Add parallel Print Page Options

Mphotho ya Kumvera

26 “ ‘Musadzipangire mafano ndipo musayimike chifanizo chosema kapena mwala woti mudzipembedza. Musayike mwala wosema mʼdziko mwanu kuti muziwugwadira. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

“ ‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova.

“ ‘Mukamayenda motsata malangizo anga ndi kumvera mosamalitsa malamulo anga, ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake. Nthaka yanu idzabala zokolola zake, ndipo mitengo ya mʼmunda idzabala zipatso zake. Mudzakhala mukupuntha tirigu mpaka nthawi yothyola mphesa, ndipo mudzakhala mukuthyola mphesa mpaka nthawi yodzala. Mudzadya chakudya chanu mpaka kukhuta ndipo mudzakhala mʼdziko lanu mwamtendere.

“ ‘Ndidzabweretsa mtendere mʼdziko lanu, ndipo muzidzagona popanda wokuopsezani. Ndidzachotsa nyama zakuthengo zoopsa mʼdziko mwanu, ndipo mʼdzikomo simudzakhala nkhondo. Mudzapirikitsa adani anu, ndipo mudzawagonjetsa ndi lupanga pamaso panu. Anthu asanu mwa inu adzapirikitsa anthu 100, ndipo anthu 100 mwa inu adzathamangitsa anthu 10,000, ndipo adani anuwo mudzawagonjetsa ndi lupanga.

“ ‘Ndidzakukumbukirani ndi kukupatsani ana ambiri ndi kukuchulukitsani. Ndidzasunga pangano langa ndi inu. 10 Mudzakhala mukudyabe chakudya chogonera ndipo mudzachotse chakudyacho mʼnkhokwe kuti mupezemo malo woyika chakudya china chatsopano. 11 Ndidzakhala pakati panu, ndipo sindidzayipidwa nanu. 12 Ine ndidzayendayenda pakati panu ndipo ndidzakhala Mulungu wanu. Inu mudzakhala anthu anga. 13 Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti musakhalenso akapolo a Aigupto. Ndinadula mipiringidzo ya goli lanu ndi kukuthandizani kuti muziyenda momasuka.

Chilango Chakusamvera

14 “ ‘Koma mukadzapanda kundimvera ndi kuphwanya malamulo anga onsewa, 15 ndipo ngati mudzanyoza malangizo anga ndi kunyansidwa ndi malamulo anga, ndi kulephera kumvera zonse zimene ndakulamulani, ndi kuswa pangano langa, 16 Ine ndidzakuchitirani izi: ndidzabweretsa zoopsa zadzidzidzi monga chifuwa chachikulu chowondetsa ndiponso malungo amene adzawononga maso ndi kufowoketsa moyo wanu. Mudzangovutika kudzala mbewu zanu chifukwa adani anu adzazidya. 17 Ndidzakufulatirani, kotero kuti adani anu adzakugonjetsani. Odana nanu adzakulamulirani ndipo inu muzidzagothawa popanda wokupirikitsani.

18 “ ‘Ngati simudzandimvera mutaona zonsezi, ndidzakulanganinso mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu. 19 Ndidzathyola mphamvu zanu zimene mukunyadirazo, ndipo ndidzasandutsa mitambo kuti ikhale yowuma ngati chitsulo, ndiponso nthaka yanu kuti ikhale ngati mkuwa. 20 Mphamvu zanu zidzapita pachabe chifukwa nthaka yanu sidzabala kanthu, ngakhale mitengo yake sidzabala zipatso zake.

21 “ ‘Ngati mudzapitirira kutsutsana nane ndi kukana kundimvera, ndidzachulukitsa masautso anu kasanu ndi kawiri molingana ndi machimo anu. 22 Ndidzabweretsa zirombo zolusa pakati panu, ndipo zidzakulandani ana anu ndi kuwononga ngʼombe zanu. Choncho zidzachepetsa chiwerengero chanu kotero kuti mʼnjira mwanu simudzapita anthu.

23 “ ‘Mukadzapanda kutembenukira kwa Ine ngakhale nditakulangani motere, ndi kumachitabe zotsutsana ndi Ine, 24 Ine mwini ndidzalimbana nanu, ndipo ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha machimo anu. 25 Ndipo ndidzabweretsa lupanga pa inu ndi kukulangani chifukwa chophwanya pangano langa. Mukadzasonkhana mʼmizinda yanu, ndidzatumiza miliri pakati panu ndipo ndidzakuperekani mʼmanja mwa adani anu. 26 Ndikadzachepetsa buledi wanu, akazi khumi adzaphika buledi wawo mu uvuni umodzi, ndipo adzakugawirani bulediyo pangʼonopangʼono. Choncho mudzadya koma wosakhuta.

27 “ ‘Mukadzapanda kundimvera ngakhale nditakulangani motere, ndi kumatsutsanabe ndi Ine, 28 pamenepo ndidzalimbana nanu mwaukali, ndipo Ine mwini ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu. 29 Mudzadya ana anu aamuna ndiponso mudzadya ana anu aakazi. 30 Ine ndidzawononga malo anu opembedzera mafano a ku mapiri. Ndidzagwetsa maguwa anu ofukizira lubani, ndipo ndidzawunjika pamodzi mitembo ya mafano anu wopanda moyowo, ndipo ndidzanyansidwa nanu. 31 Ndidzasandutsa mizinda yanu kukhala mabwinja ndi kuwononga malo anu wopatulika. Sindidzakondweranso ndi fungo lokoma la zopereka zanu. 32 Ndidzawononga dziko kotero kuti adani anu mʼmenemo adzadabwa. 33 Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzasolola lupanga langa ndi kukupirikitsani. Dziko lanu lidzawonongedwa, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja. 34 Nthawi imeneyo nthaka idzasangalalira kuyipumitsa kwake nthawi yonse imene idzakhala yosalimidwa, pamene inu mudzakhala muli mʼdziko la adani anu. Pa nthawi imeneyo dziko lidzapumula ndi kukondwerera kulipumuza kwake. 35 Nthawi zonse pamene dzikolo lidzakhala lopanda anthu, nthaka idzapumula. Mpumulo umenewu udzakhala umene nthakayo sinapumulepo pa nthawi zimene inu munkapumula muli mʼdzikomo.

36 “ ‘Kunena za amene adzatsale, ndidzayika mantha mʼmitima mwawo mʼdziko la adani awo kotero kuti adzathawa ngakhale mtswatswa wa tsamba lowuluka ndi mphepo. Adzathawa ngati akuthawa lupanga, ndipo adzagwa pansi ngakhale padzakhale wopanda kuwapirikitsa. 37 Iwo adzaphunthwitsana ngati akuthawa nkhondo, ngakhale padzakhale popanda wowapirikitsa. Choncho simudzatha kuyima pamaso pa adani anu. 38 Mudzatheratu pakati pa mitundu ya anthu. Dziko la adani anu lidzakudyani. 39 Ngakhale iwo amene adzatsale adzatheratu mʼdziko la adani awo chifukwa cha machimo awo ndi machimo a makolo awo.

40 “ ‘Tsono adzawulula machimo awo ndi machimo a makolo awo, kusakhulupirika kwawo ndi mayendedwe awo otsutsana nane, 41 zomwe zinandipangitsa kuwafulatira ndi kuwapereka mʼmanja mwa adani awo. Ndipo mitima yawo yowumayo ikadzadzichepetsa ndi kuvomera kulangidwa chifukwa cha machimo awo, 42 Ine ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo, pangano langa ndi Isake, pangano langa ndi Abrahamu. Ndidzakumbukiranso dzikolo. 43 Pakuti adzasiya dziko lawo lopanda anthu, nthaka idzakondwerera zaka zake zoyipumuza pamene iwo kudzakhala kulibe. Koma adzalangidwa chifukwa cha machimo awo popeza anakana malamulo anga ndipo mitima yawo inkayipidwa nawo malangizo anga. 44 Komabe ngakhale adzachite zonsezi ali mʼdziko la adani awo, Ine sindidzawakana kapena kuyipidwa nawo kwakuti nʼkuwawononga kwathunthu ndi kuthetsa pangano langa ndi iwo. Ine ndine Yehova Mulungu wawo. 45 Koma powachitira chifundo, ndidzakumbukira pangano langa ndi makolo awo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mitundu ina ikuona kuti Ine ndikhale Mulungu wawo. Ine ndine Yehova.’ ”

46 Amenewa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anawayika pakati pa Iye mwini ndi Aisraeli pa Phiri la Sinai kudzera mwa Mose.

Reward for Obedience

26 “‘Do not make idols(A) or set up an image(B) or a sacred stone(C) for yourselves, and do not place a carved stone(D) in your land to bow down before it. I am the Lord your God.

“‘Observe my Sabbaths(E) and have reverence for my sanctuary.(F) I am the Lord.

“‘If you follow my decrees and are careful to obey(G) my commands, I will send you rain(H) in its season,(I) and the ground will yield its crops and the trees their fruit.(J) Your threshing will continue until grape harvest and the grape harvest will continue until planting, and you will eat all the food you want(K) and live in safety in your land.(L)

“‘I will grant peace in the land,(M) and you will lie down(N) and no one will make you afraid.(O) I will remove wild beasts(P) from the land, and the sword will not pass through your country. You will pursue your enemies,(Q) and they will fall by the sword before you. Five(R) of you will chase a hundred, and a hundred of you will chase ten thousand, and your enemies will fall by the sword before you.(S)

“‘I will look on you with favor and make you fruitful and increase your numbers,(T) and I will keep my covenant(U) with you. 10 You will still be eating last year’s harvest when you will have to move it out to make room for the new.(V) 11 I will put my dwelling place[a](W) among you, and I will not abhor you.(X) 12 I will walk(Y) among you and be your God,(Z) and you will be my people.(AA) 13 I am the Lord your God,(AB) who brought you out of Egypt(AC) so that you would no longer be slaves to the Egyptians; I broke the bars of your yoke(AD) and enabled you to walk with heads held high.

Punishment for Disobedience

14 “‘But if you will not listen to me and carry out all these commands,(AE) 15 and if you reject my decrees and abhor my laws(AF) and fail to carry out all my commands and so violate my covenant,(AG) 16 then I will do this to you: I will bring on you sudden terror, wasting diseases and fever(AH) that will destroy your sight and sap your strength.(AI) You will plant seed in vain, because your enemies will eat it.(AJ) 17 I will set my face(AK) against you so that you will be defeated(AL) by your enemies;(AM) those who hate you will rule over you,(AN) and you will flee even when no one is pursuing you.(AO)

18 “‘If after all this you will not listen to me,(AP) I will punish(AQ) you for your sins seven times over.(AR) 19 I will break down your stubborn pride(AS) and make the sky above you like iron and the ground beneath you like bronze.(AT) 20 Your strength will be spent in vain,(AU) because your soil will not yield its crops, nor will the trees of your land yield their fruit.(AV)

21 “‘If you remain hostile(AW) toward me and refuse to listen to me, I will multiply your afflictions seven times over,(AX) as your sins deserve. 22 I will send wild animals(AY) against you, and they will rob you of your children, destroy your cattle and make you so few(AZ) in number that your roads will be deserted.(BA)

23 “‘If in spite of these things you do not accept my correction(BB) but continue to be hostile toward me, 24 I myself will be hostile(BC) toward you and will afflict you for your sins seven times over. 25 And I will bring the sword(BD) on you to avenge(BE) the breaking of the covenant. When you withdraw into your cities, I will send a plague(BF) among you, and you will be given into enemy hands. 26 When I cut off your supply of bread,(BG) ten women will be able to bake your bread in one oven, and they will dole out the bread by weight. You will eat, but you will not be satisfied.

27 “‘If in spite of this you still do not listen to me(BH) but continue to be hostile toward me, 28 then in my anger(BI) I will be hostile(BJ) toward you, and I myself will punish you for your sins seven times over.(BK) 29 You will eat(BL) the flesh of your sons and the flesh of your daughters.(BM) 30 I will destroy your high places,(BN) cut down your incense altars(BO) and pile your dead bodies[b] on the lifeless forms of your idols,(BP) and I will abhor(BQ) you. 31 I will turn your cities into ruins(BR) and lay waste(BS) your sanctuaries,(BT) and I will take no delight in the pleasing aroma of your offerings.(BU) 32 I myself will lay waste the land,(BV) so that your enemies who live there will be appalled.(BW) 33 I will scatter(BX) you among the nations(BY) and will draw out my sword(BZ) and pursue you. Your land will be laid waste,(CA) and your cities will lie in ruins.(CB) 34 Then the land will enjoy its sabbath years all the time that it lies desolate(CC) and you are in the country of your enemies;(CD) then the land will rest and enjoy its sabbaths. 35 All the time that it lies desolate, the land will have the rest(CE) it did not have during the sabbaths you lived in it.

36 “‘As for those of you who are left, I will make their hearts so fearful in the lands of their enemies that the sound of a windblown leaf(CF) will put them to flight.(CG) They will run as though fleeing from the sword, and they will fall, even though no one is pursuing them.(CH) 37 They will stumble over one another(CI) as though fleeing from the sword, even though no one is pursuing them. So you will not be able to stand before your enemies.(CJ) 38 You will perish(CK) among the nations; the land of your enemies will devour you.(CL) 39 Those of you who are left will waste away in the lands of their enemies because of their sins; also because of their ancestors’(CM) sins they will waste away.(CN)

40 “‘But if they will confess(CO) their sins(CP) and the sins of their ancestors(CQ)—their unfaithfulness and their hostility toward me, 41 which made me hostile(CR) toward them so that I sent them into the land of their enemies—then when their uncircumcised hearts(CS) are humbled(CT) and they pay(CU) for their sin, 42 I will remember my covenant with Jacob(CV) and my covenant with Isaac(CW) and my covenant with Abraham,(CX) and I will remember the land. 43 For the land will be deserted(CY) by them and will enjoy its sabbaths while it lies desolate without them. They will pay for their sins because they rejected(CZ) my laws and abhorred my decrees.(DA) 44 Yet in spite of this, when they are in the land of their enemies,(DB) I will not reject them or abhor(DC) them so as to destroy them completely,(DD) breaking my covenant(DE) with them. I am the Lord their God. 45 But for their sake I will remember(DF) the covenant with their ancestors whom I brought out of Egypt(DG) in the sight of the nations to be their God. I am the Lord.’”

46 These are the decrees, the laws and the regulations that the Lord established at Mount Sinai(DH) between himself and the Israelites through Moses.(DI)

Footnotes

  1. Leviticus 26:11 Or my tabernacle
  2. Leviticus 26:30 Or your funeral offerings