Add parallel Print Page Options

111 Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse
    mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

Ntchito za Yehova nʼzazikulu;
    onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,
    ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;
    Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;
    amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,
    kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;
    malangizo ake onse ndi odalirika.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,
    ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Iyeyo amawombola anthu ake;
    anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya
    dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;
    onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.
    Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

Psalm 111[a]

Praise the Lord.[b]

I will extol the Lord(A) with all my heart(B)
    in the council(C) of the upright and in the assembly.(D)

Great are the works(E) of the Lord;
    they are pondered by all(F) who delight in them.
Glorious and majestic are his deeds,
    and his righteousness endures(G) forever.
He has caused his wonders to be remembered;
    the Lord is gracious and compassionate.(H)
He provides food(I) for those who fear him;(J)
    he remembers his covenant(K) forever.

He has shown his people the power of his works,(L)
    giving them the lands of other nations.(M)
The works of his hands(N) are faithful and just;
    all his precepts are trustworthy.(O)
They are established for ever(P) and ever,
    enacted in faithfulness and uprightness.
He provided redemption(Q) for his people;
    he ordained his covenant forever—
    holy and awesome(R) is his name.

10 The fear of the Lord(S) is the beginning of wisdom;(T)
    all who follow his precepts have good understanding.(U)
    To him belongs eternal praise.(V)

Footnotes

  1. Psalm 111:1 This psalm is an acrostic poem, the lines of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
  2. Psalm 111:1 Hebrew Hallelu Yah