Yobu 5
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
5 “Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe?
Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Mkwiyo umapha chitsiru,
ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu,
koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe;
amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Anthu anjala amamudyera zokolola zake,
amamutengera ndi za pa minga pomwe,
ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Pakuti masautso satuluka mʼfumbi,
ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 Komatu munthu amabadwira kuti azunzike
monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 “Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu;
ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi,
ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Iye amakweza anthu wamba,
ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera,
kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,
ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana;
nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo;
amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo,
ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula;
nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo;
Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi,
mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa,
ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira,
ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala,
ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako,
ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa;
udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri,
ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Udzafika ku manda utakalamba,
monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona,
choncho uzimvere ndi kuzitsata.”
Job 5
English Standard Version
5 “Call now; is there anyone who will answer you?
To which of (A)the holy ones will you turn?
2 Surely vexation kills the fool,
and jealousy slays the simple.
3 (B)I have seen the fool taking root,
but suddenly I cursed his dwelling.
4 His children are (C)far from safety;
they are crushed in (D)the gate,
and there is no one to deliver them.
5 The hungry eat his harvest,
and he takes it even out of thorns,[a]
and the thirsty pant[b] after his[c] wealth.
6 For affliction does not come from the dust,
nor does trouble sprout from the ground,
7 but man is (E)born to trouble
as the sparks fly upward.
8 “As for me, I would seek God,
and to God would I commit my cause,
9 who (F)does great things and (G)unsearchable,
(H)marvelous things without number:
10 he gives (I)rain on the earth
and sends waters on the fields;
11 he (J)sets on high those who are lowly,
and those who mourn are lifted to safety.
12 He (K)frustrates the devices of the crafty,
so that their hands achieve no success.
13 He (L)catches the wise in their own craftiness,
and the schemes of the wily are brought to a quick end.
14 They meet with darkness in the daytime
and (M)grope at noonday as in the night.
15 But he (N)saves the needy from the sword of their mouth
and from the hand of the mighty.
16 So the poor have hope,
and (O)injustice shuts her mouth.
17 “Behold, (P)blessed is the one whom God reproves;
therefore (Q)despise not the discipline of the (R)Almighty.
18 For he wounds, but he (S)binds up;
he (T)shatters, but his hands heal.
19 He will (U)deliver you from six troubles;
in seven no (V)evil[d] shall touch you.
20 (W)In famine he will redeem you from death,
and in war from the power of the sword.
21 You shall be (X)hidden from the lash of the tongue,
and shall not fear destruction when it comes.
22 At destruction and famine you shall laugh,
and shall not fear (Y)the beasts of the earth.
23 For you shall be in league with the stones of the field,
and the beasts of the field shall be at peace with you.
24 You shall know that your (Z)tent is at peace,
and you shall inspect your fold and miss nothing.
25 You shall know also that your (AA)offspring shall be many,
and your descendants as (AB)the grass of the earth.
26 You shall come to your grave in (AC)ripe old age,
like a sheaf gathered up in its season.
27 Behold, this we have (AD)searched out; it is true.
Hear, and know it for your good.”[e]
Job 5
King James Version
5 Call now, if there be any that will answer thee; and to which of the saints wilt thou turn?
2 For wrath killeth the foolish man, and envy slayeth the silly one.
3 I have seen the foolish taking root: but suddenly I cursed his habitation.
4 His children are far from safety, and they are crushed in the gate, neither is there any to deliver them.
5 Whose harvest the hungry eateth up, and taketh it even out of the thorns, and the robber swalloweth up their substance.
6 Although affliction cometh not forth of the dust, neither doth trouble spring out of the ground;
7 Yet man is born unto trouble, as the sparks fly upward.
8 I would seek unto God, and unto God would I commit my cause:
9 Which doeth great things and unsearchable; marvellous things without number:
10 Who giveth rain upon the earth, and sendeth waters upon the fields:
11 To set up on high those that be low; that those which mourn may be exalted to safety.
12 He disappointeth the devices of the crafty, so that their hands cannot perform their enterprise.
13 He taketh the wise in their own craftiness: and the counsel of the froward is carried headlong.
14 They meet with darkness in the day time, and grope in the noonday as in the night.
15 But he saveth the poor from the sword, from their mouth, and from the hand of the mighty.
16 So the poor hath hope, and iniquity stoppeth her mouth.
17 Behold, happy is the man whom God correcteth: therefore despise not thou the chastening of the Almighty:
18 For he maketh sore, and bindeth up: he woundeth, and his hands make whole.
19 He shall deliver thee in six troubles: yea, in seven there shall no evil touch thee.
20 In famine he shall redeem thee from death: and in war from the power of the sword.
21 Thou shalt be hid from the scourge of the tongue: neither shalt thou be afraid of destruction when it cometh.
22 At destruction and famine thou shalt laugh: neither shalt thou be afraid of the beasts of the earth.
23 For thou shalt be in league with the stones of the field: and the beasts of the field shall be at peace with thee.
24 And thou shalt know that thy tabernacle shall be in peace; and thou shalt visit thy habitation, and shalt not sin.
25 Thou shalt know also that thy seed shall be great, and thine offspring as the grass of the earth.
26 Thou shalt come to thy grave in a full age, like as a shock of corn cometh in in his season.
27 Lo this, we have searched it, so it is; hear it, and know thou it for thy good.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The ESV® Bible (The Holy Bible, English Standard Version®), © 2001 by Crossway, a publishing ministry of Good News Publishers. ESV Text Edition: 2025.
