Add parallel Print Page Options

Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
    ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
    kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
    popondapo mapazi ake.

Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
    malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
    maufumu ndi akalonga ake.

Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
    nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
    pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
    umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.

Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
    wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
    pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.

Ambuye ali ngati mdani;
    wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
    ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
    kwa mwana wamkazi wa Yuda.

Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
    wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
    maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
    mfumu ndi wansembe.

Ambuye wakana guwa lake la nsembe
    ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
    kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
    ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.

Yehova anatsimikiza kugwetsa
    makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
    ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
    onse anawonongeka pamodzi.

Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
    wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
    palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
    masomphenya kuchokera kwa Yehova.

10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
    akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
    ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
    aweramitsa mitu yawo pansi.

11 Maso anga atopa ndi kulira,
    ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
    chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
    mʼmisewu ya mu mzinda.

12 Anawo akufunsa amayi awo kuti,
    “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
    mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
    mʼmanja mwa amayi awo.

13 Ndinganene chiyani za iwe?
    Ndingakufanizire ndi chiyani,
    iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
    kuti ndikutonthoze,
    iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
    kodi ndani angakuchiritse?

14 Masomphenya a aneneri ako
    anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
    poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
    anali achabechabe ndi osocheretsa.

15 Onse oyenda mʼnjira yako
    akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
    iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
    wokongola kotheratu,
    chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”

16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
    ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
    tili ndi moyo kuti tilione.”

17 Yehova wachita chimene anakonzeratu;
    wakwaniritsa mawu ake,
    amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
    walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
    wakweza mphamvu za adani ako.

18 Mitima ya anthu
    ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
    misozi yako itsike ngati mtsinje
    usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
    maso ako asaleke kukhetsa misozi.

19 Dzuka, fuwula usiku,
    pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
    pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
    chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
    mʼmisewu yonse ya mu mzinda.

20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
    kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
    amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
    mʼmalo opatulika a Ambuye?

21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
    pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
    aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
    mwawapha mopanda chifundo.

22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
    chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
    palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
    onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.

[a]How the Lord has covered Daughter Zion
    with the cloud of his anger[b]!(A)
He has hurled down the splendor of Israel
    from heaven to earth;
he has not remembered his footstool(B)
    in the day of his anger.(C)

Without pity(D) the Lord has swallowed(E) up
    all the dwellings of Jacob;
in his wrath he has torn down
    the strongholds(F) of Daughter Judah.
He has brought her kingdom and its princes
    down to the ground(G) in dishonor.

In fierce anger he has cut off
    every horn[c][d](H) of Israel.
He has withdrawn his right hand(I)
    at the approach of the enemy.
He has burned in Jacob like a flaming fire
    that consumes everything around it.(J)

Like an enemy he has strung his bow;(K)
    his right hand is ready.
Like a foe he has slain
    all who were pleasing to the eye;(L)
he has poured out his wrath(M) like fire(N)
    on the tent(O) of Daughter Zion.

The Lord is like an enemy;(P)
    he has swallowed up Israel.
He has swallowed up all her palaces
    and destroyed her strongholds.(Q)
He has multiplied mourning and lamentation(R)
    for Daughter Judah.(S)

He has laid waste his dwelling like a garden;
    he has destroyed(T) his place of meeting.(U)
The Lord has made Zion forget
    her appointed festivals and her Sabbaths;(V)
in his fierce anger he has spurned
    both king and priest.(W)

The Lord has rejected his altar
    and abandoned his sanctuary.(X)
He has given the walls of her palaces(Y)
    into the hands of the enemy;
they have raised a shout in the house of the Lord
    as on the day of an appointed festival.(Z)

The Lord determined to tear down
    the wall around Daughter Zion.(AA)
He stretched out a measuring line(AB)
    and did not withhold his hand from destroying.
He made ramparts(AC) and walls lament;
    together they wasted away.(AD)

Her gates(AE) have sunk into the ground;
    their bars(AF) he has broken and destroyed.
Her king and her princes are exiled(AG) among the nations,
    the law(AH) is no more,
and her prophets(AI) no longer find
    visions(AJ) from the Lord.

10 The elders of Daughter Zion
    sit on the ground in silence;(AK)
they have sprinkled dust(AL) on their heads(AM)
    and put on sackcloth.(AN)
The young women of Jerusalem
    have bowed their heads to the ground.(AO)

11 My eyes fail from weeping,(AP)
    I am in torment within(AQ);
my heart(AR) is poured out(AS) on the ground
    because my people are destroyed,(AT)
because children and infants faint(AU)
    in the streets of the city.

12 They say to their mothers,
    “Where is bread and wine?”(AV)
as they faint like the wounded
    in the streets of the city,
as their lives ebb away(AW)
    in their mothers’ arms.(AX)

13 What can I say for you?(AY)
    With what can I compare you,
    Daughter(AZ) Jerusalem?
To what can I liken you,
    that I may comfort you,
    Virgin Daughter Zion?(BA)
Your wound is as deep as the sea.(BB)
    Who can heal you?

14 The visions of your prophets
    were false(BC) and worthless;
they did not expose your sin
    to ward off your captivity.(BD)
The prophecies they gave you
    were false and misleading.(BE)

15 All who pass your way
    clap their hands at you;(BF)
they scoff(BG) and shake their heads(BH)
    at Daughter Jerusalem:(BI)
“Is this the city that was called
    the perfection of beauty,(BJ)
    the joy of the whole earth?”(BK)

16 All your enemies open their mouths
    wide against you;(BL)
they scoff and gnash their teeth(BM)
    and say, “We have swallowed her up.(BN)
This is the day we have waited for;
    we have lived to see it.”(BO)

17 The Lord has done what he planned;
    he has fulfilled(BP) his word,
    which he decreed long ago.(BQ)
He has overthrown you without pity,(BR)
    he has let the enemy gloat over you,(BS)
    he has exalted the horn[e] of your foes.(BT)

18 The hearts of the people
    cry out to the Lord.(BU)
You walls of Daughter Zion,(BV)
    let your tears(BW) flow like a river
    day and night;(BX)
give yourself no relief,
    your eyes no rest.(BY)

19 Arise, cry out in the night,
    as the watches of the night begin;
pour out your heart(BZ) like water
    in the presence of the Lord.(CA)
Lift up your hands(CB) to him
    for the lives of your children,
who faint(CC) from hunger
    at every street corner.

20 “Look, Lord, and consider:
    Whom have you ever treated like this?
Should women eat their offspring,(CD)
    the children they have cared for?(CE)
Should priest and prophet be killed(CF)
    in the sanctuary of the Lord?(CG)

21 “Young and old lie together
    in the dust of the streets;
my young men and young women
    have fallen by the sword.(CH)
You have slain them in the day of your anger;
    you have slaughtered them without pity.(CI)

22 “As you summon to a feast day,
    so you summoned against me terrors(CJ) on every side.
In the day of the Lord’s anger
    no one escaped(CK) or survived;
those I cared for and reared(CL)
    my enemy has destroyed.”

Footnotes

  1. Lamentations 2:1 This chapter is an acrostic poem, the verses of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
  2. Lamentations 2:1 Or How the Lord in his anger / has treated Daughter Zion with contempt
  3. Lamentations 2:3 Or off / all the strength; or every king
  4. Lamentations 2:3 Horn here symbolizes strength.
  5. Lamentations 2:17 Horn here symbolizes strength.