Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

110 Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,
    “Khala ku dzanja langa lamanja
mpaka nditasandutsa adani ako
    kukhala chopondapo mapazi ako.”

Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;
    udzalamulira pakati pa adani ako.
Ankhondo ako adzakhala odzipereka
    pa tsiku lako la nkhondo.
Atavala chiyero chaulemerero,
    kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,
    udzalandira mame a unyamata wako.

Yehova walumbira
    ndipo sadzasintha maganizo ake:
“Ndiwe wansembe mpaka muyaya
    monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

Ambuye ali kudzanja lako lamanja;
    Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
Adzaweruza anthu a mitundu ina,
    adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;
    choncho adzaweramutsa mutu wake.

Psalm 110

Of David. A psalm.

The Lord says(A) to my lord:[a]

“Sit at my right hand(B)
    until I make your enemies
    a footstool for your feet.”(C)

The Lord will extend your mighty scepter(D) from Zion,(E) saying,
    “Rule(F) in the midst of your enemies!”
Your troops will be willing
    on your day of battle.
Arrayed in holy splendor,(G)
    your young men will come to you
    like dew from the morning’s womb.[b](H)

The Lord has sworn
    and will not change his mind:(I)
“You are a priest forever,(J)
    in the order of Melchizedek.(K)

The Lord is at your right hand[c];(L)
    he will crush kings(M) on the day of his wrath.(N)
He will judge the nations,(O) heaping up the dead(P)
    and crushing the rulers(Q) of the whole earth.
He will drink from a brook along the way,[d]
    and so he will lift his head high.(R)

Footnotes

  1. Psalm 110:1 Or Lord
  2. Psalm 110:3 The meaning of the Hebrew for this sentence is uncertain.
  3. Psalm 110:5 Or My lord is at your right hand, Lord
  4. Psalm 110:7 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.