Masalimo 112
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
112 Tamandani Yehova.
Wodala munthu amene amaopa Yehova,
amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko;
mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima;
wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu,
amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
6 Ndithu sadzagwedezeka;
munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika;
mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha;
potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka,
chilungamo chake chimanka mpaka muyaya;
nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima;
adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka.
Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Psalm 112
New International Version
Psalm 112[a]
2 Their children(E) will be mighty in the land;
the generation of the upright will be blessed.
3 Wealth and riches(F) are in their houses,
and their righteousness endures(G) forever.
4 Even in darkness light dawns(H) for the upright,
for those who are gracious and compassionate and righteous.(I)
5 Good will come to those who are generous and lend freely,(J)
who conduct their affairs with justice.
6 Surely the righteous will never be shaken;(K)
they will be remembered(L) forever.
7 They will have no fear of bad news;
their hearts are steadfast,(M) trusting in the Lord.(N)
8 Their hearts are secure, they will have no fear;(O)
in the end they will look in triumph on their foes.(P)
9 They have freely scattered their gifts to the poor,(Q)
their righteousness endures(R) forever;
their horn[c] will be lifted(S) high in honor.
Footnotes
- Psalm 112:1 This psalm is an acrostic poem, the lines of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
- Psalm 112:1 Hebrew Hallelu Yah
- Psalm 112:9 Horn here symbolizes dignity.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.