Add parallel Print Page Options

Tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo

16 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose. Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.

“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi. Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.

“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake. Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele. Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo. 10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.

11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja. 12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani. 13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe. 14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.

15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho. 16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo. 17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.

18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe. 19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.

20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe. 21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu. 22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.

23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko. 24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu. 25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.

26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa. 27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe. 28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.

29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu, 30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova. 31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya. 32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika. 33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.

34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.”

Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.

The Day of Atonement(A)

16 The Lord spoke to Moses after the death of the two sons of Aaron who died when they approached the Lord.(B) The Lord said to Moses: “Tell your brother Aaron that he is not to come whenever he chooses(C) into the Most Holy Place(D) behind the curtain(E) in front of the atonement cover(F) on the ark, or else he will die. For I will appear(G) in the cloud(H) over the atonement cover.

“This is how Aaron is to enter the Most Holy Place:(I) He must first bring a young bull(J) for a sin offering[a] and a ram for a burnt offering.(K) He is to put on the sacred linen tunic,(L) with linen undergarments next to his body; he is to tie the linen sash around him and put on the linen turban.(M) These are sacred garments;(N) so he must bathe himself with water(O) before he puts them on.(P) From the Israelite community(Q) he is to take two male goats(R) for a sin offering and a ram for a burnt offering.

“Aaron is to offer the bull for his own sin offering to make atonement for himself and his household.(S) Then he is to take the two goats and present them before the Lord at the entrance to the tent of meeting. He is to cast lots(T) for the two goats—one lot for the Lord and the other for the scapegoat.[b](U) Aaron shall bring the goat whose lot falls to the Lord and sacrifice it for a sin offering. 10 But the goat chosen by lot as the scapegoat shall be presented alive before the Lord to be used for making atonement(V) by sending it into the wilderness as a scapegoat.

11 “Aaron shall bring the bull for his own sin offering to make atonement for himself and his household,(W) and he is to slaughter the bull for his own sin offering. 12 He is to take a censer full of burning coals(X) from the altar before the Lord and two handfuls of finely ground fragrant incense(Y) and take them behind the curtain. 13 He is to put the incense on the fire before the Lord, and the smoke of the incense will conceal the atonement cover(Z) above the tablets of the covenant law, so that he will not die.(AA) 14 He is to take some of the bull’s blood(AB) and with his finger sprinkle it on the front of the atonement cover; then he shall sprinkle some of it with his finger seven times before the atonement cover.(AC)

15 “He shall then slaughter the goat for the sin offering for the people(AD) and take its blood behind the curtain(AE) and do with it as he did with the bull’s blood: He shall sprinkle(AF) it on the atonement cover and in front of it. 16 In this way he will make atonement(AG) for the Most Holy Place(AH) because of the uncleanness and rebellion of the Israelites, whatever their sins have been. He is to do the same for the tent of meeting,(AI) which is among them in the midst of their uncleanness. 17 No one is to be in the tent of meeting from the time Aaron goes in to make atonement in the Most Holy Place until he comes out, having made atonement for himself, his household and the whole community of Israel.

18 “Then he shall come out to the altar(AJ) that is before the Lord and make atonement for it. He shall take some of the bull’s blood and some of the goat’s blood and put it on all the horns of the altar.(AK) 19 He shall sprinkle some of the blood on it with his finger seven times to cleanse it and to consecrate it from the uncleanness of the Israelites.(AL)

20 “When Aaron has finished making atonement for the Most Holy Place, the tent of meeting and the altar, he shall bring forward the live goat.(AM) 21 He is to lay both hands on the head of the live goat(AN) and confess(AO) over it all the wickedness and rebellion of the Israelites—all their sins—and put them on the goat’s head. He shall send the goat away into the wilderness in the care of someone appointed for the task. 22 The goat will carry on itself all their sins(AP) to a remote place; and the man shall release it in the wilderness.

23 “Then Aaron is to go into the tent of meeting and take off the linen garments(AQ) he put on before he entered the Most Holy Place, and he is to leave them there.(AR) 24 He shall bathe himself with water in the sanctuary area(AS) and put on his regular garments.(AT) Then he shall come out and sacrifice the burnt offering for himself and the burnt offering for the people,(AU) to make atonement for himself and for the people.(AV) 25 He shall also burn the fat of the sin offering on the altar.

26 “The man who releases the goat as a scapegoat(AW) must wash his clothes(AX) and bathe himself with water;(AY) afterward he may come into the camp. 27 The bull and the goat for the sin offerings, whose blood was brought into the Most Holy Place to make atonement, must be taken outside the camp;(AZ) their hides, flesh and intestines are to be burned up. 28 The man who burns them must wash his clothes and bathe himself with water; afterward he may come into the camp.(BA)

29 “This is to be a lasting ordinance(BB) for you: On the tenth day of the seventh month(BC) you must deny yourselves[c](BD) and not do any work(BE)—whether native-born(BF) or a foreigner residing among you— 30 because on this day atonement will be made(BG) for you, to cleanse you. Then, before the Lord, you will be clean from all your sins.(BH) 31 It is a day of sabbath rest, and you must deny yourselves;(BI) it is a lasting ordinance.(BJ) 32 The priest who is anointed and ordained(BK) to succeed his father as high priest is to make atonement. He is to put on the sacred linen garments(BL) 33 and make atonement for the Most Holy Place, for the tent of meeting and the altar, and for the priests and all the members of the community.(BM)

34 “This is to be a lasting ordinance(BN) for you: Atonement is to be made once a year(BO) for all the sins of the Israelites.”

And it was done, as the Lord commanded Moses.

Footnotes

  1. Leviticus 16:3 Or purification offering; here and throughout this chapter
  2. Leviticus 16:8 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain; also in verses 10 and 26.
  3. Leviticus 16:29 Or must fast; also in verse 31