Yesaya 64
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
64 Inu Yehova, bwanji mukanangongʼamba mlengalenga ndi kutsika pansi,
kuti mapiri agwedezeke pamaso panu!
2 Monga momwe moto umatenthera tchire
ndiponso kuwiritsa madzi,
tsikani kuti adani anu adziwe dzina lanu,
ndiponso kuti mitundu ya anthu injenjemere pamaso panu.
3 Pakuti nthawi ina pamene munatsika munachita zinthu zoopsa zimene sitinaziyembekezere,
ndipo mapiri anagwedezeka pamaso panu.
4 Chikhalire palibe ndi mmodzi yemwe anamvapo
kapena kuona
Mulungu wina wonga Inu,
amene amachitira zinthu zotere amene amadikira pa Iye.
5 Inu mumabwera kudzathandiza onse amene amakondwera pochita zolungama,
amene amakumbukira njira zanu.
Koma Inu munakwiya,
ife tinapitiriza kuchimwa.
Kodi nanga tingapulumutsidwe bwanji?
6 Tonsefe takhala ngati anthu amene ndi odetsedwa,
ndipo ntchito zathu zili ngati sanza za msambo;
tonse tafota ngati tsamba,
ndipo machimo athu akutiwuluzira kutali ngati mphepo.
7 Palibe amene amapemphera kwa Inu
kutekeseka kuti apemphe chithandizo kwa Inu;
pakuti mwatifulatira
ndi kutisiya chifukwa cha machimo athu.
8 Komabe, Inu Yehova ndinu Atate athu.
Ife ndife chowumba, Inu ndinu wowumba;
ife tonse ndi ntchito ya manja anu.
9 Inu Yehova, musatikwiyire kopitirira muyeso
musakumbukire machimo athu mpaka muyaya.
Chonde, mutiganizire, ife tikupempha,
pakuti tonsefe ndi anthu anu.
10 Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu;
ngakhaletu Ziyoni wasanduka chipululu, Yerusalemu ndi wamasiye.
11 Nyumba yanu yopatulika ndi yaulemu, kumene makolo athu ankakutamandani,
yatenthedwa ndi moto
ndipo malo onse amene tinkawakonda asanduka bwinja.
12 Inu Yehova, zonse zachitikazi, kodi mungokhala osatithandiza?
Kodi mudzapitirizabe kukhala chete ndi kutilangabe mopitirira muyeso?
Isaiah 64
New King James Version
A Prayer for Help
64 Oh, that You would [a]rend the heavens!
That You would come down!
That the mountains might shake at Your (A)presence—
2 As fire burns brushwood,
As fire causes water to boil—
To make Your name known to Your adversaries,
That the nations may tremble at Your presence!
3 When (B)You did awesome things for which we did not look,
You came down,
The mountains shook at Your presence.
4 For since the beginning of the world
(C)Men have not heard nor perceived by the ear,
Nor has the eye seen any God besides You,
Who acts for the one who waits for Him.
5 You meet him who rejoices and does righteousness,
Who remembers You in Your ways.
You are indeed angry, for we have sinned—
(D)In these ways we continue;
And we need to be saved.
6 But we are all like an unclean thing,
And all (E)our righteousnesses are like [b]filthy rags;
We all (F)fade as a leaf,
And our iniquities, like the wind,
Have taken us away.
7 And there is no one who calls on Your name,
Who stirs himself up to take hold of You;
For You have hidden Your face from us,
And have [c]consumed us because of our iniquities.
8 But now, O Lord,
You are our Father;
We are the clay, and You our (G)potter;
And all we are the work of Your hand.
9 Do not be furious, O Lord,
Nor remember iniquity forever;
Indeed, please look—we all are Your people!
10 Your holy cities are a wilderness,
Zion is a wilderness,
Jerusalem a desolation.
11 Our holy and beautiful [d]temple,
Where our fathers praised You,
Is burned up with fire;
And all (H)our pleasant things [e]are laid waste.
12 (I)Will You restrain Yourself because of these things, O Lord?
(J)Will You [f]hold Your peace, and afflict us very severely?
Footnotes
- Isaiah 64:1 tear open
- Isaiah 64:6 Lit. a filthy garment
- Isaiah 64:7 Lit. caused us to melt
- Isaiah 64:11 Lit. house
- Isaiah 64:11 have become a ruin
- Isaiah 64:12 keep silent
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.
