandiyankha;
    munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.

Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova,
    pamene amva mawu a pakamwa panu.
Iwo ayimbe za njira za Yehova,
    pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.

Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa,
    koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
Ngakhale ndiyende pakati pa masautso,
    mumasunga moyo wanga;
mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga,
    mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine;
    chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha
    musasiye ntchito ya manja anu.

Psalm 138

Of David.

I will praise you, Lord, with all my heart;
    before the “gods”(A) I will sing(B) your praise.
I will bow down toward your holy temple(C)
    and will praise your name(D)
    for your unfailing love and your faithfulness,(E)
for you have so exalted your solemn decree
    that it surpasses your fame.(F)
When I called,(G) you answered me;(H)
    you greatly emboldened(I) me.

May all the kings of the earth(J) praise you, Lord,
    when they hear what you have decreed.
May they sing(K) of the ways of the Lord,
    for the glory of the Lord(L) is great.

Though the Lord is exalted, he looks kindly on the lowly;(M)
    though lofty, he sees them(N) from afar.
Though I walk(O) in the midst of trouble,
    you preserve my life.(P)
You stretch out your hand(Q) against the anger of my foes;(R)
    with your right hand(S) you save me.(T)
The Lord will vindicate(U) me;
    your love, Lord, endures forever(V)
    do not abandon(W) the works of your hands.(X)