Add parallel Print Page Options

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

128 Odala ndi onse amene amaopa Yehova,
    amene amayenda mʼnjira zake.
Udzadya chipatso cha ntchito yako;
    madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka
    mʼkati mwa nyumba yako;
ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi
    kuzungulira tebulo lako.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa
    amene amaopa Yehova.

Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni
    masiku onse a moyo wako;
uwone zokoma za Yerusalemu,
    ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

Psalm 128

A song of ascents.

Blessed are all who fear the Lord,(A)
    who walk in obedience to him.(B)
You will eat the fruit of your labor;(C)
    blessings and prosperity(D) will be yours.
Your wife will be like a fruitful vine(E)
    within your house;
your children(F) will be like olive shoots(G)
    around your table.
Yes, this will be the blessing(H)
    for the man who fears the Lord.(I)

May the Lord bless you from Zion;(J)
    may you see the prosperity of Jerusalem(K)
    all the days of your life.
May you live to see your children’s children—(L)
    peace be on Israel.(M)