Maliro 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
2 Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
popondapo mapazi ake.
2 Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
maufumu ndi akalonga ake.
3 Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4 Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 Ambuye ali ngati mdani;
wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6 Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
mfumu ndi wansembe.
7 Ambuye wakana guwa lake la nsembe
ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8 Yehova anatsimikiza kugwetsa
makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
onse anawonongeka pamodzi.
9 Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
aweramitsa mitu yawo pansi.
11 Maso anga atopa ndi kulira,
ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
mʼmisewu ya mu mzinda.
12 Anawo akufunsa amayi awo kuti,
“Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
mʼmanja mwa amayi awo.
13 Ndinganene chiyani za iwe?
Ndingakufanizire ndi chiyani,
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
kuti ndikutonthoze,
iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
kodi ndani angakuchiritse?
14 Masomphenya a aneneri ako
anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
anali achabechabe ndi osocheretsa.
15 Onse oyenda mʼnjira yako
akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
wokongola kotheratu,
chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
tili ndi moyo kuti tilione.”
17 Yehova wachita chimene anakonzeratu;
wakwaniritsa mawu ake,
amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
wakweza mphamvu za adani ako.
18 Mitima ya anthu
ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
misozi yako itsike ngati mtsinje
usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19 Dzuka, fuwula usiku,
pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
mʼmalo opatulika a Ambuye?
21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
mwawapha mopanda chifundo.
22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
Lamentations 2
New International Version
2 [a]How the Lord has covered Daughter Zion
with the cloud of his anger[b]!(A)
He has hurled down the splendor of Israel
from heaven to earth;
he has not remembered his footstool(B)
in the day of his anger.(C)
2 Without pity(D) the Lord has swallowed(E) up
all the dwellings of Jacob;
in his wrath he has torn down
the strongholds(F) of Daughter Judah.
He has brought her kingdom and its princes
down to the ground(G) in dishonor.
3 In fierce anger he has cut off
every horn[c][d](H) of Israel.
He has withdrawn his right hand(I)
at the approach of the enemy.
He has burned in Jacob like a flaming fire
that consumes everything around it.(J)
4 Like an enemy he has strung his bow;(K)
his right hand is ready.
Like a foe he has slain
all who were pleasing to the eye;(L)
he has poured out his wrath(M) like fire(N)
on the tent(O) of Daughter Zion.
5 The Lord is like an enemy;(P)
he has swallowed up Israel.
He has swallowed up all her palaces
and destroyed her strongholds.(Q)
He has multiplied mourning and lamentation(R)
for Daughter Judah.(S)
6 He has laid waste his dwelling like a garden;
he has destroyed(T) his place of meeting.(U)
The Lord has made Zion forget
her appointed festivals and her Sabbaths;(V)
in his fierce anger he has spurned
both king and priest.(W)
7 The Lord has rejected his altar
and abandoned his sanctuary.(X)
He has given the walls of her palaces(Y)
into the hands of the enemy;
they have raised a shout in the house of the Lord
as on the day of an appointed festival.(Z)
8 The Lord determined to tear down
the wall around Daughter Zion.(AA)
He stretched out a measuring line(AB)
and did not withhold his hand from destroying.
He made ramparts(AC) and walls lament;
together they wasted away.(AD)
9 Her gates(AE) have sunk into the ground;
their bars(AF) he has broken and destroyed.
Her king and her princes are exiled(AG) among the nations,
the law(AH) is no more,
and her prophets(AI) no longer find
visions(AJ) from the Lord.
10 The elders of Daughter Zion
sit on the ground in silence;(AK)
they have sprinkled dust(AL) on their heads(AM)
and put on sackcloth.(AN)
The young women of Jerusalem
have bowed their heads to the ground.(AO)
11 My eyes fail from weeping,(AP)
I am in torment within(AQ);
my heart(AR) is poured out(AS) on the ground
because my people are destroyed,(AT)
because children and infants faint(AU)
in the streets of the city.
12 They say to their mothers,
“Where is bread and wine?”(AV)
as they faint like the wounded
in the streets of the city,
as their lives ebb away(AW)
in their mothers’ arms.(AX)
13 What can I say for you?(AY)
With what can I compare you,
Daughter(AZ) Jerusalem?
To what can I liken you,
that I may comfort you,
Virgin Daughter Zion?(BA)
Your wound is as deep as the sea.(BB)
Who can heal you?
14 The visions of your prophets
were false(BC) and worthless;
they did not expose your sin
to ward off your captivity.(BD)
The prophecies they gave you
were false and misleading.(BE)
15 All who pass your way
clap their hands at you;(BF)
they scoff(BG) and shake their heads(BH)
at Daughter Jerusalem:(BI)
“Is this the city that was called
the perfection of beauty,(BJ)
the joy of the whole earth?”(BK)
16 All your enemies open their mouths
wide against you;(BL)
they scoff and gnash their teeth(BM)
and say, “We have swallowed her up.(BN)
This is the day we have waited for;
we have lived to see it.”(BO)
17 The Lord has done what he planned;
he has fulfilled(BP) his word,
which he decreed long ago.(BQ)
He has overthrown you without pity,(BR)
he has let the enemy gloat over you,(BS)
he has exalted the horn[e] of your foes.(BT)
18 The hearts of the people
cry out to the Lord.(BU)
You walls of Daughter Zion,(BV)
let your tears(BW) flow like a river
day and night;(BX)
give yourself no relief,
your eyes no rest.(BY)
19 Arise, cry out in the night,
as the watches of the night begin;
pour out your heart(BZ) like water
in the presence of the Lord.(CA)
Lift up your hands(CB) to him
for the lives of your children,
who faint(CC) from hunger
at every street corner.
20 “Look, Lord, and consider:
Whom have you ever treated like this?
Should women eat their offspring,(CD)
the children they have cared for?(CE)
Should priest and prophet be killed(CF)
in the sanctuary of the Lord?(CG)
Footnotes
- Lamentations 2:1 This chapter is an acrostic poem, the verses of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
- Lamentations 2:1 Or How the Lord in his anger / has treated Daughter Zion with contempt
- Lamentations 2:3 Or off / all the strength; or every king
- Lamentations 2:3 Horn here symbolizes strength.
- Lamentations 2:17 Horn here symbolizes strength.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.